Add parallel Print Page Options

Tsono tiyeni tisangoyima pa maphunziro oyambirira enieni a Khristu koma tipitirire kuti mukule msinkhu. Tisaphunzitsenso zinthu zomwe zili ngati maziko, monga za kutembenuka mtima kusiya ntchito zosapindulitsa pa moyo wosatha, za kukhulupirira Mulungu, za maubatizo, za kusanjika manja, za kuuka kwa akufa ndi za chiweruzo chotsiriza. Ndipo Mulungu akalola, tidzaterodi.

Nʼkosatheka kuwabwezanso anthu amene nthawi ina anawunikiridwa. Iwowa analawapo mphatso yochokera kumwamba, nʼkulandira nawo Mzimu Woyera. Analawa kukoma kwa mawu a Mulungu ndi mphamvu za nthawi ikubwera. Popeza anabwerera mʼmbuyo, nʼkosatheka kuti atembenukenso mtima chifukwa akupachikanso Mwana wa Mulungu ndi kumunyozetsa poyera.

Nthaka yolandira mvula kawirikawiri nʼkubala mbewu zopindulitsa oyilima, Mulungu amayidalitsa. Koma nthaka yobereka minga ndi nthula ndi yopanda phindu ndipo ili pafupi kutembereredwa. Matsiriziro ake idzatenthedwa mʼmoto.

Okondedwa anga, ngakhale tikuyankhula zimenezi, ife tikudziwa kuti muli nazo zinthu zabwino zomwe zimabwera pamodzi ndi chipulumutso. 10 Mulungu ndi wolungama, sangayiwale ntchito zanu ndi chikondi chanu chimene munamuonetsa pothandiza anthu ake monga mmene mukuchitirabe tsopano. 11 Ife tikufuna kuti aliyense wa inu aonetse changu chomwechi mpaka kumapeto, kuti zichitikedi zomwe mukuyembekezera. 12 Ife sitikufuna kuti inu mukhale aulesi, koma mutsatire anthu amene, pokhulupirira ndi kupirira, akulandira zimene zinalonjezedwa.

Kukhazikika kwa Malonjezo a Mulungu

13 Pamene Mulungu ankamulonjeza Abrahamu, popeza panalibe wamkulu womuposa, amene akanamutchula ndikulumbira mwa Iye, analumbira mwa Iye yekha kuti, 14 “Ine ndidzakudalitsa ndithu, ndipo ndidzakupatsa zidzukulu zambiri.” 15 Ndipo Abrahamu atayembekezera mofatsa, analandira zimene anamulonjezazo.

16 Anthu amalumbira mʼdzina la wina amene akuwaposa, ndipo lumbiro lotere limatsimikizira zomwe zayankhulidwa ndi kuthetsa mikangano yonse. 17 Momwemonso Mulungu pofuna kutsimikizira anthu amene adzalandire lonjezo, kuti Iye sangasinthe maganizo, anatsimikiza lonjezo lakelo ndi lumbiro. 18 Mulungu anachita zinthu ziwiri, lonjezo ndi lumbiro, zimene sizingathe kusintha ndipo Mulungu sangathe kunama. Choncho Mulungu akutilimbikitsa mtima ife amene tinathawira kwa Iye kuti tichigwiritsitse chiyembekezo chimene tinalandira. 19 Chiyembekezo chimenechi tili nacho ngati nangula wa moyo wathu. Nʼchokhazikika ndi chosagwedezeka ndipo chimalowa mʼkatikati mwa malo opatulika, kuseri kwa chinsalu chotchinga. 20 Yesu anatitsogolera kupita kumeneko, nalowako mʼmalo mwathu. Iye anasanduka Mkulu wa ansembe onse wamuyaya, monga mwa dongosolo la unsembe wa Melikizedeki.

Therefore let us move beyond(A) the elementary teachings(B) about Christ and be taken forward to maturity, not laying again the foundation of repentance from acts that lead to death,[a](C) and of faith in God, instruction about cleansing rites,[b](D) the laying on of hands,(E) the resurrection of the dead,(F) and eternal judgment. And God permitting,(G) we will do so.

It is impossible for those who have once been enlightened,(H) who have tasted the heavenly gift,(I) who have shared in the Holy Spirit,(J) who have tasted the goodness(K) of the word of God(L) and the powers of the coming age and who have fallen[c] away, to be brought back to repentance.(M) To their loss they are crucifying the Son of God(N) all over again and subjecting him to public disgrace. Land that drinks in the rain often falling on it and that produces a crop useful to those for whom it is farmed receives the blessing of God. But land that produces thorns and thistles is worthless and is in danger of being cursed.(O) In the end it will be burned.

Even though we speak like this, dear friends,(P) we are convinced of better things in your case—the things that have to do with salvation. 10 God is not unjust; he will not forget your work and the love you have shown him as you have helped his people and continue to help them.(Q) 11 We want each of you to show this same diligence to the very end, so that what you hope(R) for may be fully realized. 12 We do not want you to become lazy, but to imitate(S) those who through faith and patience(T) inherit what has been promised.(U)

The Certainty of God’s Promise

13 When God made his promise to Abraham, since there was no one greater for him to swear by, he swore by himself,(V) 14 saying, “I will surely bless you and give you many descendants.”[d](W) 15 And so after waiting patiently, Abraham received what was promised.(X)

16 People swear by someone greater than themselves, and the oath confirms what is said and puts an end to all argument.(Y) 17 Because God wanted to make the unchanging(Z) nature of his purpose very clear to the heirs of what was promised,(AA) he confirmed it with an oath. 18 God did this so that, by two unchangeable things in which it is impossible for God to lie,(AB) we who have fled to take hold of the hope(AC) set before us may be greatly encouraged. 19 We have this hope as an anchor for the soul, firm and secure. It enters the inner sanctuary behind the curtain,(AD) 20 where our forerunner, Jesus, has entered on our behalf.(AE) He has become a high priest(AF) forever, in the order of Melchizedek.(AG)

Footnotes

  1. Hebrews 6:1 Or from useless rituals
  2. Hebrews 6:2 Or about baptisms
  3. Hebrews 6:6 Or age, if they fall
  4. Hebrews 6:14 Gen. 22:17