Add parallel Print Page Options

Mbale Zisanu ndi Ziwiri za Mkwiyo wa Mulungu

16 Kenaka ndinamva mawu ofuwula kuchokera ku Nyumba ya Mulungu ija kuwuza angelo asanu ndi awiri kuti, “Pitani, katsanulireni pa dziko lapansi ukali wa Mulungu umene uli mʼmbale zisanu ndi ziwirizi!”

Mngelo woyamba anapita natsanula mbale yake pa dziko lapansi ndipo zilonda zoyipa ndi zowawa zinabuka pa anthu amene anali ndi chizindikiro cha chirombo chija, napembedza fano lake.

Mngelo wachiwiri anapita natsanula mbale yake pa nyanja ndipo madzi ake anasanduka magazi, magazi ake ngati a munthu wakufa. Chamoyo chilichonse cha mʼnyanjamo chinafa.

Mngelo wachitatu anapita natsanula mbale yake pa mitsinje ndi akasupe amadzi ndipo zinasanduka magazi. Kenaka ndinamva mngelo wolamulira madzi uja akuti,

“Inu mwachita chilungamo, Inu Woyerayo,
    amene mulipo ndipo munalipo;
pakuti iwo anakhetsa magazi a oyera anu ndi aneneri anu,
    nʼchifukwa chake mwawapatsa magazi kuti amwe, zomwe zikuwayenera.”

Kenaka ndinamva mawu ochokera ku guwa lansembe akuti,

“Inde, Ambuye Mulungu Wamphamvuzonse,
    chiweruzo chanu ndi choona ndi cholungama.”

Mngelo wachinayi anapita natsanula mbale yake pa dzuwa ndipo dzuwa linapatsidwa mphamvu yopsereza anthu ndi moto. Anapserera nako kutentha kwakukuluko ndipo anatukwana Mulungu, amene anali ndi ulamuliro pa miliri imeneyi, koma anakana kulapa ndi kumulemekeza.

10 Mngelo wachisanu anapita natsanula mbale yake pa mpando waufumu wa chirombo chija ndipo mdima unagwa ponse pamene panali ufumu wake. Anthu analuma malilime awo chifukwa cha ululu. 11 Ndipo anatukwana Mulungu wakumwamba chifukwa cha maululu awo ndi zilonda zawo koma anakana kulapa pa zimene anachita.

12 Mngelo wachisanu ndi chimodzi anapita natsanula mbale yake pa mtsinje waukulu wa Yufurate, ndipo madzi ake anaphwa kuti pakhale njira yodzera mafumu ochokera kummawa. 13 Kenaka ndinaona mizimu yoyipa itatu imene inkaoneka ngati achule; inatuluka mʼkamwa mwa chinjoka chija, mʼkamwa mwa chirombo chija ndi mʼkamwa mwa mneneri wonyenga uja. 14 Imeneyi ndiyo mizimu ya ziwanda imene imachita zizindikiro zodabwitsa ndipo imatuluka kupita kwa mafumu a dziko lonse, kukawasonkhanitsa ku nkhondo ya pa tsiku lalikulu la Mulungu Wamphamvuzonse.

15 “Taonani, ndikubwera ngati mbala! Wodala munthu amene ali maso, nasunga zovala zake, kuti asayende maliseche kuti angaonetse maliseche ake.”

16 Kenaka mizimu ija inasonkhanitsa pamodzi mafumu ku malo amene mʼChihebri amatchedwa Armagedo.

17 Mngelo wachisanu ndi chiwiri anatsanulira mbale yake mu mlengalenga ndipo ku Nyumba ya Mulungu kunamveka mawu ofuwula kuchokera ku mpando waufumu kuti, “Kwatha!” 18 Kenaka kunachitika mphenzi, phokoso, mabingu ndi chivomerezi choopsa. Chivomerezi ngati ichi sichinachitikepo chikhalire cha munthu pa dziko lapansi. Chinali chivomerezi choopsa kwambiri. 19 Mzinda waukuluwo unagawika magawo atatu ndipo mizinda ya mitundu ya anthu inagwa. Mulungu anakumbukira Babuloni Wamkulu namupatsa chikho chake chodzaza ndi vinyo wa ukali wa mkwiyo wake. 20 Chilumba chilichonse chinathawa ndipo mapiri sanaonekenso. 21 Matalala akuluakulu olemera pafupifupi makilogalamu makumi asanu anagwa kuchokera kumwamba kugwera pa anthu. Ndipo anthu anatukwana Mulungu chifukwa cha mliri wa matalala popeza unali mliri woopsa kwambiri.

The Seven Bowls of God’s Wrath

16 Then I heard a loud voice from the temple(A) saying to the seven angels,(B) “Go, pour out the seven bowls of God’s wrath on the earth.”(C)

The first angel went and poured out his bowl on the land,(D) and ugly, festering sores(E) broke out on the people who had the mark of the beast and worshiped its image.(F)

The second angel poured out his bowl on the sea, and it turned into blood like that of a dead person, and every living thing in the sea died.(G)

The third angel poured out his bowl on the rivers and springs of water,(H) and they became blood.(I) Then I heard the angel in charge of the waters say:

“You are just in these judgments,(J) O Holy One,(K)
    you who are and who were;(L)
for they have shed the blood of your holy people and your prophets,(M)
    and you have given them blood to drink(N) as they deserve.”

And I heard the altar(O) respond:

“Yes, Lord God Almighty,(P)
    true and just are your judgments.”(Q)

The fourth angel(R) poured out his bowl on the sun,(S) and the sun was allowed to scorch people with fire.(T) They were seared by the intense heat and they cursed the name of God,(U) who had control over these plagues, but they refused to repent(V) and glorify him.(W)

10 The fifth angel poured out his bowl on the throne of the beast,(X) and its kingdom was plunged into darkness.(Y) People gnawed their tongues in agony 11 and cursed(Z) the God of heaven(AA) because of their pains and their sores,(AB) but they refused to repent of what they had done.(AC)

12 The sixth angel poured out his bowl on the great river Euphrates,(AD) and its water was dried up to prepare the way(AE) for the kings from the East.(AF) 13 Then I saw three impure spirits(AG) that looked like frogs;(AH) they came out of the mouth of the dragon,(AI) out of the mouth of the beast(AJ) and out of the mouth of the false prophet.(AK) 14 They are demonic spirits(AL) that perform signs,(AM) and they go out to the kings of the whole world,(AN) to gather them for the battle(AO) on the great day(AP) of God Almighty.

15 “Look, I come like a thief!(AQ) Blessed is the one who stays awake(AR) and remains clothed, so as not to go naked and be shamefully exposed.”(AS)

16 Then they gathered the kings together(AT) to the place that in Hebrew(AU) is called Armageddon.(AV)

17 The seventh angel poured out his bowl into the air,(AW) and out of the temple(AX) came a loud voice(AY) from the throne, saying, “It is done!”(AZ) 18 Then there came flashes of lightning, rumblings, peals of thunder(BA) and a severe earthquake.(BB) No earthquake like it has ever occurred since mankind has been on earth,(BC) so tremendous was the quake. 19 The great city(BD) split into three parts, and the cities of the nations collapsed. God remembered(BE) Babylon the Great(BF) and gave her the cup filled with the wine of the fury of his wrath.(BG) 20 Every island fled away and the mountains could not be found.(BH) 21 From the sky huge hailstones,(BI) each weighing about a hundred pounds,[a] fell on people. And they cursed God(BJ) on account of the plague of hail,(BK) because the plague was so terrible.

Footnotes

  1. Revelation 16:21 Or about 45 kilograms