Add parallel Print Page Options

22 Ngati uwona ngʼombe kapena nkhosa ya mʼbale wako ikusochera, usayilekerere koma uyesetse kuyibwezera kwa iye. Ngati mʼbale wakoyo sakhala pafupi kapena sukudziwa kuti ndi yandani, uyitengere ku nyumba kwako ndi kuyisamala mpaka mwini wake atayilondola ndipo umubwezere. Uzitero ndithu ngati upeza bulu kapena mkanjo kapena chilichonse chimene chatayika. Osachilekerera.

Ngati wapeza bulu kapena ngʼombe ya mʼbale wako itagwa panjira, usayilekerere. Ithandize kuti idzuke.

Akazi asavale zovala za amuna, kapena mwamuna kuvala zovala za akazi, pakuti Yehova Mulungu wanu amanyansidwa ndi aliyense wochita izi.

Ukapeza chisa cha mbalame mʼmphepete mwa msewu, kaya ndi mu mtengo kapena pansi, mbalame yayikazi itafungatira ana kapena mazira, usatenge mbalameyo pamodzi ndi ana ake omwe. Anawo mukhoza kutenga koma onetsetsani kuti mayi wawo mwamutaya kuti apite, kuti zinthu zizikuyenderani bwino ndiponso kuti mukhale ndi moyo wautali.

Mukamanga nyumba yatsopano, mutchingire khonde lake la pa denga kuti inu musapezeke ndi mlandu wopha munthu ngati wina agwa kuchokera pa khonde la pa dengalo.

Musadzale mbewu zamitundu iwiri mʼmunda wanu wa mpesa, ngati mutero, si mbewu zanu zokha zimene zidzakhale zodetsedwa, komanso zipatso za mʼmunda wamphesawo.

10 Musatipule pogwiritsa ntchito ngʼombe ndi bulu pa goli limodzi.

11 Musamavale chovala chopangidwa mophatikiza ubweya ndi thonje.

12 Muzipanga mphonje mʼngodya za mkanjo umene mumavala.

Malamulo a Ukwati

13 Ngati munthu akwatira mkazi, ndipo atagona naye nʼkusamufunanso 14 namunyoza ndi kumuyipitsira dzina nʼkumati, “Ine ndinakwatira mkazi uyu, koma pamene ndinakhala naye, sindinachione chizindikiro cha unamwali wake,” 15 zikatero abambo ndi amayi ake ayenera kubweretsa chitsimikizo chakuti anali namwali kwa akuluakulu a mzinda ku chipata. 16 Abambo ake a mtsikanayo adzanene kwa akuluakuluwo kuti, “Ine ndinamupatsa munthu uyu mwana wanga wamkazi kuti amukwatire, koma sakumufunanso. 17 Tsopano wamunyoza ndipo wanena kuti, ‘Ine sindinapeze kuti mwana wanu wamkaziyu ndi namwali.’ Koma tsopano onani chitsimikizo ichi cha unamwali wa mwana wanga wamkazi.” Kenaka makolo a mtsikanayo adzaonetse kansalu kwa akuluakulu aja, 18 ndipo akuluakuluwo adzamugwire munthuyo namupatsa chilango. 19 Iwo adzamulipitse ndalama zasiliva zokwana 100 nazipereka kwa abambo a mtsikana, chifukwa munthu uyu wayipitsa dzina la mtsikana wa Chiisraeli. Ayenera kukhalabe mkazi wake ndipo asadzamuleke moyo wake wonse.

20 Koma ngati zomunenerazo ndi zoona, ndipo kuti chitsimikizo cha unamwali wa mtsikanayo sichinapezeke, 21 iyeyu ayenera kumutengera pa khomo pa abambo ake pamene anthu a mu mzinda wake akamuphere ndi miyala. Iyeyo wachita chinthu chochititsa manyazi mu Israeli pochita chiwerewere akanali pa khomo pa abambo ake. Muyenera kuchotsa zoyipa pakati panu.

22 Ngati munthu apezeka akugona ndi mkazi wa mwini wake, ayenera kuphedwa munthuyo pamodzi ndi mkazi yemwe wagona nayeyo. Muyenera kuchotsa zoyipa mu Israeli.

23 Ngati munthu mu mzinda akumana ndi mkazi yemwe anachita kale chinkhoswe nagona naye, 24 muwatengere awiriwo ku chipata cha mzinda ndi kuwapha ndi miyala. Aphedwe chifukwa mtsikanayo anali pafupi ndi anthu ndipo sanakuwe kuti ena amuthandize ndipo mwamunayo chifukwa anayipitsa mkazi wa mwini. Muyenera kuchotsa choyipa pakati panu.

25 Koma ngati munthu akumana ndi mkazi kutchire yemwe anachita kale chinkhoswe namugwiririra, mwamuna yekhayo ndiye woyenera kuphedwa. 26 Mtsikanayo musamuchite chilichonse, palibe tchimo limene wachita loti ayenera kuphedwa. Mlandu uwu ufanana ndi wa munthu amene alimbana ndi kupha mnzake woyandikana naye, 27 pakuti mwamunayo anamupeza mtsikanayo kutchire, ndipo ngakhale mtsikana wachinkhosweyo anakuwa, panalibe anamulanditsa.

28 Ngati munthu apezana ndi namwali woti sanachite chinkhoswe, namugwiririra, munthuyo nʼkupezeka, 29 ayenera kuwalipira abambo ake a namwaliyo ndalama za siliva makumi asanu. Iye ayenera kumukwatira mkaziyo chifukwa wamuyipitsa, ndipo sadzamulekanso moyo wake wonse.

30 Munthu asakwatire mkazi wa abambo ake pakuti ayenera kuchitira ulemu pogona pa abambo ake.

22 If you see your fellow Israelite’s ox or sheep straying, do not ignore it but be sure to take it back to its owner.(A) If they do not live near you or if you do not know who owns it, take it home with you and keep it until they come looking for it. Then give it back. Do the same if you find their donkey or cloak or anything else they have lost. Do not ignore it.

If you see your fellow Israelite’s donkey(B) or ox fallen on the road, do not ignore it. Help the owner get it to its feet.(C)

A woman must not wear men’s clothing, nor a man wear women’s clothing, for the Lord your God detests anyone who does this.

If you come across a bird’s nest beside the road, either in a tree or on the ground, and the mother is sitting on the young or on the eggs, do not take the mother with the young.(D) You may take the young, but be sure to let the mother go,(E) so that it may go well with you and you may have a long life.(F)

When you build a new house, make a parapet around your roof so that you may not bring the guilt of bloodshed on your house if someone falls from the roof.(G)

Do not plant two kinds of seed in your vineyard;(H) if you do, not only the crops you plant but also the fruit of the vineyard will be defiled.[a]

10 Do not plow with an ox and a donkey yoked together.(I)

11 Do not wear clothes of wool and linen woven together.(J)

12 Make tassels on the four corners of the cloak you wear.(K)

Marriage Violations

13 If a man takes a wife and, after sleeping with her(L), dislikes her 14 and slanders her and gives her a bad name, saying, “I married this woman, but when I approached her, I did not find proof of her virginity,” 15 then the young woman’s father and mother shall bring to the town elders at the gate(M) proof that she was a virgin. 16 Her father will say to the elders, “I gave my daughter in marriage to this man, but he dislikes her. 17 Now he has slandered her and said, ‘I did not find your daughter to be a virgin.’ But here is the proof of my daughter’s virginity.” Then her parents shall display the cloth before the elders of the town, 18 and the elders(N) shall take the man and punish him. 19 They shall fine him a hundred shekels[b] of silver and give them to the young woman’s father, because this man has given an Israelite virgin a bad name. She shall continue to be his wife; he must not divorce her as long as he lives.

20 If, however, the charge is true(O) and no proof of the young woman’s virginity can be found, 21 she shall be brought to the door of her father’s house and there the men of her town shall stone her to death. She has done an outrageous thing(P) in Israel by being promiscuous while still in her father’s house. You must purge the evil from among you.

22 If a man is found sleeping with another man’s wife, both the man who slept(Q) with her and the woman must die.(R) You must purge the evil from Israel.

23 If a man happens to meet in a town a virgin pledged to be married and he sleeps with her, 24 you shall take both of them to the gate of that town and stone them to death—the young woman because she was in a town and did not scream for help, and the man because he violated another man’s wife. You must purge the evil from among you.(S)

25 But if out in the country a man happens to meet a young woman pledged to be married and rapes her, only the man who has done this shall die. 26 Do nothing to the woman; she has committed no sin deserving death. This case is like that of someone who attacks and murders a neighbor, 27 for the man found the young woman out in the country, and though the betrothed woman screamed,(T) there was no one to rescue her.

28 If a man happens to meet a virgin who is not pledged to be married and rapes her and they are discovered,(U) 29 he shall pay her father fifty shekels[c] of silver. He must marry the young woman, for he has violated her. He can never divorce her as long as he lives.

30 A man is not to marry his father’s wife; he must not dishonor his father’s bed.[d](V)

Footnotes

  1. Deuteronomy 22:9 Or be forfeited to the sanctuary
  2. Deuteronomy 22:19 That is, about 2 1/2 pounds or about 1.2 kilograms
  3. Deuteronomy 22:29 That is, about 1 1/4 pounds or about 575 grams
  4. Deuteronomy 22:30 In Hebrew texts this verse (22:30) is numbered 23:1.