Add parallel Print Page Options

Kumwamba ndi Dziko Lapansi Zatsopano

21 Kenaka ndinaona kumwamba kwatsopano ndi dziko lapansi latsopano pakuti kumwamba koyamba ndi dziko lapansi loyamba zinapita ndipo kunalibenso nyanja ina iliyonse. Ndinaona mzinda wopatulika, Yerusalemu watsopano, ukutsika kuchokera kumwamba kwa Mulungu, utakonzedwa ngati mkwatibwi wovala zokongola kukonzekera mwamuna wake. Ndipo ndinamva mawu ofuwula kuchokera ku Mpando Waufumu kuti, “Taonani! Malo wokhalapo Mulungu ali pakati pa anthu, ndipo Iye adzakhala ndi anthuwo. Iwo adzakhala anthu ake ndipo Mulungu mwini adzakhala nawo nakhala Mulungu wawo. ‘Mulungu adzapukuta misozi yonse mʼmaso mwawo. Sikudzakhalanso imfa kapena kukhuza maliro kapena kulira kapena ululu popeza zakale zapita.’ ”

Amene anakhala pa mpando waufumuyo anati, “Ndikulenga zinthu zonse zikhale zatsopano!” Ndipo anati, “Lemba izi, pakuti mawu awa ndi okhulupirika ndi woona.”

Iye anandiwuza kuti, “Kwatha. Ine ndine Alefa ndi Omega, Woyamba ndi Wotsiriza. Kwa onse akumva ludzu, ndidzawapatsa zakumwa zaulere zochokera ku kasupe wamadzi amoyo. Iye amene adzapambane adzalandira zonsezi, ndipo ndidzakhala Mulungu wake ndi Iye adzakhala mwana wanga. Koma amantha, osakhulupirira, okonda zonyansa, opha anthu, achiwerewere, amatsenga, opembedza mafano ndi abodza, malo awo adzakhala nyanja yamoto ya sulufule wotentha. Iyi ndi imfa yachiwiri.”

Mzinda wa Yerusalemu Watsopano

Mmodzi wa angelo asanu ndi awiri aja, anali ndi mbale zisanu ndi ziwiri zodzaza ndi miliri yotsiriza isanu ndi iwiri anandiwuza kuti, “Bwera, ine ndidzakuonetsa mkwatibwi wa Mwana Wankhosa.” 10 Ndipo anandinyamula mwa Mzimu Woyera kupita nane ku phiri lalikulu ndi lalitali nandionetsa mzinda wopatulika, Yerusalemu ukutsika kuchokera kumwamba kwa Mulungu. 11 Unawala ndi ulemerero wa Mulungu, ndipo kuthwanima kwake kunali ngati mwala wamtengowapatali, ngati jasipa; woyera ngati krustalo. 12 Mzindawo unali ndi mpanda waukulu ndi wautali, unali ndi zipata khumi ndi ziwiri, ndipo panali angelo khumi ndi awiri. Pa chipata chilichonse panayima mngelo. Pa chipata chilichonse panalembedwa dzina la fuko la Israeli. 13 Kummawa kunali zipata zitatu, kumpoto zitatu, kummwera zitatu ndi kumadzulo zitatu. 14 Mpanda wa mzindawu unali ndi maziko khumi ndi awiri ndipo pa mazikopo panali mayina khumi ndi awiri a atumwi a Mwana Wankhosa.

15 Mngelo amene ankayankhula nane uja anali ndi ndodo yagolide yoyezera mzindawo, zipata zake ndi mpanda wake. 16 Mzindawo unamangidwa mofanana kutalika kwake, mulitali ndi mulifupi munali mofanana. Anayeza mzindawo ndi ndodo ija ndipo anapeza kuti mulitali, mulifupi ndi msinkhu wake kutalika kwake kunali makilomita 2,200. 17 Anayesa mpanda uja ndipo kuchindikala kwake kunali kopitirirapo mamita 65 monga mwa muyeso wa anthu umene mngelo anagwiritsa ntchito. 18 Mpandawo unapangidwa ndi yasipa, ndipo mzindawo unali wagolide oyengeka owala ngati galasi. 19 Maziko a mpanda wa mzindawo anali okongoletsedwa ndi miyala yamtengowapatali ya mtundu uliwonse. Maziko oyamba anali yasipa, achiwiri anali safiro, achitatu ndi kalikedo, achinayi ndi simaragido, 20 achisanu ndi sardiyo, achisanu ndi chiwiri ndi krusolito, achisanu ndi chitatu ndi berulo, achisanu ndi chinayi ndi topaziyo, a khumi ndi krusoprazo, a khumi ndi chimodzi ndi huakito, a khumi ndi chiwiri ndi emetusto. 21 Zipata khumi ndi ziwiri zija zinapangidwa ndi ngale, chipata chilichonse chinapangidwa ndi ngale imodzi. Misewu ya mzindawo inali yopangidwa ndi golide oyengeka, owala ngati galasi.

22 Ine sindinaone Nyumba ya Mulungu iliyonse mu mzindawo chifukwa Ambuye Mulungu Wamphamvuzonse ndi Mwana Wankhosa ndiwo Nyumba yake. 23 Palibe chifukwa choti dzuwa kapena mwezi ziwale popeza mu mzindawo ulemerero wa Mulungu ndiwo umawalamo ndipo nyale yake ndi Mwana Wankhosa uja. 24 Mitundu ya anthu idzayenda mʼkuwala kwake ndipo mafumu a dziko lapansi adzabweretsa ulemerero wawo mu mzindamo. 25 Zipata zake sizidzatsekedwa ngakhale tsiku limodzi lomwe pakuti sikudzakhala usiku kumeneko. 26 Ulemerero ndi ulemu wa mitundu ya anthu adzapita nazo kumeneko. 27 Kanthu kosayeretsedwa sikadzalowamo, kuphatikizanso aliyense wochita zinthu zochititsa manyazi ndi zachinyengo, koma okhawo amene mayina awo alembedwa mʼbuku lamoyo la Mwana Wankhosa.

A New Heaven and a New Earth

21 Then I saw “a new heaven and a new earth,”[a](A) for the first heaven and the first earth had passed away,(B) and there was no longer any sea. I saw the Holy City,(C) the new Jerusalem, coming down out of heaven from God,(D) prepared as a bride(E) beautifully dressed for her husband. And I heard a loud voice from the throne saying, “Look! God’s dwelling place is now among the people, and he will dwell with them.(F) They will be his people, and God himself will be with them and be their God.(G) ‘He will wipe every tear from their eyes.(H) There will be no more death’[b](I) or mourning or crying or pain,(J) for the old order of things has passed away.”(K)

He who was seated on the throne(L) said, “I am making everything new!”(M) Then he said, “Write this down, for these words are trustworthy and true.”(N)

He said to me: “It is done.(O) I am the Alpha and the Omega,(P) the Beginning and the End. To the thirsty I will give water without cost(Q) from the spring of the water of life.(R) Those who are victorious(S) will inherit all this, and I will be their God and they will be my children.(T) But the cowardly, the unbelieving, the vile, the murderers, the sexually immoral, those who practice magic arts, the idolaters and all liars(U)—they will be consigned to the fiery lake of burning sulfur.(V) This is the second death.”(W)

The New Jerusalem, the Bride of the Lamb

One of the seven angels who had the seven bowls full of the seven last plagues(X) came and said to me, “Come, I will show you the bride,(Y) the wife of the Lamb.” 10 And he carried me away(Z) in the Spirit(AA) to a mountain great and high, and showed me the Holy City, Jerusalem, coming down out of heaven from God.(AB) 11 It shone with the glory of God,(AC) and its brilliance was like that of a very precious jewel, like a jasper,(AD) clear as crystal.(AE) 12 It had a great, high wall with twelve gates,(AF) and with twelve angels at the gates. On the gates were written the names of the twelve tribes of Israel.(AG) 13 There were three gates on the east, three on the north, three on the south and three on the west. 14 The wall of the city had twelve foundations,(AH) and on them were the names of the twelve apostles(AI) of the Lamb.

15 The angel who talked with me had a measuring rod(AJ) of gold to measure the city, its gates(AK) and its walls. 16 The city was laid out like a square, as long as it was wide. He measured the city with the rod and found it to be 12,000 stadia[c] in length, and as wide and high as it is long. 17 The angel measured the wall using human(AL) measurement, and it was 144 cubits[d] thick.[e] 18 The wall was made of jasper,(AM) and the city of pure gold, as pure as glass.(AN) 19 The foundations of the city walls were decorated with every kind of precious stone.(AO) The first foundation was jasper,(AP) the second sapphire, the third agate, the fourth emerald, 20 the fifth onyx, the sixth ruby,(AQ) the seventh chrysolite, the eighth beryl, the ninth topaz, the tenth turquoise, the eleventh jacinth, and the twelfth amethyst.[f] 21 The twelve gates(AR) were twelve pearls,(AS) each gate made of a single pearl. The great street of the city was of gold, as pure as transparent glass.(AT)

22 I did not see a temple(AU) in the city, because the Lord God Almighty(AV) and the Lamb(AW) are its temple. 23 The city does not need the sun or the moon to shine on it, for the glory of God(AX) gives it light,(AY) and the Lamb(AZ) is its lamp. 24 The nations will walk by its light, and the kings of the earth will bring their splendor into it.(BA) 25 On no day will its gates(BB) ever be shut,(BC) for there will be no night there.(BD) 26 The glory and honor of the nations will be brought into it.(BE) 27 Nothing impure will ever enter it, nor will anyone who does what is shameful or deceitful,(BF) but only those whose names are written in the Lamb’s book of life.(BG)

Footnotes

  1. Revelation 21:1 Isaiah 65:17
  2. Revelation 21:4 Isaiah 25:8
  3. Revelation 21:16 That is, about 1,400 miles or about 2,200 kilometers
  4. Revelation 21:17 That is, about 200 feet or about 65 meters
  5. Revelation 21:17 Or high
  6. Revelation 21:20 The precise identification of some of these precious stones is uncertain.