Add parallel Print Page Options

Buku la Mwana Wankhosa

Kenaka ndinaona buku mʼdzanja la wokhala pa mpando waufumu uja. Bukulo linali lolembedwa mbali zonse ndipo linali lomatidwa ndi zomatira zisanu ndi ziwiri. Ndipo ndinaona mngelo wamphamvu akulengeza ndi mawu okweza kuti, “Ndani ali woyenera kumatula zomatira ndi kufutukula bukuli?” Koma panalibe ndi mmodzi yemwe kumwamba kapena pa dziko lapansi kapena kunsi kwa dziko lapansi woti afutukule bukulo kapena kuona zamʼkati mwake. Ndinalira kwambiri chifukwa panalibe amene anapezeka woyenera kufutukula bukuli kapena kuona zamʼkati mwake. Tsono mmodzi mwa akuluakulu aja anati kwa ine, “Usalire! Taona, Mkango wa fuko la Yuda, Muzu wa Davide, wapambana. Iye angathe kufutukula bukuli ndi kumatula zomatira zisanu ndi ziwirizo.”

Kenaka ndinaona Mwana Wankhosa akuoneka ngati wophedwa atayimirira pakatikati pa mpando waufumu uja ndi zamoyo zinayi zija ndi akuluakulu aja. Mwana Wankhosayo anali ndi nyanga zisanu ndi ziwiri ndi maso asanu ndi awiri omwe ndi Mizimu isanu ndi iwiri ya Mulungu yomwe anayitumiza ku dziko lonse lapansi. Iye anabwera natenga buku lija limene linali mʼdzanja lamanja la wokhala pa mpando waufumuyo. Ndipo atalitenga, zamoyo zinayi zija ndi akuluakulu 24 aja anadzigwetsa pansi pamaso pa Mwana Wankhosa. Aliyense wa akuluakuluwo anali ndi zeze ndiponso mbale zagolide zodzaza ndi lubani. Lubaniyo ndi mapemphero a oyera mtima. Ndipo ankayimba nyimbo yatsopano yakuti,

“Inu ndinu woyenera kulandira bukuli
    ndi kumatula zomatira zake,
chifukwa munaphedwa,
    ndipo magazi anu munagulira Mulungu
    anthu a fuko lililonse, a chiyankhulo chilichonse, ndi mtundu uliwonse.
10 Inu munawasandutsa kukhala mtundu waufumu ndi ansembe otumikira Mulungu,
    ndipo adzalamulira dziko lapansi.”

11 Kenaka nditayangʼananso ndinamva mawu a angelo ambiri, miyandamiyanda kuchulukitsa ndi miyandamiyanda. Anazungulira mpando waufumu pamodzi ndi zamoyo zija ndi akuluakulu aja. 12 Ndipo angelowo anayimba ndi mawu ofuwula akuti,

“Mwana Wankhosa amene anaphedwayu
    ndi woyenera kulandira ulamuliro, chuma, nzeru, mphamvu, ulemu,
    ulemerero ndi mayamiko.”

13 Kenaka ndinamva mawu a cholengedwa chilichonse kumwamba, pa dziko lapansi, kunsi kwa dziko lapansi, pa nyanja ndi zonse zili mʼmenemo zikuyimba kuti,

“Kwa wokhala pa mpando waufumu ndi kwa Mwana Wankhosa,
    kukhale mayamiko, ulemu, ulemerero ndi mphamvu
mpaka muyaya!”

14 Zamoyo zinayi zija zinati: “Ameni,” ndipo akuluakulu aja anadzigwetsa pansi napembedza.

The Scroll and the Lamb

Then I saw in the right hand of him who sat on the throne(A) a scroll with writing on both sides(B) and sealed(C) with seven seals. And I saw a mighty angel(D) proclaiming in a loud voice, “Who is worthy to break the seals and open the scroll?” But no one in heaven or on earth or under the earth could open the scroll or even look inside it. I wept and wept because no one was found who was worthy to open the scroll or look inside. Then one of the elders said to me, “Do not weep! See, the Lion(E) of the tribe of Judah,(F) the Root of David,(G) has triumphed. He is able to open the scroll and its seven seals.”

Then I saw a Lamb,(H) looking as if it had been slain, standing at the center of the throne, encircled by the four living creatures(I) and the elders.(J) The Lamb had seven horns and seven eyes,(K) which are the seven spirits[a](L) of God sent out into all the earth. He went and took the scroll from the right hand of him who sat on the throne.(M) And when he had taken it, the four living creatures(N) and the twenty-four elders(O) fell down before the Lamb. Each one had a harp(P) and they were holding golden bowls full of incense, which are the prayers(Q) of God’s people. And they sang a new song, saying:(R)

“You are worthy(S) to take the scroll
    and to open its seals,
because you were slain,
    and with your blood(T) you purchased(U) for God
    persons from every tribe and language and people and nation.(V)
10 You have made them to be a kingdom and priests(W) to serve our God,
    and they will reign[b] on the earth.”(X)

11 Then I looked and heard the voice of many angels, numbering thousands upon thousands, and ten thousand times ten thousand.(Y) They encircled the throne and the living creatures(Z) and the elders.(AA) 12 In a loud voice they were saying:

“Worthy is the Lamb,(AB) who was slain,(AC)
    to receive power and wealth and wisdom and strength
    and honor and glory and praise!”(AD)

13 Then I heard every creature in heaven and on earth and under the earth(AE) and on the sea, and all that is in them, saying:

“To him who sits on the throne(AF) and to the Lamb(AG)
    be praise and honor and glory and power,
for ever and ever!”(AH)

14 The four living creatures(AI) said, “Amen,”(AJ) and the elders(AK) fell down and worshiped.(AL)

Footnotes

  1. Revelation 5:6 That is, the sevenfold Spirit
  2. Revelation 5:10 Some manuscripts they reign