Add parallel Print Page Options

Chirombo Chotuluka Mʼnyanja

13 Ndipo ndinaona chirombo chikutuluka mʼnyanja. Chinali ndi nyanga khumi ndi mitu isanu ndi iwiri. Pa nyanga iliyonse chinavala chipewa chaufumu, ndipo pa mutu uliwonse panali dzina lonyoza Mulungu. Chirombo chimene ndinachionacho chinali ngati kambuku, mapazi ake ngati chimbalangondo, kukamwa kwake ngati kwa mkango. Chinjoka chija chinapatsa chirombocho mphamvu zake, mpando wake waufumu ndiponso ulamuliro waukulu. Umodzi wa mitu wa chirombocho unkaoneka ngati uli ndi bala losati nʼkupola, koma nʼkuti balalo litapola. Dziko lonse linadabwa ndipo linatsatira chirombocho. Anthu anapembedza chinjoka chija chifukwa chinapereka ulamuliro wake kwa chirombocho. Nachonso chirombo chija anachipembedza nʼkumafunsa kuti, “Ndani angafanane ndi chirombochi? Ndani angachite nacho nkhondo?”

Chirombo chija chinaloledwa kuyankhula mawu onyada ndi achipongwe kwa Mulungu. Chinapatsidwa mphamvu zolamulira pa miyezi 42. Ndipo chinayamba kuyankhula mawu achipongwe onyoza Mulungu, dzina lake, malo okhalamo ndi onse amene amakhala kumwamba. Chinaloledwa kuchita nkhondo ndi oyera mtima ndi kuwagonjetsa. Ndipo chinapatsidwanso mphamvu zolamulira anthu a fuko lililonse, mtundu uliwonse ndi chiyankhulo chilichonse. Anthu onse okhala pa dziko lapansi adzapembedza chirombocho, aliyense amene chilengedwere cha dziko lapansi dzina lake silinalembedwe mʼbuku la amoyo la Mwana Wankhosa anaphedwa uja.

Iye amene ali ndi makutu, amve.

10 “Woyenera kupita ku ukapolo,
    adzapita ku ukapolo.
Woyenera kufa ndi lupanga,
    adzafa ndi lupanga.”

Pamenepa kwa anthu a Mulungu pakufunika kupirira ndi kukhulupirika.

Chirombo Chotuluka Mʼnthaka

11 Kenaka ndinaona chirombo china chikutuluka mʼnthaka. Chinali ndi nyanga ziwiri ngati mwana wankhosa koma kuyankhula kwake ngati chinjoka. 12 Chinalamulira ndi mphamvu zonse za chirombo choyamba chija, ndipo chinachititsa kuti dziko lapansi ndi anthu okhalamo alambire chirombo choyamba chija, chimene bala lake losati nʼkupola linali litapola. 13 Ndipo chinachita zizindikiro zazikulu zodabwitsa, mpaka kumagwetsa moto pa dziko lapansi kuchokera kumwamba anthu akuona. 14 Chifukwa cha zizindikiro zimene chinaloledwa kuchita mʼmalo mwa chirombo choyamba chija, chimene bala lake linapola, chinanyenga anthu okhala pa dziko lapansi. Chinalamula anthu kuti apange fano mopereka ulemu kwa chirombo chimene chinavulazidwa ndi lupanga, koma nʼkukhalabe ndi moyo. 15 Chirombo cha chiwirichi chinapatsidwa mphamvu zakupereka mpweya kwa fano la chirombo choyamba chija kuti liyankhule ndi kuphetsa aliyense wokana kupembedza fanolo. 16 Chinakakamiza aliyense, wamngʼono, wamkulu, wolemera, wosauka, mfulu ndi kapolo kuti alembedwe chizindikiro pa dzanja lamanja kapena pa mphumi. 17 Chinkachita zimenezi kuti wina aliyense asaloledwe kugula kapena kugulitsa kanthu ngati alibe chizindikiro chimenechi, chimene ndi dzina la chirombocho kapena nambala yotanthauza dzina lake.

18 Pano pafunika nzeru. Munthu amene ali ndi nzeru atanthauze nambala ya chirombocho, pakuti nambalayo ikutanthauza munthu. Nambala yake ndi 666.

The Beast out of the Sea

13 The dragon[a] stood on the shore of the sea. And I saw a beast coming out of the sea.(A) It had ten horns and seven heads,(B) with ten crowns on its horns, and on each head a blasphemous name.(C) The beast I saw resembled a leopard,(D) but had feet like those of a bear(E) and a mouth like that of a lion.(F) The dragon gave the beast his power and his throne and great authority.(G) One of the heads of the beast seemed to have had a fatal wound, but the fatal wound had been healed.(H) The whole world was filled with wonder(I) and followed the beast. People worshiped the dragon because he had given authority to the beast, and they also worshiped the beast and asked, “Who is like(J) the beast? Who can wage war against it?”

The beast was given a mouth to utter proud words and blasphemies(K) and to exercise its authority for forty-two months.(L) It opened its mouth to blaspheme God, and to slander his name and his dwelling place and those who live in heaven.(M) It was given power to wage war(N) against God’s holy people and to conquer them. And it was given authority over every tribe, people, language and nation.(O) All inhabitants of the earth(P) will worship the beast—all whose names have not been written in the Lamb’s book of life,(Q) the Lamb(R) who was slain from the creation of the world.[b](S)

Whoever has ears, let them hear.(T)

10 “If anyone is to go into captivity,
    into captivity they will go.
If anyone is to be killed[c] with the sword,
    with the sword they will be killed.”[d](U)

This calls for patient endurance and faithfulness(V) on the part of God’s people.(W)

The Beast out of the Earth

11 Then I saw a second beast, coming out of the earth.(X) It had two horns like a lamb, but it spoke like a dragon.(Y) 12 It exercised all the authority(Z) of the first beast on its behalf,(AA) and made the earth and its inhabitants worship the first beast,(AB) whose fatal wound had been healed.(AC) 13 And it performed great signs,(AD) even causing fire to come down from heaven(AE) to the earth in full view of the people. 14 Because of the signs(AF) it was given power to perform on behalf of the first beast, it deceived(AG) the inhabitants of the earth.(AH) It ordered them to set up an image in honor of the beast who was wounded by the sword and yet lived.(AI) 15 The second beast was given power to give breath to the image of the first beast, so that the image could speak and cause all who refused to worship(AJ) the image to be killed.(AK) 16 It also forced all people, great and small,(AL) rich and poor, free and slave, to receive a mark on their right hands or on their foreheads,(AM) 17 so that they could not buy or sell unless they had the mark,(AN) which is the name of the beast or the number of its name.(AO)

18 This calls for wisdom.(AP) Let the person who has insight calculate the number of the beast, for it is the number of a man.[e](AQ) That number is 666.

Footnotes

  1. Revelation 13:1 Some manuscripts And I
  2. Revelation 13:8 Or written from the creation of the world in the book of life belonging to the Lamb who was slain
  3. Revelation 13:10 Some manuscripts anyone kills
  4. Revelation 13:10 Jer. 15:2
  5. Revelation 13:18 Or is humanity’s number