Add parallel Print Page Options

Mayi ndi Chinjoka

12 Chizindikiro chachikulu chinaoneka kuthambo; mayi atavala dzuwa, mapazi ake ataponda mwezi, pamutu pake pali chipewa chaufumu chokhala ndi nyenyezi khumi ndi ziwiri. Mayiyo anali woyembekezera ndipo pa nthawi yake yochira analira mokuwa chifukwa cha ululu wakubala. Kenaka ku thambo kunaonekanso chizindikiro china; chinjoka chachikulu kwambiri, chofiira chomwe chinali ndi mitu isanu ndi iwiri ndi nyanga khumi; pamutu uliwonse chitavala chipewa chaufumu. Mchira wake unakokolola gawo limodzi la magawo atatu a nyenyezi kuzichotsa ku thambo ndi kuziponya pa dziko lapansi. Chinjoka chija chinadzayima patsogolo pa mayi uja amene anali pafupi kuberekayu kuti mwanayo akangobadwa chimudye. Mayiyo anabereka mwana wamwamuna amene adzalamulira anthu a mitundu ina yonse ndi ndodo yachitsulo. Ndipo mwanayo analandidwa ku dzanja la mayiyo ndi kupita naye kwa Mulungu ku mpando wake waufumu. Mayiyo anathawira ku chipululu ku malo kumene Mulungu anamukonzera, kumene akasamalidweko masiku 1,260.

Zitatero, kumwamba kunayambika nkhondo. Mikayeli ndi angelo ake kumenyana ndi chinjoka chija. Chinjokacho ndi angelo ake anabwezeranso. Koma analibe mphamvu ndipo anagonjetsedwa nathamangitsidwa kumwambako. Chinjoka chachikulu chija chinagwetsedwa pansi. Ichocho ndiye njoka yakalekale ija yotchedwa Mdierekezi kapena Satana, amene amasocheretsa anthu a pa dziko lonse lapansi. Chinaponyedwa pa dziko la pansi pamodzi ndi angelo ake.

10 Kenaka ndinamva mawu ofuwula kumwamba akunena kuti,

“Tsopano chipulumutso, mphamvu,
    ufumu wa Mulungu wathu
    ndi ulamuliro wa Khristu wake zabwera.
Pakuti woneneza abale athu uja,
    amene amangokhalira kuwaneneza pamaso pa Mulungu usana ndi usiku,
    wagwetsedwa pansi.
11 Abale athuwo anamugonjetsa
    ndi magazi a Mwana Wankhosa
    ndiponso mawu a umboni wawo.
Iwo anadzipereka kwathunthu,
    moti sanakonde miyoyo yawo.
12 Choncho, kondwerani, inu dziko lakumwamba
    ndi onse okhala kumeneko!
Koma tsoka dziko lapansi ndi nyanja
    chifukwa Mdierekezi wagwetsedwa kwa inu!
Iye wadzazidwa ndi ukali
    chifukwa akudziwa kuti nthawi yake ndi yochepa.”

13 Pamene chinjokacho chinaona kuti chagwetsedwa pa dziko lapansi, chinayamba kuthamangitsa mayi uja amene anali atabala mwana wamwamunayu. 14 Mayiyo anapatsidwa mapiko awiri a chiwombankhanga chachikulu kuti athawire ku malo ake aja a ku chipululu. Kumeneko adzasamalidwako zaka zitatu ndi theka kuti chinjoka chija chisamupeze. 15 Kenaka chinjoka chija chinalavulira mayiyo madzi ambiri ngati mtsinje, kuti madziwo amukokolole. 16 Koma dziko lapansi linamuthandiza mayiyo. Nthaka inatsekuka ndi kumeza mtsinje uja unachokera mʼkamwa mwa chinjokacho. 17 Pamenepo chinjokacho chinamupsera mtima mayiyo ndipo chinachoka kupita kukachita nkhondo ndi ana ena onse a mayiyo, ndiye kuti anthu amene anasunga malamulo a Mulungu ndi kuchitira umboni za Yesu.

18 Kenaka ndinaona chinjokacho chitayima mʼmbali mwa nyanja.

The Woman and the Dragon

12 A great sign(A) appeared in heaven:(B) a woman clothed with the sun, with the moon under her feet and a crown of twelve stars(C) on her head. She was pregnant and cried out in pain(D) as she was about to give birth. Then another sign appeared in heaven:(E) an enormous red dragon(F) with seven heads(G) and ten horns(H) and seven crowns(I) on its heads. Its tail swept a third(J) of the stars out of the sky and flung them to the earth.(K) The dragon stood in front of the woman who was about to give birth, so that it might devour her child(L) the moment he was born. She gave birth to a son, a male child, who “will rule all the nations with an iron scepter.”[a](M) And her child was snatched up(N) to God and to his throne. The woman fled into the wilderness to a place prepared for her by God, where she might be taken care of for 1,260 days.(O)

Then war broke out in heaven. Michael(P) and his angels fought against the dragon,(Q) and the dragon and his angels(R) fought back. But he was not strong enough, and they lost their place in heaven. The great dragon was hurled down—that ancient serpent(S) called the devil,(T) or Satan,(U) who leads the whole world astray.(V) He was hurled to the earth,(W) and his angels with him.

10 Then I heard a loud voice in heaven(X) say:

“Now have come the salvation(Y) and the power
    and the kingdom of our God,
    and the authority of his Messiah.
For the accuser of our brothers and sisters,(Z)
    who accuses them before our God day and night,
    has been hurled down.
11 They triumphed over(AA) him
    by the blood of the Lamb(AB)
    and by the word of their testimony;(AC)
they did not love their lives so much
    as to shrink from death.(AD)
12 Therefore rejoice, you heavens(AE)
    and you who dwell in them!
But woe(AF) to the earth and the sea,(AG)
    because the devil has gone down to you!
He is filled with fury,
    because he knows that his time is short.”

13 When the dragon(AH) saw that he had been hurled to the earth, he pursued the woman who had given birth to the male child.(AI) 14 The woman was given the two wings of a great eagle,(AJ) so that she might fly to the place prepared for her in the wilderness, where she would be taken care of for a time, times and half a time,(AK) out of the serpent’s reach. 15 Then from his mouth the serpent(AL) spewed water like a river, to overtake the woman and sweep her away with the torrent. 16 But the earth helped the woman by opening its mouth and swallowing the river that the dragon had spewed out of his mouth. 17 Then the dragon was enraged at the woman and went off to wage war(AM) against the rest of her offspring(AN)—those who keep God’s commands(AO) and hold fast their testimony about Jesus.(AP)

Footnotes

  1. Revelation 12:5 Psalm 2:9