Add parallel Print Page Options

Israeli Adzawonongedwa

Ine ndinaona Ambuye atayima pambali pa guwa lansembe, ndipo anati:

“Kantha mitu ya nsanamira
    kuti ziwundo za nyumba zigwedezeke.
Muzigwetsere pa mitu ya anthu onse,
    onse amene atsalira ndidzawapha ndi lupanga.
Palibe ndi mmodzi yemwe amene adzathawe,
    palibe amene adzapulumuke.
Ngakhale atakumba pansi mpaka ku malo a anthu akufa,
    dzanja langa lidzawatulutsa kumeneko.
Ngakhale atakwera kumwamba
    Ine ndidzawatsakamutsa kumeneko.
Ngakhale atakabisala pamwamba pa phiri la Karimeli,
    Ine ndidzawasaka kumeneko ndi kuwagwira.
Ngakhale atakabisala pansi pa nyanja yayikulu,
    ndidzalamula njoka kuti iwalume kumeneko.
Ngakhale adani awo awakusire ku ukapolo,
    ndidzalamula lupanga kuti liwaphe kumeneko.
Ndidzawayangʼanitsitsa
    kuti zoyipa ziwagwere; osati zabwino.”

Ambuye Yehova Wamphamvuzonse
    amene amakhudza dziko lapansi ndipo dzikolo limasungunuka,
    onse amene amakhala mʼmenemo amalira.
Dziko lonse lidzadzaza ngati mtsinje wa Nailo,
    kenaka nʼkuphwera ngati mtsinje wa ku Igupto.
Iye amene amamanga malo ake okhalamo kumwamba,
    ndi kuyika maziko ake pa dziko lapansi,
Iye amene amayitana madzi a ku nyanja
    ndikuwakhuthulira pa dziko lapansi,
    dzina lake ndiye Yehova.

“Kodi kwa Ine, inu Aisraeli, simuli
    chimodzimodzi ndi Akusi?”
            Akutero Yehova.
“Kodi sindine amene ndinatulutsa Israeli ku Igupto,
    Afilisti ku Kafitori
    ndi Aaramu ku Kiri?

“Taonani, maso a Ambuye Yehova
    ali pa ufumu wochimwawu.
Ndidzawufafaniza
    pa dziko lapansi.
Komabe sindidzawononga kotheratu
    nyumba ya Yakobo,”
            akutero Yehova.
“Pakuti ndidzalamula,
    ndipo ndidzagwedeza nyumba ya Israeli
    pakati pa mitundu yonse ya anthu
monga momwe amasefera ufa mʼsefa,
    koma palibe nʼkamwala kamodzi komwe kamene kadzagwe pansi.
10 Anthu onse ochimwa pakati pa anthu anga
    adzaphedwa ndi lupanga,
onse amene amanena kuti,
    ‘Tsoka silidzatigwera ife kapena kutiwononga.’

Kubwezeretsedwa kwa Israeli

11 “Tsiku limenelo ndidzabwezeretsa
    nyumba ya Davide imene inagwa.
Ndidzakonzanso malo amene anagumuka,
    ndi kuyimanganso
    monga inalili poyamba,
12 kuti adzatengenso otsala a Edomu
    ndi mitundu yonse imene imatchedwa ndi dzina langa,”
            akutero Yehova amene adzachita zinthu izi.

13 Yehova akunena kuti

“Nthawi ikubwera pamene mlimi wotipula adzapyola wokolola
    ndipo woponda mphesa adzapyola wodzala mbewu.
Mapiri adzachucha vinyo watsopano
    ndi kuyenderera pa zitunda zonse.
14 Ndidzawabwezeranso pabwino anthu anga Aisraeli;
    mizinda imene inali mabwinja idzamangidwanso ndipo azidzakhalamo.
Adzalima minda ya mpesa ndipo adzamwa vinyo wake;
    adzalima minda ndipo adzadya zipatso zake.
15 Ndidzakhazika Aisraeli mʼdziko mwawo,
    ndipo sadzachotsedwamonso mʼdziko
    limene Ine ndawapatsa,”

            akutero Yehova Mulungu wako.

Israel to Be Destroyed

I saw the Lord standing by the altar, and he said:

“Strike the tops of the pillars
    so that the thresholds shake.
Bring them down on the heads(A) of all the people;
    those who are left I will kill with the sword.
Not one will get away,
    none will escape.(B)
Though they dig down to the depths below,(C)
    from there my hand will take them.
Though they climb up to the heavens above,(D)
    from there I will bring them down.(E)
Though they hide themselves on the top of Carmel,(F)
    there I will hunt them down and seize them.(G)
Though they hide from my eyes at the bottom of the sea,(H)
    there I will command the serpent(I) to bite them.(J)
Though they are driven into exile by their enemies,
    there I will command the sword(K) to slay them.

“I will keep my eye on them
    for harm(L) and not for good.(M)(N)

The Lord, the Lord Almighty—
he touches the earth and it melts,(O)
    and all who live in it mourn;
the whole land rises like the Nile,
    then sinks like the river of Egypt;(P)
he builds his lofty palace[a](Q) in the heavens
    and sets its foundation[b] on the earth;
he calls for the waters of the sea
    and pours them out over the face of the land—
    the Lord is his name.(R)

“Are not you Israelites
    the same to me as the Cushites[c]?”(S)
declares the Lord.
“Did I not bring Israel up from Egypt,
    the Philistines(T) from Caphtor[d](U)
    and the Arameans from Kir?(V)

“Surely the eyes of the Sovereign Lord
    are on the sinful kingdom.
I will destroy(W) it
    from the face of the earth.
Yet I will not totally destroy
    the descendants of Jacob,”
declares the Lord.(X)
“For I will give the command,
    and I will shake the people of Israel
    among all the nations
as grain(Y) is shaken in a sieve,(Z)
    and not a pebble will reach the ground.(AA)
10 All the sinners among my people
    will die by the sword,(AB)
all those who say,
    ‘Disaster will not overtake or meet us.’(AC)

Israel’s Restoration

11 “In that day

“I will restore David’s(AD) fallen shelter(AE)
    I will repair its broken walls
    and restore its ruins(AF)
    and will rebuild it as it used to be,(AG)
12 so that they may possess the remnant of Edom(AH)
    and all the nations that bear my name,[e](AI)
declares the Lord, who will do these things.(AJ)

13 “The days are coming,”(AK) declares the Lord,

“when the reaper(AL) will be overtaken by the plowman(AM)
    and the planter by the one treading(AN) grapes.
New wine(AO) will drip from the mountains
    and flow from all the hills,(AP)
14     and I will bring(AQ) my people Israel back from exile.[f](AR)

“They will rebuild the ruined cities(AS) and live in them.
    They will plant vineyards(AT) and drink their wine;
    they will make gardens and eat their fruit.(AU)
15 I will plant(AV) Israel in their own land,(AW)
    never again to be uprooted(AX)
    from the land I have given them,”(AY)

says the Lord your God.(AZ)

Footnotes

  1. Amos 9:6 The meaning of the Hebrew for this phrase is uncertain.
  2. Amos 9:6 The meaning of the Hebrew for this word is uncertain.
  3. Amos 9:7 That is, people from the upper Nile region
  4. Amos 9:7 That is, Crete
  5. Amos 9:12 Hebrew; Septuagint so that the remnant of people / and all the nations that bear my name may seek me
  6. Amos 9:14 Or will restore the fortunes of my people Israel