Add parallel Print Page Options

Mngelo ndi Kabuku

10 Kenaka ndinaona mngelo wina wamphamvu akutsika kuchokera kumwamba. Anavala mtambo ndipo anali ndi utawaleza pamutu pake. Nkhope yake inali ngati dzuwa, ndipo miyendo yake inali ngati mizati yamoto. Mʼdzanja lake munali kabuku kakangʼono kotsekulidwa. Phazi lake lamanja linaponda mʼnyanja ndipo phazi lake lamanzere linaponda pa mtunda. Mngeloyo anafuwula kwambiri ngati kubangula kwa mkango. Atangofuwula, kunamveka kugunda kwa mabingu asanu ndi awiri. Mabingu asanu ndi awiriwo atangogunda, ine ndinkati ndizilemba; koma ndinamva mawu kuchokera kumwamba kuti, “Zisunge mu mtima zimene mabingu asanu ndi awiriwo anena ndipo usazilembe.”

Kenaka mngelo amene ndinamuona ataponda mʼnyanja ndi ku mtunda uja, anakweza dzanja lake lamanja kumwamba. Mngeloyo analumbira mʼdzina la Iye wokhala ndi moyo mpaka muyaya, amene analenga kumwamba ndi zonse zili kumeneko, dziko lapansi ndi zonse zili mʼmenemo, nyanja ndi zonse zili mʼmenemo, nati, “Pasakhalenso zochedwa tsopano! Koma patsala pangʼono kuti mngelo wachisanu ndi chiwiri uja awombe lipenga lake, chinsinsi cha Mulungu chidzachitika monga momwe analengezera kwa atumiki ake, aneneri.”

Pamenepo mawu amene ndinamva kuchokera kumwamba aja, anandiyankhulanso, anati, “Pita katenge buku lotsekulidwalo mʼdzanja la mngelo amene waponda pa nyanja ndi pa mtundayo.”

Choncho ndinapita kwa mngeloyo ndipo ndinamupempha kuti andipatse kabukuko. Iye anati, “Tenga, idya. Mʼmimba mwako kaziwawa koma mʼkamwa mwako kazizuna ngati uchi.” 10 Ndinatenga kabukuko mʼdzanja la mngeloyo ndipo ndinadyadi. Mʼkamwa mwanga kankazuna ngati uchi, koma nditakameza, mʼmimbamu munkawawa. 11 Ndipo anandiwuza kuti, “Iwe uyenera kulalikiranso za mitundu yambiri ya anthu, za mayiko, ziyankhulo ndi za mafumu.”

The Angel and the Little Scroll

10 Then I saw another mighty angel(A) coming down from heaven.(B) He was robed in a cloud, with a rainbow(C) above his head; his face was like the sun,(D) and his legs were like fiery pillars.(E) He was holding a little scroll,(F) which lay open in his hand. He planted his right foot on the sea and his left foot on the land,(G) and he gave a loud shout like the roar of a lion.(H) When he shouted, the voices of the seven thunders(I) spoke. And when the seven thunders spoke, I was about to write;(J) but I heard a voice from heaven(K) say, “Seal up what the seven thunders have said and do not write it down.”(L)

Then the angel I had seen standing on the sea and on the land(M) raised his right hand to heaven.(N) And he swore(O) by him who lives for ever and ever,(P) who created the heavens and all that is in them, the earth and all that is in it, and the sea and all that is in it,(Q) and said, “There will be no more delay!(R) But in the days when the seventh angel is about to sound his trumpet,(S) the mystery(T) of God will be accomplished, just as he announced to his servants the prophets.”(U)

Then the voice that I had heard from heaven(V) spoke to me once more: “Go, take the scroll(W) that lies open in the hand of the angel who is standing on the sea and on the land.”

So I went to the angel and asked him to give me the little scroll. He said to me, “Take it and eat it. It will turn your stomach sour, but ‘in your mouth it will be as sweet as honey.’[a](X) 10 I took the little scroll from the angel’s hand and ate it. It tasted as sweet as honey in my mouth,(Y) but when I had eaten it, my stomach turned sour. 11 Then I was told, “You must prophesy(Z) again about many peoples, nations, languages and kings.”(AA)

Footnotes

  1. Revelation 10:9 Ezek. 3:3