Add parallel Print Page Options

Nsembe Yopepesera Munthu Akaphedwa Mosadziwika Bwino

21 Ngati munthu apezeka ataphedwa mʼmunda mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kukhala lanu koma inu osadziwa amene wamupha, akuluakulu anu ndi oweruza adzapite ndi kuyeza kutalikirana kuchokera pamene pali mtembowo ndi mizinda yoyandikira. Kenaka akuluakulu a mzinda wapafupi kwambiri ndi mtembowo adzatenge ngʼombe imene sinagwirepo ntchito kapena kuvalapo goli ndi kuyikusira ku chigwa chimene sichinalimidwepo ndiponso kumene kuli mtsinje woyenda. Ku chigwa kumeneko ayenera kukayithyola khosi ngʼombeyo. Ansembe, ana a Aaroni, adzapite patsogolo pangʼono, popeza ndiwo amene Yehova Mulungu wanu anawasankha kuti azitumikira, kupereka mdalitso mʼdzina la Yehova ndi kugamula milandu yonse yamikangano ndi yovulazana. Kenaka akuluakulu a mzinda wapafupi kwambiri ndi mtembowo adzasamba mʼmanja pamwamba pa ngʼombe yothyoledwa khosi ija, nadzatsimikiza kuti, “Manja athu sanakhetse magazi awa ndipo sitinaonerere kuphedwako. Yehova, landirani nsembe yopepesa ya anthu anu Aisraeli amene munawapulumutsa, ndipo muwakhululukire tchimo la kupha munthu wosalakwa.” Mukatero ndiye kuti adzapezeka kuti ndi osalakwa. Kotero mudzadzichotsera nokha tchimo lokhetsa magazi wosalakwa, popeza mwachita zoyenera pamaso pa Yehova.

Kukwatira Mkazi Wogwidwa ku Nkhondo

10 Mukapita kukachita nkhondo ndi adani anu, Yehova Mulungu wanu nawapereka adani anuwo mʼmanja mwanu muwagwira ukapolo, 11 ndiye ngati muona mkazi wokongola pakati pa ogwidwawo nakutengani mtima, mukhoza kumutenga kuti akhale mkazi wanu. 12 Mumutengere ku nyumba kwanu, kumumeta tsitsi lake, mumuwenge zikhadabo zake 13 ndipo avulidwe zovala zimene anagwidwa nazo. Atakhala mʼnyumba mwanu nalira maliro a abambo ndi amayi ake kwa mwezi wathunthu, ndiye mukhoza kupita kwa iye ndi kukhala mwamuna wake ndipo iyeyo adzakhala mkazi wanu. 14 Ngati simukukondweretsedwa naye, muloleni kuti apite kumene afuna. Musamugulitse kapena kumuzunza ngati kapolo, popeza mwamuchotsa ulemu.

Ufulu wa Mwana Woyamba Kubadwa

15 Ngati munthu ali ndi akazi awiri, nakonda wina koposa mnzake, onsewa ndikubereka ana aamuna koma woyamba nakhala mwana wa mkazi amene samukondayo, 16 akamagawa chuma chake akanali moyo kwa ana akewo, asapereke ufulu wa mwana woyamba kubadwa kwa mwana wamwamuna wa mkazi amene amamukonda mʼmalo mwa mwana wake woyamba kubadwa weniweni amene ndi mwana wamkazi amene samukonda. 17 Iye ayenera kuonetsa kuti mwana wake wamwamuna wa mkazi wosakondedwayo ndiye woyamba kubadwa pomupatsa miyeso iwiri ya zonse zimene ali nazo. Mwana wamwamuna ameneyo ndiye chizindikiro cha mphamvu za abambo ake. Ufulu wokhala mwana wamwamuna woyamba ndi wake.

Mwana Wamwamuna Wowukira

18 Ngati munthu ali ndi mwana wamwamuna wosamvera ndi wowukira amene samvera a abambo ake ndi amayi ake akamuweruza, 19 abambo ndi amayi ake amugwire ndi kupita naye kwa akuluakulu ku chipata cha mzinda wake ndipo 20 akawawuze akuluakuluwo kuti, “Mwana wathu wamwamunayu ndi wosamva ndi wowukira. Iyeyu satimvera. Ndi mwana wadyera komanso ndi chidakwa.” 21 Pamenepo anthu onse a mu mzinda wake adzamuphe ndi miyala. Muyenera kuchotsa zoyipa pakati panu. Aisraeli onse adzamva zimenezi ndipo adzachita mantha.

Malamulo Osiyanasiyana

22 Ngati munthu wopezeka ndi mlandu wopha mnzake waphedwa ndipo mtembo wake wapachikidwa pamtengo, 23 musasiye mtembowo pa mtengopo usiku wonse. Muonetsetse kuti mwakawukwirira tsiku lomwelo, chifukwa aliyense wopachikidwa pamtengo ndi wotembereredwa ndi Mulungu. Musayipitse dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani ngati cholowa chanu.

Atonement for an Unsolved Murder

21 If someone is found slain, lying in a field in the land the Lord your God is giving you to possess, and it is not known who the killer was,(A) your elders and judges shall go out and measure the distance from the body to the neighboring towns. Then the elders of the town nearest the body shall take a heifer that has never been worked and has never worn a yoke(B) and lead it down to a valley that has not been plowed or planted and where there is a flowing stream. There in the valley they are to break the heifer’s neck. The Levitical priests shall step forward, for the Lord your God has chosen them to minister and to pronounce blessings(C) in the name of the Lord and to decide all cases of dispute and assault.(D) Then all the elders of the town nearest the body shall wash their hands(E) over the heifer whose neck was broken in the valley, and they shall declare: “Our hands did not shed this blood, nor did our eyes see it done. Accept this atonement for your people Israel, whom you have redeemed, Lord, and do not hold your people guilty of the blood of an innocent person.” Then the bloodshed will be atoned for,(F) and you will have purged(G) from yourselves the guilt of shedding innocent blood, since you have done what is right in the eyes of the Lord.

Marrying a Captive Woman

10 When you go to war against your enemies and the Lord your God delivers them into your hands(H) and you take captives,(I) 11 if you notice among the captives a beautiful(J) woman and are attracted to her,(K) you may take her as your wife. 12 Bring her into your home and have her shave her head,(L) trim her nails 13 and put aside the clothes she was wearing when captured. After she has lived in your house and mourned her father and mother for a full month,(M) then you may go to her and be her husband and she shall be your wife. 14 If you are not pleased with her, let her go wherever she wishes. You must not sell her or treat her as a slave, since you have dishonored her.(N)

The Right of the Firstborn

15 If a man has two wives,(O) and he loves one but not the other, and both bear him sons but the firstborn is the son of the wife he does not love,(P) 16 when he wills his property to his sons, he must not give the rights of the firstborn to the son of the wife he loves in preference to his actual firstborn, the son of the wife he does not love.(Q) 17 He must acknowledge the son of his unloved wife as the firstborn by giving him a double(R) share of all he has. That son is the first sign of his father’s strength.(S) The right of the firstborn belongs to him.(T)

A Rebellious Son

18 If someone has a stubborn and rebellious(U) son(V) who does not obey his father and mother(W) and will not listen to them when they discipline him, 19 his father and mother shall take hold of him and bring him to the elders at the gate of his town. 20 They shall say to the elders, “This son of ours is stubborn and rebellious. He will not obey us. He is a glutton and a drunkard.” 21 Then all the men of his town are to stone him to death.(X) You must purge the evil(Y) from among you. All Israel will hear of it and be afraid.(Z)

Various Laws

22 If someone guilty of a capital offense(AA) is put to death and their body is exposed on a pole, 23 you must not leave the body hanging on the pole overnight.(AB) Be sure to bury(AC) it that same day, because anyone who is hung on a pole is under God’s curse.(AD) You must not desecrate(AE) the land the Lord your God is giving you as an inheritance.