Add parallel Print Page Options

Yesu ndi Wamkulu Kuposa Mose

Nʼchifukwa chake abale oyera mtima, amenenso munayitanidwa ndi kumwamba, lingalirani za Yesu amene ndi Mtumwi ndi Mkulu wa ansembe wa chikhulupiriro chimene timavomereza. Iye anali wokhulupirika kwa Mulungu amene anamupatsa udindowo, monga momwe Mose anali wokhulupirika mʼnyumba yonse ya Mulungu. Yesu anapezeka woyenera kulandira ulemu waukulu kuposa Mose, monga momwemonso womanga nyumba amalandira ulemu waukulu kuposa nyumbayo. Pakuti nyumba iliyonse imamangidwa ndi munthu wina, koma amene anapanga zonse ndi Mulungu. Mose anali wokhulupirika monga mtumiki mʼnyumba yonse ya Mulungu, kuchitira umboni zimene zidzayankhulidwe mʼtsogolo. Koma Khristu ndi wokhulupirika monga mwana pa nyumba ya Mulungu. Ndipo ndife nyumba yake ngati tipitirire kulimbika mtima ndi kunyadira zomwe tikuyembekerazo.

Chenjezo pa Kusakhulupirira

Tsono monga Mzimu Woyera akuti,

“Lero mukamva mawu ake,
    musawumitse mitima yanu
ngati munachitira pamene munawukira,
    pa nthawi yoyesedwa mʼchipululu.
Pamene makolo anu anandiputa ndi kundiyesa,
    ndipo kwa zaka makumi anayi anaona zimene Ine ndinachita.
10 Nʼchifukwa chake ndinawukwiyira mʼbadowo,
    ndipo Ine ndinati, ‘Nthawi zonse mitima yawo imasochera,
    ndipo iwo sadziwa njira zanga.’
11 Kotero Ine ndinalumbira nditakwiya kuti,
    ‘Iwo sadzalowa mu mpumulo wanga.’ ”

12 Abale samalani, kuti pasapezeke wina aliyense mwa inu wokhala ndi mtima woyipa ndi wosakhulupirira, womulekanitsa ndi Mulungu wamoyo. 13 Koma muzilimbikitsana tsiku ndi tsiku, ikanalipo nthawi imene imatchedwa kuti “Lero” kuti aliyense wa inu mtima wake usawumitsidwe ndi chinyengo cha tchimo. 14 Pakuti timakhala anzake a Khristu, ngati tigwiritsitsa mpaka potsiriza chitsimikizo chimene tinali nacho pachiyambi. 15 Monga kunanenedwa kuti,

“Lero ngati mumva mawu ake,
    musawumitse mitima yanu
    ngati momwe munachitira pamene munawukira.”

16 Nanga amene anamva ndi kuwukira anali ndani? Kodi si onse amene Mose anawatulutsa mu Igupto? 17 Nanga amene Mulungu anawakwiyira zaka makumi anayi anali ndani? Kodi si anthu amene anachimwa, amene mitembo yawo inatsala mʼchipululu muja? 18 Nanga Mulungu ankanena za ndani kuti sadzalowa mu mpumulo wake? Pajatu ankanena za anthu amene sanamvere aja. 19 Tsono ife tikuona kuti sanalowe chifukwa cha kusakhulupirika kwawo.

Jesus Greater Than Moses

Therefore, holy brothers and sisters,(A) who share in the heavenly calling,(B) fix your thoughts on Jesus, whom we acknowledge(C) as our apostle and high priest.(D) He was faithful to the one who appointed him, just as Moses was faithful in all God’s house.(E) Jesus has been found worthy of greater honor than Moses,(F) just as the builder of a house has greater honor than the house itself. For every house is built by someone, but God is the builder of everything.(G) “Moses was faithful as a servant(H) in all God’s house,”[a](I) bearing witness to what would be spoken by God in the future. But Christ is faithful as the Son(J) over God’s house. And we are his house,(K) if indeed we hold firmly(L) to our confidence and the hope(M) in which we glory.

Warning Against Unbelief

So, as the Holy Spirit says:(N)

“Today, if you hear his voice,
    do not harden your hearts(O)
as you did in the rebellion,
    during the time of testing in the wilderness,
where your ancestors tested and tried me,
    though for forty years they saw what I did.(P)
10 That is why I was angry with that generation;
    I said, ‘Their hearts are always going astray,
    and they have not known my ways.’
11 So I declared on oath in my anger,(Q)
    ‘They shall never enter my rest.’ (R)[b](S)

12 See to it, brothers and sisters, that none of you has a sinful, unbelieving heart that turns away from the living God.(T) 13 But encourage one another daily,(U) as long as it is called “Today,” so that none of you may be hardened by sin’s deceitfulness.(V) 14 We have come to share in Christ, if indeed we hold(W) our original conviction firmly to the very end.(X) 15 As has just been said:

“Today, if you hear his voice,
    do not harden your hearts
    as you did in the rebellion.”[c](Y)

16 Who were they who heard and rebelled? Were they not all those Moses led out of Egypt?(Z) 17 And with whom was he angry for forty years? Was it not with those who sinned, whose bodies perished in the wilderness?(AA) 18 And to whom did God swear that they would never enter his rest(AB) if not to those who disobeyed?(AC) 19 So we see that they were not able to enter, because of their unbelief.(AD)

Footnotes

  1. Hebrews 3:5 Num. 12:7
  2. Hebrews 3:11 Psalm 95:7-11
  3. Hebrews 3:15 Psalm 95:7,8