Add parallel Print Page Options

Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu mwachifuniro cha Mulungu, ndi Timoteyo mʼbale wathu.

Kulembera abale oyera mtima ndi okhulupirira a ku Kolose mwa Khristu.

Chisomo ndi mtendere kwa inu zochokera kwa Mulungu Atate athu.

Kuyamika ndi Pemphero

Timayamika Mulungu Atate wa Ambuye athu Yesu Khristu, nthawi zonse pamene tikukupemphererani. Timayamika chifukwa tinamva za chikhulupiriro chanu mwa Khristu Yesu ndi za chikondi chanu pa oyera mtima onse. Chikhulupiriro ndi chikondi, gwero lake ndi chiyembekezo chomwe muli nacho chodzalandira zimene anakusungirani kumwamba. Munamva kale za zimenezi kudzera mʼmawu a choonadi, Uthenga Wabwino umene unafika kwa inu. Pa dziko lonse lapansi Uthenga Wabwino ukubereka chipatso ndi kukula monga momwe zakhala zikuchitikira pakati panu kuyambira tsiku limene munawumva ndi kuzindikira chisomo cha Mulungu mu choonadi chonse. Inu munaphunzira zimenezi kuchokera kwa Epafra, mtumiki mnzathu wokondedwa, amene ndi mtumiki wokhulupirika wa Khristu mʼmalo mwathu. Iye anatiwuza za chikondi chanu chimene Mzimu anakupatsani.

Chifukwa cha ichi, kuyambira tsiku limene tinamva za inu, sitinasiye kukupemphererani ndi kumupempha Mulungu kuti akudzazeni ndi chidziwitso cha chifuniro chake kudzera mu nzeru yonse yauzimu ndi kumvetsetsa. 10 Ndipo tikupempherera zimenezi ndi cholinga chakuti inu mukhale moyo oyenera Ambuye ndi kumukondweretsa mʼnjira zonse. Kubereka chipatso pa ntchito iliyonse yabwino, ndi kukula mʼchidziwitso cha Mulungu. 11 Timapempheranso kuti Mulungu akulimbikitseni ndi mphamvu yake yonse ya ulemerero wake, kuti muzipirira zonse ndi mitima yofatsa ndi ya chimwemwe 12 ndi kuyamika Atate nthawi zonse, amene wakuyenerezani kuti mulandire nawo chuma cha oyera mtima mu ufumu wa kuwunika. 13 Pakuti Iye anatipulumutsa ku ulamuliro wa mdima ndi kutibweretsa mu ufumu wa Mwana wake wokondedwa. 14 Mwa Iyeyu ife tinawomboledwa ndi kukhululukidwa machimo.

Kupambana Koposa kwa Khristu

15 Mwanayu ndiye chithunzi cha Mulungu wosaonekayo. Iye ndiye Mwana wake woyamba kubadwa ndi wolamulira zolengedwa zonse. 16 Pakuti zinthu zonse zinalengedwa kudzera mwa Iye. Zinthu zakumwamba ndi za pa dziko lapansi, zooneka ndi zosaoneka, maufumu, akuluakulu, aulamuliro ndi amphamvu. Zinthu zonse zinalengedwa kudzera mwa Iye ndipo anazilengera Iyeyo. 17 Iyeyo analipo zinthu zonse zisanalengedwe ndipo zinthu zonse zimamangika pamodzi mwa Iye. 18 Iye ndiyenso mutu wa thupi, limene ndi mpingo. Iye ndiye chiyambi chake, woyamba kuuka kwa akufa, kuti Iyeyo akhale wopambana zonse. 19 Pakuti kunamukomera Mulungu kuti umulungu wake wonse ukhalemo mwa Khristu. 20 Ndipo kudzera mwa Iye Mulungu ayanjanitsenso zinthu zonse ndi Iye mwini, zinthu za pa dziko lapansi, kapena zinthu za kumwamba. Iye anachita mtendere kudzera mʼmagazi ake, wokhetsedwa pa mtanda.

21 Kale inu munali kutali ndi Mulungu ndipo munali adani a Mulungu mʼmaganizo mwanu chifukwa cha khalidwe lanu loyipa. 22 Koma tsopano Iye anakuyanjanitsani mʼthupi la Khristu kudzera mu imfa kuti akuperekeni pamaso pake oyera, opanda banga ndi opanda chotsutsidwa nacho 23 ngati mupitirirabe kukhala mʼchikhulupiriro chanu, okhazikika ndi olimba, osasunthidwa kuchoka pa chiyembekezo chimene munachigwira mu Uthenga Wabwino. Uwu ndi Uthenga Wabwino umene munawumva, umene wakhala ukulalikidwa kwa olengedwa onse a pansi pa thambo, ndi umenenso, ine Paulo ndinakhala mtumiki wake.

Utumiki wa Paulo ku Mpingo

24 Tsopano ine ndikukondwa kuti ndinavutika chifukwa cha inu, ndipo ndikukwaniritsa mʼthupi langa zimene zikuperewera pa masautso a Khristu, chifukwa cha thupi lake, limene ndi Mpingo. 25 Ine ndakhala mtumiki wake mwa lamulo limene Mulungu anandipatsa kuti ndipereke Mawu a Mulungu athunthu, 26 chinsinsi chimene chakhala chikubisika kwa nthawi ndi mibado, koma tsopano chawululidwa kwa oyera mtima. 27 Kwa iwo amene Mulungu anawasankha kuti awadziwitse pakati pa a mitundu ina, ulemerero wa chuma cha chinsinsi ichi, amene ndi Khristu mwa inu, chiyembekezo cha ulemerero.

28 Ife tikulalikira Khristu, kulangiza ndi kuphunzitsa aliyense mwa nzeru zonse kuti timupereke aliyense wangwiro mwa Khristu. 29 Ndi cholinga chimenechi, ine ndikugwira ntchito molimbika ndi mwamphamvu zonse zimene Iye anachita mwa ine.

Paul, an apostle(A) of Christ Jesus by the will of God,(B) and Timothy(C) our brother,

To God’s holy people in Colossae, the faithful brothers and sisters[a] in Christ:

Grace(D) and peace to you from God our Father.[b](E)

Thanksgiving and Prayer

We always thank God,(F) the Father of our Lord Jesus Christ, when we pray for you, because we have heard of your faith in Christ Jesus and of the love(G) you have for all God’s people(H) the faith and love that spring from the hope(I) stored up for you in heaven(J) and about which you have already heard in the true message(K) of the gospel that has come to you. In the same way, the gospel is bearing fruit(L) and growing throughout the whole world(M)—just as it has been doing among you since the day you heard it and truly understood God’s grace. You learned it from Epaphras,(N) our dear fellow servant,[c] who is a faithful minister(O) of Christ on our[d] behalf, and who also told us of your love in the Spirit.(P)

For this reason, since the day we heard about you,(Q) we have not stopped praying for you.(R) We continually ask God to fill you with the knowledge of his will(S) through all the wisdom and understanding that the Spirit gives,[e](T) 10 so that you may live a life worthy(U) of the Lord and please him(V) in every way: bearing fruit in every good work, growing in the knowledge of God,(W) 11 being strengthened with all power(X) according to his glorious might so that you may have great endurance and patience,(Y) 12 and giving joyful thanks to the Father,(Z) who has qualified you[f] to share in the inheritance(AA) of his holy people in the kingdom of light.(AB) 13 For he has rescued us from the dominion of darkness(AC) and brought us into the kingdom(AD) of the Son he loves,(AE) 14 in whom we have redemption,(AF) the forgiveness of sins.(AG)

The Supremacy of the Son of God

15 The Son is the image(AH) of the invisible God,(AI) the firstborn(AJ) over all creation. 16 For in him all things were created:(AK) things in heaven and on earth, visible and invisible, whether thrones or powers or rulers or authorities;(AL) all things have been created through him and for him.(AM) 17 He is before all things,(AN) and in him all things hold together. 18 And he is the head(AO) of the body, the church;(AP) he is the beginning and the firstborn(AQ) from among the dead,(AR) so that in everything he might have the supremacy. 19 For God was pleased(AS) to have all his fullness(AT) dwell in him, 20 and through him to reconcile(AU) to himself all things, whether things on earth or things in heaven,(AV) by making peace(AW) through his blood,(AX) shed on the cross.

21 Once you were alienated from God and were enemies(AY) in your minds(AZ) because of[g] your evil behavior. 22 But now he has reconciled(BA) you by Christ’s physical body(BB) through death to present you(BC) holy in his sight, without blemish and free from accusation(BD) 23 if you continue(BE) in your faith, established(BF) and firm, and do not move from the hope(BG) held out in the gospel. This is the gospel that you heard and that has been proclaimed to every creature under heaven,(BH) and of which I, Paul, have become a servant.(BI)

Paul’s Labor for the Church

24 Now I rejoice(BJ) in what I am suffering for you, and I fill up in my flesh what is still lacking in regard to Christ’s afflictions,(BK) for the sake of his body, which is the church.(BL) 25 I have become its servant(BM) by the commission God gave me(BN) to present to you the word of God(BO) in its fullness— 26 the mystery(BP) that has been kept hidden for ages and generations, but is now disclosed to the Lord’s people. 27 To them God has chosen to make known(BQ) among the Gentiles the glorious riches(BR) of this mystery, which is Christ in you,(BS) the hope of glory.

28 He is the one we proclaim, admonishing(BT) and teaching everyone with all wisdom,(BU) so that we may present everyone fully mature(BV) in Christ. 29 To this end I strenuously(BW) contend(BX) with all the energy Christ so powerfully works in me.(BY)

Footnotes

  1. Colossians 1:2 The Greek word for brothers and sisters (adelphoi) refers here to believers, both men and women, as part of God’s family; also in 4:15.
  2. Colossians 1:2 Some manuscripts Father and the Lord Jesus Christ
  3. Colossians 1:7 Or slave
  4. Colossians 1:7 Some manuscripts your
  5. Colossians 1:9 Or all spiritual wisdom and understanding
  6. Colossians 1:12 Some manuscripts us
  7. Colossians 1:21 Or minds, as shown by