Add parallel Print Page Options

Angelo Asanu ndi Awiri Okhala ndi Miliri Isanu ndi Iwiri

15 Kumwamba ndinaona chizindikiro china chachikulu ndi chodabwitsa: angelo asanu ndi awiri ali ndi miliri isanu ndi iwiri yomaliza chifukwa Mulungu anakwiya kotheratu. Ndipo ndinaona chimene chinaoneka ngati nyanja yonyezimira yosakaniza ndi moto, ndipo pambali pa nyanjayo panayima amene anagonjetsa chirombo chija ndi fano lake, ndi nambala yotanthauza dzina lake. Anthuwo ananyamula azeze amene Mulungu anawapatsa. Iwo ankayimba nyimbo ya Mose, mtumiki wa Mulungu, ndi nyimbo ya Mwana Wankhosa. Nyimbo yake inkati,

“Zochita zanu ndi zazikulu ndi zodabwitsa,
    Ambuye Mulungu Wamphamvuzonse
Njira zanu ndi zachilungamo ndi zoona,
    Mfumu ya mitundu yonse.
Inu Ambuye, ndani angapande kukuopani,
    ndi kulemekeza dzina lanu?
Pakuti Inu nokha ndiye woyera.
Anthu a mitundu yonse adzabwera
    kudzapembedza pamaso panu,
pakuti ntchito zanu zolungama zaonekera poyera.”

Zitatha izi, ndinaona kumwamba Nyumba ya Mulungu imene ndi Tenti ya Umboni, atatsekula. Mʼnyumbamo munatuluka angelo asanu ndi awiri ndi miliri isanu ndi iwiri. Angelowo anavala nsalu zoyera bwino zonyezimira ndi malamba agolide pa zifuwa zawo. Ndipo kenaka chimodzi cha zamoyo zinayi zija chinapereka kwa angelo asanu ndi awiri mbale zisanu ndi ziwiri zodzaza ndi ukali wa Mulungu amene ali ndi moyo mpaka muyaya. Ndipo Nyumba ya Mulungu inadzaza ndi utsi wochokera ku ulemerero wa Mulungu ndi ku mphamvu zake, ndipo panalibe yemwe akanalowa mʼNyumbayo mpaka miliri isanu ndi iwiri ya angelo asanu ndi awiri aja itatha.

Seven Angels With Seven Plagues

15 I saw in heaven another great and marvelous sign:(A) seven angels(B) with the seven last plagues(C)—last, because with them God’s wrath is completed. And I saw what looked like a sea of glass(D) glowing with fire and, standing beside the sea, those who had been victorious(E) over the beast(F) and its image(G) and over the number of its name.(H) They held harps(I) given them by God and sang the song of God’s servant(J) Moses(K) and of the Lamb:(L)

“Great and marvelous are your deeds,(M)
    Lord God Almighty.(N)
Just and true are your ways,(O)
    King of the nations.[a]
Who will not fear you, Lord,(P)
    and bring glory to your name?(Q)
For you alone are holy.
All nations will come
    and worship before you,(R)
for your righteous acts(S) have been revealed.”[b]

After this I looked, and I saw in heaven the temple(T)—that is, the tabernacle of the covenant law(U)—and it was opened.(V) Out of the temple(W) came the seven angels with the seven plagues.(X) They were dressed in clean, shining linen(Y) and wore golden sashes around their chests.(Z) Then one of the four living creatures(AA) gave to the seven angels(AB) seven golden bowls filled with the wrath of God, who lives for ever and ever.(AC) And the temple was filled with smoke(AD) from the glory of God and from his power, and no one could enter the temple(AE) until the seven plagues of the seven angels were completed.

Footnotes

  1. Revelation 15:3 Some manuscripts ages
  2. Revelation 15:4 Phrases in this song are drawn from Psalm 111:2,3; Deut. 32:4; Jer. 10:7; Psalms 86:9; 98:2.