Add parallel Print Page Options

Babuloni Wagwa, Haleluya!

19 Zitatha izi, ndinamva chimene chinamveka ngati phokoso la gulu lalikulu mmwamba likufuwula kuti,

“Haleluya!
Chipulumutso ndi ulemerero ndi mphamvu ndi za Mulungu wathu,
    pakuti chiweruzo chake ndi choona ndi cha chilungamo.
Iye waweruza mkazi wadama wotchuka uja
    amene anayipitsa dziko lonse lapansi ndi zigololo zake.
Iye wabwezera pa mkaziyo magazi a atumiki ake.”

Ndipo anafuwulanso kuti,

“Haleluya!
Utsi wochokera kwa mkazi wadamayo udzakwera kumwamba mpaka muyaya.”

Akuluakulu 24 aja ndi zamoyo zinayi zija anadzigwetsa pansi kupembedza Mulungu amene anakhala pa mpando waufumu. Ndipo anafuwula kuti,

“Ameni, Haleluya!”

Kenaka mawu anachoka ku mpando waufumu kuti,

“Lemekezani Mulungu wathu
    inu nonse atumiki ake,
inu amene mumamuopa,
    nonse angʼono ndi akulu!”

Kenaka ndinamva chimene chinamveka ngati gulu lalikulu, ngati mkokomo wamadzi othamanga ndipo ngati kugunda kwakukulu kwa bingu, ndipo anati,

“Haleluya!
    Pakuti Ambuye Mulungu wathu Wamphamvuzonse akulamulira.
Tiyeni tisangalale ndi kukondwera
    ndi kumutamanda!
Pakuti nthawi ya ukwati wa Mwana Wankhosa yafika,
    ndipo Mkwatibwi wakonzekeratu.
Wapatsidwa nsalu yoyera kwambiri, yowala ndi yosada
    kuti avale.”

(Nsalu yoyera kwambiri ikuyimira ntchito zolungama za oyera mtima).

Kenaka mngelo anandiwuza kuti, “Lemba kuti, Odala amene ayitanidwa ku phwando la ukwati wa Mwana Wankhosa.” Ndipo anatinso, “Awa ndiwo mawu woona a Mulungu.”

10 Pamenepo ndinadzigwetsa pa mapazi ake kumupembedza. Koma anandiwuza kuti, “Usatero ayi, ine ndine mtumiki mnzako ngati iwe yemwe, ndiponso ngati abale ako amene asunga umboni wa Yesu. Pembedza Mulungu. Pakuti umboni wa Yesu ndiye mzimu wa uneneri.”

Wokwera pa Kavalo Woyera

11 Ndinaona kumwamba kutatsekuka ndipo patsogolo panga panali kavalo woyera, amene anakwerapo dzina lake linali Wokhulupirika ndiponso Woona. Poweruza ndi kuchita nkhondo, amachita molungama. 12 Maso ake anali ngati malawi amoto, ndipo pamutu pake panali zipewa zaufumu zambiri. Anali ndi dzina lolembedwa, lodziwika ndi Iye yekha, osati wina aliyense. 13 Iye anavala mkanjo woviyika mʼmagazi, ndipo dzina lake ndi Mawu a Mulungu. 14 Magulu ankhondo akumwamba ankamutsatira atakwera pa akavalo oyera, ndipo iwowo atavala nsalu zoyera kwambiri ndi zosada. 15 Mʼkamwa mwake munatuluka lupanga lakuthwa limene anati akaphe nalo mitundu ya anthu. Iye adzalamulira ndi ndodo yachitsulo. Iye anaponda choponderamo mphesa cha ukali wa Mulungu Wamphamvuzonse. 16 Pa chovala ndi pa ntchafu pake panalembedwa dzina ili:

MFUMU YA MAFUMU NDI MBUYE WA AMBUYE.

17 Ndipo ndinaona mngelo atayimirira pa dzuwa amene anafuwula ndi mawu okweza kwa mbalame zonse zowuluka mlengalenga kuti, “Bwerani, sonkhanani pamodzi ku phwando lalikulu la Mulungu. 18 Kuti mudye mnofu wa mafumu, wa akulu a ankhondo, ndi wa anthu amphamvu, wa akavalo ndi okwerapo awo, ndi wa anthu onse, mfulu ndi akapolo, angʼono ndi aakulu.”

19 Kenaka ndinaona chirombo chija ndi mafumu a dziko lapansi ndi magulu ankhondo atasonkhana pamodzi kuti achite nkhondo ndi wokwera pa kavalo ndi ankhondo ake. 20 Koma chirombocho chinagwidwa pamodzi ndi mneneri wonyenga uja amene anachita zizindikiro zodabwitsa pamaso pake. Ndi zizindikirozi anasocheretsa amene analembedwa chizindikiro cha chirombocho napembedza fano lake. Onse awiri anaponyedwa amoyo mʼnyanja yamoto yasulufule wotentha. 21 Ena onse anaphedwa ndi lupanga lija linatuluka mʼkamwa mwa wokwera pa kavalo uja, ndipo mbalame zonse zinadya mokwanira mnofu wa anthu akufawo.

Threefold Hallelujah Over Babylon’s Fall

19 After this I heard what sounded like the roar of a great multitude(A) in heaven shouting:

“Hallelujah!(B)
Salvation(C) and glory and power(D) belong to our God,
    for true and just are his judgments.(E)
He has condemned the great prostitute(F)
    who corrupted the earth by her adulteries.
He has avenged on her the blood of his servants.”(G)

And again they shouted:

“Hallelujah!(H)
The smoke from her goes up for ever and ever.”(I)

The twenty-four elders(J) and the four living creatures(K) fell down(L) and worshiped God, who was seated on the throne. And they cried:

“Amen, Hallelujah!”(M)

Then a voice came from the throne, saying:

“Praise our God,
    all you his servants,(N)
you who fear him,
    both great and small!”(O)

Then I heard what sounded like a great multitude,(P) like the roar of rushing waters(Q) and like loud peals of thunder, shouting:

“Hallelujah!(R)
    For our Lord God Almighty(S) reigns.(T)
Let us rejoice and be glad
    and give him glory!(U)
For the wedding of the Lamb(V) has come,
    and his bride(W) has made herself ready.
Fine linen,(X) bright and clean,
    was given her to wear.”

(Fine linen stands for the righteous acts(Y) of God’s holy people.)

Then the angel said to me,(Z) “Write this:(AA) Blessed are those who are invited to the wedding supper of the Lamb!”(AB) And he added, “These are the true words of God.”(AC)

10 At this I fell at his feet to worship him.(AD) But he said to me, “Don’t do that! I am a fellow servant with you and with your brothers and sisters who hold to the testimony of Jesus. Worship God!(AE) For it is the Spirit of prophecy who bears testimony to Jesus.”(AF)

The Heavenly Warrior Defeats the Beast

11 I saw heaven standing open(AG) and there before me was a white horse, whose rider(AH) is called Faithful and True.(AI) With justice he judges and wages war.(AJ) 12 His eyes are like blazing fire,(AK) and on his head are many crowns.(AL) He has a name written on him(AM) that no one knows but he himself.(AN) 13 He is dressed in a robe dipped in blood,(AO) and his name is the Word of God.(AP) 14 The armies of heaven were following him, riding on white horses and dressed in fine linen,(AQ) white(AR) and clean. 15 Coming out of his mouth is a sharp sword(AS) with which to strike down(AT) the nations. “He will rule them with an iron scepter.”[a](AU) He treads the winepress(AV) of the fury of the wrath of God Almighty. 16 On his robe and on his thigh he has this name written:(AW)

king of kings and lord of lords.(AX)

17 And I saw an angel standing in the sun, who cried in a loud voice to all the birds(AY) flying in midair,(AZ) “Come,(BA) gather together for the great supper of God,(BB) 18 so that you may eat the flesh of kings, generals, and the mighty, of horses and their riders, and the flesh of all people,(BC) free and slave,(BD) great and small.”(BE)

19 Then I saw the beast(BF) and the kings of the earth(BG) and their armies gathered together to wage war against the rider on the horse(BH) and his army. 20 But the beast was captured, and with it the false prophet(BI) who had performed the signs(BJ) on its behalf.(BK) With these signs he had deluded(BL) those who had received the mark of the beast(BM) and worshiped its image.(BN) The two of them were thrown alive into the fiery lake(BO) of burning sulfur.(BP) 21 The rest were killed with the sword(BQ) coming out of the mouth of the rider on the horse,(BR) and all the birds(BS) gorged themselves on their flesh.

Footnotes

  1. Revelation 19:15 Psalm 2:9