Add parallel Print Page Options

Mboni Ziwiri

11 Ndinapatsidwa bango longa ndodo yoyezera ndipo ndinawuzidwa kuti, “Pita, kayeze Nyumba ya Mulungu ndi guwa lansembe, ndipo ukawerenge anthu opembedza mʼNyumbamo. Koma bwalo lakunja ulisiye, usaliyeze chifukwa linaperekedwa kwa a mitundu ina. Iwo adzawupondereza mzinda woyerawo kwa miyezi 42. Ndipo ndidzapereka mphamvu kwa mboni zanga ziwiri, zitavala ziguduli, ndipo kwa masiku 1,260 zidzakhala zikulalikira.” Mboni ziwirizo ndi mitengo iwiri ya olivi ndi zoyikapo nyale ziwiri zija zimene zili pamaso pa Ambuye wa dziko lapansi. Ngati wina atafuna kuzipweteka mbonizo, moto umatuluka mʼkamwa mwawo ndikuwononga adani awo. Mbonizo zili ndi mphamvu yomanga mvula kuti isagwe pa nthawi imene akulalikirayo; ndipo zili ndi mphamvu yosanduliza madzi kukhala magazi ndi yokantha dziko lapansi ndi miliri ya mitundumitundu nthawi iliyonse imene zingafune.

Tsono zikadzatsiriza umboni wawowo, chirombo chotuluka mʼChidzenje chakuya chija chidzachita nawo nkhondo nʼkuzigonjetsa mpaka kuzipha. Mitembo yawo idzakhala ili gone pabwalo la mu mzinda waukulu umene mozimbayitsa umatchedwa Sodomu ndi Igupto, kumenenso Ambuye wawo anapachikidwako. Kwa masiku atatu ndi theka, anthu ochokera ku mtundu uliwonse, fuko lililonse, chiyankhulo chilichonse ndi dziko lililonse, azidzayangʼanitsitsa mitembo yawoyo koma adzakana kuyikwirira. 10 Anthu okhala pa dziko lapansi adzasangalala nazo zimenezi. Adzachita chikondwerero ndi kutumizirana mphatso, chifukwa aneneri awiri amenewa ankasautsa anthu okhala pa dziko lapansi.

11 Koma patapita masiku atatu ndi theka aja, mpweya wopatsa moyo wochoka kwa Mulungu unalowa mwa aneneriwo, ndipo anayimirira, ndipo amene anawaona anachita mantha aakulu. 12 Kenaka aneneri aja anamva mawu ofuwula ochokera kumwamba owawuza kuti, “Bwerani kuno.” Ndipo anapitadi kumwamba mu mtambo adani awo aja akuwaona.

13 Nthawi yomweyo panachitika chivomerezi choopsa mwakuti chigawo chimodzi cha magawo khumi a mzinda chinagwa. Anthu 7,000 anaphedwa ndi chivomerezicho, ndipo opulumukawo anachita mantha kwambiri nayamba kutamanda Mulungu wakumwamba.

14 Tsoka lachiwiri lapita; koma tsoka lachitatu likubwera posachedwapa.

Lipenga Lachisanu ndi Chiwiri

15 Mngelo wachisanu ndi chiwiri anawomba lipenga lake, ndipo kumwamba kunamveka mawu ofuwula amene anati,

“Ufumu wa dziko lapansi uli
    mʼmanja mwa Ambuye athu ndi Khristu wake uja,
    ndipo adzalamulira mpaka muyaya.”

16 Ndipo akuluakulu 24 aja okhala pa mipando yawo yaufumu pamaso pa Mulungu, anadzigwetsa chafufumimba napembedza Mulungu 17 Iwo anati,

“Ife tikuyamika Inu Ambuye Mulungu Wamphamvuzonse,
    amene mulipo ndipo munalipo,
chifukwa mwaonetsa mphamvu yanu yayikulu,
    ndipo mwayamba kulamulira.
18 A mitundu ina anapsa mtima;
    koma yafika nthawi yoonetsa mkwiyo.
Nthawi yakwana yoweruza anthu akufa,
    yopereka mphotho kwa atumiki anu, aneneri,
anthu oyera mtima anu ndi amene amaopa dzina lanu,
    wamngʼono pamodzi ndi wamkulu yemwe.
Yafika nthawi yowononga amene awononga dziko lapansi.”

19 Pamenepo anatsekula Nyumba ya Mulungu kumwamba ndipo mʼkati mwake munaoneka Bokosi la Chipangano. Kenaka kunachita mphenzi, phokoso, mabingu, chivomerezi ndipo kunachita mkuntho wamatalala akuluakulu.

The Two Witnesses

11 I was given a reed like a measuring rod(A) and was told, “Go and measure the temple of God and the altar, with its worshipers. But exclude the outer court;(B) do not measure it, because it has been given to the Gentiles.(C) They will trample on the holy city(D) for 42 months.(E) And I will appoint my two witnesses,(F) and they will prophesy for 1,260 days,(G) clothed in sackcloth.”(H) They are “the two olive trees”(I) and the two lampstands, and “they stand before the Lord of the earth.”[a](J) If anyone tries to harm them, fire comes from their mouths and devours their enemies.(K) This is how anyone who wants to harm them must die.(L) They have power to shut up the heavens(M) so that it will not rain during the time they are prophesying;(N) and they have power to turn the waters into blood(O) and to strike the earth with every kind of plague as often as they want.

Now when they have finished their testimony, the beast(P) that comes up from the Abyss(Q) will attack them,(R) and overpower and kill them. Their bodies will lie in the public square of the great city(S)—which is figuratively called Sodom(T) and Egypt—where also their Lord was crucified.(U) For three and a half days some from every people, tribe, language and nation(V) will gaze on their bodies and refuse them burial.(W) 10 The inhabitants of the earth(X) will gloat over them and will celebrate by sending each other gifts,(Y) because these two prophets had tormented those who live on the earth.

11 But after the three and a half days(Z) the breath[b] of life from God entered them,(AA) and they stood on their feet, and terror struck those who saw them. 12 Then they heard a loud voice from heaven saying to them, “Come up here.”(AB) And they went up to heaven in a cloud,(AC) while their enemies looked on.

13 At that very hour there was a severe earthquake(AD) and a tenth of the city collapsed. Seven thousand people were killed in the earthquake, and the survivors were terrified and gave glory(AE) to the God of heaven.(AF)

14 The second woe has passed; the third woe is coming soon.(AG)

The Seventh Trumpet

15 The seventh angel sounded his trumpet,(AH) and there were loud voices(AI) in heaven, which said:

“The kingdom of the world has become
    the kingdom of our Lord and of his Messiah,(AJ)
    and he will reign for ever and ever.”(AK)

16 And the twenty-four elders,(AL) who were seated on their thrones before God, fell on their faces(AM) and worshiped God, 17 saying:

“We give thanks(AN) to you, Lord God Almighty,(AO)
    the One who is and who was,(AP)
because you have taken your great power
    and have begun to reign.(AQ)
18 The nations were angry,(AR)
    and your wrath has come.
The time has come for judging the dead,(AS)
    and for rewarding your servants the prophets(AT)
and your people who revere your name,
    both great and small(AU)
and for destroying those who destroy the earth.”

19 Then God’s temple(AV) in heaven was opened, and within his temple was seen the ark of his covenant.(AW) And there came flashes of lightning, rumblings, peals of thunder,(AX) an earthquake and a severe hailstorm.(AY)

Footnotes

  1. Revelation 11:4 See Zech. 4:3,11,14.
  2. Revelation 11:11 Or Spirit (see Ezek. 37:5,14)