Add parallel Print Page Options

Masomphenya a Danieli a Nkhosa Yayimuna ndi Mbuzi Yayimuna

Chaka chachitatu cha ulamuliro wa mfumu Belisazara, Ine Danieli, ndinaonanso masomphenya, ena atatha amene anandionekera poyamba. Ndinaona mʼmasomphenya kuti ndinali mu mzinda wotetezedwa wa Susa mʼchigawo cha Elamu. Mʼmasomphenyawo ndinaona nditayima pafupi ndi mtsinje wa Ulai. Nditakweza maso ndinaona nkhosa yayimuna ya nyanga ziwiri, itayima pafupi ndi mtsinje. Nyanga zakezo zinali zazitali. Nyanga imodzi inali yotalika kuposa inzake, ndipo iyi inaphuka inzakeyo itamera kale. Ndinaona nkhosa yayimunayo ikuthamanga mwaukali kupita kumadzulo, kumpoto ndi kummwera. Palibe chirombo chimene chikanatha kulimbana nayo, ndipo palibe akanatha kulanditsa kanthu kwa iyo. Iyo inachita monga inafunira ndipo inali ndi mphamvu zambiri.

Pamene ndinali kulingalira za zinthu zimenezi, mwadzidzidzi mbuzi yayimuna inatulukira cha kumadzulo, kudutsa dziko lonse lapansi mwaliwiro ikuyenda mʼmalele mokhamokha. Mbuzi yayimunayo inali ndi nyanga yayikulu pakati pa maso ake. Inabwera molunjika nkhosa yayimuna ya nyanga ziwiri ija imene ndinaona itayima pafupi ndi mtsinje. Ndipo inayithamangira mwaukali. Inafika pafupi ndipo inalimbana nayo mwaukali nkhosa yayimuna ija nʼkuthyola nyanga zake ziwiri. Nkhosa yayimunayo inalibenso mphamvu zogonjetsera mbuziyo; choncho mbuzi ija inagwetsa nkhosayo pansi nʼkuyipondaponda, ndipo palibe akanatha kulanditsa nkhosayo kwa mbuziyo. Mbuziyo inayamba kudzikuza kwambiri chifukwa cha mphamvu zake koma pamene mphamvuzo zinakula kwambiri nyanga yake yayikulu inathyoka, ndipo mʼmalo mwake panamera nyanga zinayi moloza mbali zonse zinayi.

Pa imodzi mwa nyangazo panatuluka nyanga imene inali yocheperapo koma inakula kwambiri kuloza kummwera ndi kummawa ndi kuloza dziko lokongola. 10 Inakula mpaka inafikira gulu lankhondo la kumwamba, ndipo inagwetsera ena a gulu lankhondolo ndi ena a gulu la nyenyezi ku dziko lapansi ndi kuwapondaponda. 11 Inadzikuza yokha mpaka kufikira kwa mfumu ya gululo: inathetsa nsembe zimene zinkaperekedwa tsiku ndi tsiku, ndipo inagwetsa nyumba yake yopatulika. 12 Gulu lake la nkhondo linathetsa nsembe zoperekera machimo za tsiku ndi tsiku; chipembedzo choonadi chinaponderezedwa pansi. Nyangayi inapambana mu zonse zimene inachita.

13 Kenaka ndinamva wina akuyankhula; ndipo woyera winanso anamufunsa kuti, “Kodi zimene ndikuziona mʼmasomphenyazi zidzatha liti? Nsembe zoperekera machimo za tsiku ndi tsiku zidzakhala zoletsedwa mpaka liti? Nanga chonyansa chosokoneza chidzakhalapo mpaka liti? Kodi gulu la ankhondo lidzapondereza malo opatulika mpaka liti?”

14 Iye anandiyankha kuti, “Zidzachitika patapita masiku 2,300; pambuyo pake malo opatulika adzabwezeretsedwa monga kale.”

Kumasulira kwa Masomphenya

15 Ine Danieli ndikuyangʼanitsitsa masomphenyawa ndi kuyesa kuwazindikira, kuwamvetsa, ndinangoona wina wooneka ngati munthu atayima patsogolo panga. 16 Ndipo ndinamva mawu a munthu kuchokera mʼmbali mwa mtsinje wa Ulai akuyitana kuti, “Gabrieli, muwuze munthuyu tanthauzo la masomphenyawo.”

17 Atayandikira kumene ndinayima, ndinachita mantha ndi kugwa chafufumimba. Iye anati, “Mwana wa munthu, zindikira kuti masomphenyawa akunena za nthawi yachimaliziro.”

18 Pamene ankandiyankhula ndinadzigwetsa pansi chafufumimba, nʼkugona tulo tofa nato. Kenaka anandikhudza ndi kundiyimiritsa.

19 Iye anati, “Ine ndikuwuza zimene zidzachitike ukadzatha mkwiyo, chifukwa masomphenyawa ndi a nthawi ya chimaliziro.” 20 Nkhosa yayimuna ya nyanga ziwiri imene unayiona, ikuyimira mafumu a Amedi ndi Aperezi. 21 Mbuzi yayimuna ija ndi mfumu ya Agriki, ndipo nyanga yayikulu pakati pa maso ake aja ndi mfumu yoyamba. 22 Kunena za nyanga inathyoka ija ndi nyanga zinayi zimene zinaphuka mʼmalo mwake zikutanthauza maufumu anayi amene adzatuluka mʼdziko lake; koma sizidzafanana mphamvu ndi ufumu woyambawo.

23 “Pa masiku otsiriza a maufumuwa, machimo awo atachulukitsa, padzadzuka mfumu yaukali ndi yochenjera kwambiri. 24 Idzakhala yamphamvu kwambiri koma osati mphamvu za iyo yokha. Idzawononga koopsa ndipo idzapambana mu chilichonse chimene idzachite. Mfumuyi idzawononga anthu amphamvu ndi anthu oyera omwe. 25 Chifukwa cha kuchenjera kwake chinyengo chidzachuluka pa nthawi ya ulamuliro wake, ndipo idzadzikuza kuposa onse. Pamene oyera mtima adzaona ngati kuti ali otetezedwa, iyo idzawononga ambiri ndi kuwukira ngakhale Mfumu ya mafumu. Komabe idzawonongedwa, koma osati ndi mphamvu za munthu.

26 “Masomphenya okhudza madzulo ndi mmawa amene unawaona aja ndi woona, koma uwasunge masomphenyawa mwachinsinsi popeza ndi onena za masiku a mʼtsogolo kwambiri.”

27 Ine Danieli ndinafowoka ndipo ndinadwala masiku angapo. Kenaka ndinadzuka ndi kupitiriza ntchito za mfumu. Ndinada nkhawa ndi masomphenyawo; ndipo sindinathe kuwamvetsa.

Daniel’s Vision of a Ram and a Goat

In the third year of King Belshazzar’s(A) reign, I, Daniel, had a vision,(B) after the one that had already appeared to me. In my vision I saw myself in the citadel of Susa(C) in the province of Elam;(D) in the vision I was beside the Ulai Canal. I looked up,(E) and there before me was a ram(F) with two horns, standing beside the canal, and the horns were long. One of the horns was longer than the other but grew up later. I watched the ram as it charged toward the west and the north and the south. No animal could stand against it, and none could rescue from its power.(G) It did as it pleased(H) and became great.

As I was thinking about this, suddenly a goat with a prominent horn between its eyes came from the west, crossing the whole earth without touching the ground. It came toward the two-horned ram I had seen standing beside the canal and charged at it in great rage. I saw it attack the ram furiously, striking the ram and shattering its two horns. The ram was powerless to stand against it; the goat knocked it to the ground and trampled on it,(I) and none could rescue the ram from its power.(J) The goat became very great, but at the height of its power the large horn was broken off,(K) and in its place four prominent horns grew up toward the four winds of heaven.(L)

Out of one of them came another horn, which started small(M) but grew in power to the south and to the east and toward the Beautiful Land.(N) 10 It grew until it reached(O) the host of the heavens, and it threw some of the starry host down to the earth(P) and trampled(Q) on them. 11 It set itself up to be as great as the commander(R) of the army of the Lord;(S) it took away the daily sacrifice(T) from the Lord, and his sanctuary was thrown down.(U) 12 Because of rebellion, the Lord’s people[a] and the daily sacrifice were given over to it. It prospered in everything it did, and truth was thrown to the ground.(V)

13 Then I heard a holy one(W) speaking, and another holy one said to him, “How long will it take for the vision to be fulfilled(X)—the vision concerning the daily sacrifice, the rebellion that causes desolation, the surrender of the sanctuary and the trampling underfoot(Y) of the Lord’s people?”

14 He said to me, “It will take 2,300 evenings and mornings; then the sanctuary will be reconsecrated.”(Z)

The Interpretation of the Vision

15 While I, Daniel, was watching the vision(AA) and trying to understand it, there before me stood one who looked like a man.(AB) 16 And I heard a man’s voice from the Ulai(AC) calling, “Gabriel,(AD) tell this man the meaning of the vision.”(AE)

17 As he came near the place where I was standing, I was terrified and fell prostrate.(AF) “Son of man,”[b] he said to me, “understand that the vision concerns the time of the end.”(AG)

18 While he was speaking to me, I was in a deep sleep, with my face to the ground.(AH) Then he touched me and raised me to my feet.(AI)

19 He said: “I am going to tell you what will happen later in the time of wrath,(AJ) because the vision concerns the appointed time(AK) of the end.[c](AL) 20 The two-horned ram that you saw represents the kings of Media and Persia.(AM) 21 The shaggy goat is the king of Greece,(AN) and the large horn between its eyes is the first king.(AO) 22 The four horns that replaced the one that was broken off represent four kingdoms that will emerge from his nation but will not have the same power.

23 “In the latter part of their reign, when rebels have become completely wicked, a fierce-looking king, a master of intrigue, will arise. 24 He will become very strong, but not by his own power. He will cause astounding devastation and will succeed in whatever he does. He will destroy those who are mighty, the holy people.(AP) 25 He will cause deceit(AQ) to prosper, and he will consider himself superior. When they feel secure, he will destroy many and take his stand against the Prince of princes.(AR) Yet he will be destroyed, but not by human power.(AS)

26 “The vision of the evenings and mornings that has been given you is true,(AT) but seal(AU) up the vision, for it concerns the distant future.”(AV)

27 I, Daniel, was worn out. I lay exhausted(AW) for several days. Then I got up and went about the king’s business.(AX) I was appalled(AY) by the vision; it was beyond understanding.

Footnotes

  1. Daniel 8:12 Or rebellion, the armies
  2. Daniel 8:17 The Hebrew phrase ben adam means human being. The phrase son of man is retained as a form of address here because of its possible association with “Son of Man” in the New Testament.
  3. Daniel 8:19 Or because the end will be at the appointed time