Add parallel Print Page Options

Yehova akuti,

“Chifukwa anthu a ku Mowabu akunka nachimwirachimwira,
    Ine sindileka kuwalanga.
Popeza anatentha mafupa a mfumu ya ku Edomu,
    mpaka kuwasandutsa phulusa,
Ine ndidzatumiza moto pa Mowabu,
    umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Keriyoti.
Mowabu adzafera pakati pa nkhondo yoopsa,
    mʼkati mwa mfuwu wa nkhondo ndi kuliza malipenga.
Ndidzawononga wolamulira wake
    ndi kupha akuluakulu onse amene ali pamodzi ndi iye,”
            akutero Yehova.

Yehova akuti,

“Chifukwa anthu a ku Yuda akunka nachimwirachimwira,
    Ine sindileka kuwalanga.
Popeza iwo akana lamulo la Yehova
    ndipo sanasunge malangizo ake,
popeza asocheretsedwa ndi milungu yabodza,
    milungu imene makolo awo ankayitsatira,
Ine ndidzatumiza moto pa Yuda,
    umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Yerusalemu.”

Chilango cha Anthu a ku Israeli

Yehova akuti,

“Chifukwa anthu a ku Israeli akunka nachimwirachimwira,
    Ine sindileka kuwalanga.
Iwo amagulitsa anthu olungama ndi siliva,
    ndi osauka ndi nsapato.
Amapondereza anthu osauka
    ngati akuponda fumbi,
    ndipo sawaweruza mwachilungamo anthu oponderezedwa.
Abambo ndi mwana wawo amagonana ndi mtsikana mmodzi yemweyo,
    ndipo potero amanyozetsa dzina langa loyera.
Anthuwo amakagonana mʼmbali mwa guwa lililonse la nsembe
    pa zovala zimene anatenga ngati chikole.
Mʼnyumba ya mulungu wawo
    amamweramo vinyo amene analipiritsa anthu pa milandu.

“Ine ndinawononga Aamori pamaso pawo,
    ngakhale iwo anali anthu ataliatali ngati mikungudza
    ndiponso amphamvu ngati mitengo ya thundu.
Ndinawononga zipatso zawo
    ndiponso mizu yawo.

10 “Ine ndinakutulutsani ku Igupto,
    ndipo ndinakutsogolerani mʼchipululu kwa zaka makumi anayi,
    kudzakupatsani dziko la Aamori.
11 Ine ndinawutsanso ena mwa ana ako kuti akhale aneneri,
    ndi ena mwa anyamata ako kuti akhale anaziri.
Kodi si choncho, inu Aisraeli?”
            akutero Yehova.
12 “Koma inu munawamwetsa vinyo anaziri aja,
    ndipo munalamula aneneri kuti asanenere.

13 “Tsono Ine ndidzakupsinjani
    monga imapsinjikira ngolo imene yadzaza ndi tirigu.
14 Munthu waliwiro sadzatha kuthawa,
    munthu wamphamvu sadzakhalanso ndi nyonga,
    wankhondo sadzapulumutsa moyo wake.
15 Munthu wa uta sadzalimbika,
    msilikali wothamanga kwambiri sadzapulumuka,
    ndipo wokwera pa akavalo sadzapulumutsa moyo wake.
16 Ngakhale asilikali olimba mtima kwambiri
    adzathawa ali maliseche pa tsikulo,”
            akutero Yehova.

This is what the Lord says:

“For three sins of Moab,(A)
    even for four, I will not relent.
Because he burned to ashes(B)
    the bones of Edom’s king,
I will send fire on Moab
    that will consume the fortresses of Kerioth.[a](C)
Moab will go down in great tumult
    amid war cries(D) and the blast of the trumpet.(E)
I will destroy her ruler(F)
    and kill all her officials with him,”(G)
says the Lord.(H)

This is what the Lord says:

“For three sins of Judah,(I)
    even for four, I will not relent.
Because they have rejected the law(J) of the Lord
    and have not kept his decrees,(K)
because they have been led astray(L) by false gods,[b](M)
    the gods[c] their ancestors followed,(N)
I will send fire(O) on Judah
    that will consume the fortresses(P) of Jerusalem.(Q)

Judgment on Israel

This is what the Lord says:

“For three sins of Israel,
    even for four, I will not relent.(R)
They sell the innocent for silver,
    and the needy for a pair of sandals.(S)
They trample on the heads of the poor
    as on the dust of the ground
    and deny justice to the oppressed.
Father and son use the same girl
    and so profane my holy name.(T)
They lie down beside every altar
    on garments taken in pledge.(U)
In the house of their god
    they drink wine(V) taken as fines.(W)

“Yet I destroyed the Amorites(X) before them,
    though they were tall(Y) as the cedars
    and strong as the oaks.(Z)
I destroyed their fruit above
    and their roots(AA) below.
10 I brought you up out of Egypt(AB)
    and led(AC) you forty years in the wilderness(AD)
    to give you the land of the Amorites.(AE)

11 “I also raised up prophets(AF) from among your children
    and Nazirites(AG) from among your youths.
Is this not true, people of Israel?”
declares the Lord.
12 “But you made the Nazirites drink wine
    and commanded the prophets not to prophesy.(AH)

13 “Now then, I will crush you
    as a cart crushes when loaded with grain.(AI)
14 The swift will not escape,(AJ)
    the strong(AK) will not muster their strength,
    and the warrior will not save his life.(AL)
15 The archer(AM) will not stand his ground,
    the fleet-footed soldier will not get away,
    and the horseman(AN) will not save his life.(AO)
16 Even the bravest warriors(AP)
    will flee naked on that day,”
declares the Lord.

Footnotes

  1. Amos 2:2 Or of her cities
  2. Amos 2:4 Or by lies
  3. Amos 2:4 Or lies