Add parallel Print Page Options

Zipatso Zoyamba ndi Chakhumi

26 Mukalowa ndi kukhazikika mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa chanu, mutengeko zina mwa zipatso zoyamba pa zonse zimene mudzakola mʼnthaka ya dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ndi kuziyika mʼdengu. Mukatero mupite kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzakhazikitsako dzina lake ndipo mudzamuwuze wansembe amene ali pa ntchito pa nthawiyo kuti, “Ndikunenetsa lero kwa Yehova Mulungu wanu kuti ndabwera ku dziko limene Yehova analumbirira makolo athu kuti adzatipatsa ife.” Wansembe adzatenga dengulo mʼmanja mwanu ndi kuliyika pansi patsogolo pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu. Ndipo mudzanenetsa pamaso pa Yehova Mulungu wanu kuti, “Abambo anga anali Mwaramu woyendayenda, anapita ku Igupto ndi anthu ochepa nakhala kumeneko. Pambuyo pake anakhala mtundu waukulu, wamphamvu ndi wochuluka. Koma Aigupto anatisautsa natizunza, kumatigwiritsa ntchito yakalavulagaga. Kenaka tinafuwulira Yehova, Mulungu wa makolo athu ndipo Yehova anamva mawu athu ndi kuona kusauka, kuvutika ndi kuponderezedwa kwathu. Kotero Yehova anatitulutsa ku Igupto ndi dzanja lake lamphamvu ndi mkono wotambasuka ndi zoopsa zazikulu ndi zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa. Iye anatibweretsa ku malo ano natipatsa dziko loyenda mkaka ndi uchi lino. 10 Ndipo tsopano ndikubweretsa zipatso zoyamba zimene inu Yehova mwandipatsa.” Ikani dengulo pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi kuwerama mopereka ulemu pamaso pake. 11 Ndipo inu ndi Alevi pamodzi ndi alendo okhala pakati panu mudzakondwera mʼzinthu zonse zabwino zimene Yehova Mulungu wanu wakupatsani, inu ndi a pa banja panu.

12 Mukatha kupatula chakhumi pa zonse zimene mwakolola mʼchaka chachitatu chimene ndi chaka chakhumi, muzichipereka kwa wansembe, mlendo, ana ndi akazi amasiye, kuti pamenepo adye mʼmizinda yanu nakhuta. 13 Kenaka munene kwa Yehova Mulungu wanu kuti “Ndatulutsamo mʼnyumba mwanga gawo lopatulika ndipo ndalipereka kwa Mlevi, mlendo, ana ndi akazi amasiye, monga mwa zonse zimene munalamula. Sindinapatuke pa zimene munalamula kapena kuyiwala ndi chimodzi chomwe. 14 Sindinadye kalikonse ka gawo lopatulika pamene ndimalira maliro kapena kuchotsapo kalikonse ka gawo lopatulika pamene ndinali wodetsedwa, kapena kuperekako nsembe kwa akufa kalikonse ka gawoli. Ine ndamvera Yehova Mulungu wanga, ndachita chilichonse chimene inu munandilamula. 15 Yangʼanani pa dziko kuchokera kumwamba, ku malo anu wopatulika, ndi kudalitsa anthu anu Aisraeli ndi dziko loyenda mkaka ndi uchi limene mwatipatsa ife monga momwe munalonjezera pa malumbiro anu kwa makolo athu.”

Tsatirani Malamulo a Yehova

16 Yehova Mulungu wanu akukulamulani lero lino kuti mutsate malangizo ndi malamulo ake ndipo muwasunge mosamalitsa ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse. 17 Mwanena motsimikiza lero lino kuti Yehova ndiye Mulungu wanu ndi kuti mudzayenda mʼnjira zake, kusunga malangizo, malamulo ndi zonse akukulamulani ndi kutinso mudzamumvera. 18 Ndipo Yehova wanenetsa lero lino kuti inu ndinu anthu ake, chuma chake chamtengowapatali monga momwe analonjezera, ndipo mukuyenera kusunga malamulo ake onse. 19 Iye wanenetsa kuti adzakuyikani kukhala oyamikika, otchuka ndi olemekezeka koposa mitundu yonse imene anayilenga. Komanso mudzakhala anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu monga momwe analonjezera.

Firstfruits and Tithes

26 When you have entered the land the Lord your God is giving you as an inheritance and have taken possession of it and settled in it, take some of the firstfruits(A) of all that you produce from the soil of the land the Lord your God is giving you and put them in a basket. Then go to the place the Lord your God will choose as a dwelling for his Name(B) and say to the priest in office at the time, “I declare today to the Lord your God that I have come to the land the Lord swore to our ancestors to give us.” The priest shall take the basket from your hands and set it down in front of the altar of the Lord your God. Then you shall declare before the Lord your God: “My father was a wandering(C) Aramean,(D) and he went down into Egypt with a few people(E) and lived there and became a great nation,(F) powerful and numerous. But the Egyptians mistreated us and made us suffer,(G) subjecting us to harsh labor.(H) Then we cried out to the Lord, the God of our ancestors, and the Lord heard our voice(I) and saw(J) our misery,(K) toil and oppression.(L) So the Lord brought us out of Egypt(M) with a mighty hand and an outstretched arm,(N) with great terror and with signs and wonders.(O) He brought us to this place and gave us this land, a land flowing with milk and honey;(P) 10 and now I bring the firstfruits of the soil that you, Lord, have given me.(Q)” Place the basket before the Lord your God and bow down before him. 11 Then you and the Levites(R) and the foreigners residing among you shall rejoice(S) in all the good things the Lord your God has given to you and your household.

12 When you have finished setting aside a tenth(T) of all your produce in the third year, the year of the tithe,(U) you shall give it to the Levite, the foreigner, the fatherless and the widow, so that they may eat in your towns and be satisfied. 13 Then say to the Lord your God: “I have removed from my house the sacred portion and have given it to the Levite, the foreigner, the fatherless and the widow, according to all you commanded. I have not turned aside from your commands nor have I forgotten any of them.(V) 14 I have not eaten any of the sacred portion while I was in mourning, nor have I removed any of it while I was unclean,(W) nor have I offered any of it to the dead. I have obeyed the Lord my God; I have done everything you commanded me. 15 Look down from heaven,(X) your holy dwelling place, and bless(Y) your people Israel and the land you have given us as you promised on oath to our ancestors, a land flowing with milk and honey.”

Follow the Lord’s Commands

16 The Lord your God commands you this day to follow these decrees and laws; carefully observe them with all your heart and with all your soul.(Z) 17 You have declared this day that the Lord is your God and that you will walk in obedience to him, that you will keep his decrees, commands and laws—that you will listen to him.(AA) 18 And the Lord has declared this day that you are his people, his treasured possession(AB) as he promised, and that you are to keep all his commands. 19 He has declared that he will set you in praise,(AC) fame and honor high above all the nations(AD) he has made and that you will be a people holy(AE) to the Lord your God, as he promised.