Add parallel Print Page Options

Pamaso pa Mulungu ndi pamaso pa Khristu Yesu, amene adzaweruza amoyo ndi akufa omwe pamene adzaonekera ndi ufumu wake, ndikukulamula kuti: Lalikira Mawu; khala wokonzeka pa nthawi yake, ngakhale pamene si pa nthawi yake. Konza zolakwa zawo, dzudzula ndipo limbikitsa moleza mtima kwambiri ndi malangizo osamalitsa. Pakuti idzafika nthawi imene anthu adzakana chiphunzitso choona. Mʼmalo mwake, chifukwa chokhumba kumva zowakomera zokha, adzasonkhanitsa aphunzitsi ambiri omawawuza zimene iwo akufuna kumva. Sadzafuna kumva choona koma adzafuna kumva nthano chabe. Koma iwe, khala tcheru nthawi zonse, pirira mʼzovuta, gwira ntchito ya mlaliki, gwira ntchito zonse za utumiki wako.

Pakuti moyo wanga wayamba kale kuthiridwa ngati nsembe, ndipo nthawi yakwana yoti ndinyamuke ulendo wanga. Ndamenya nkhondo yabwino, ndatsiriza bwino mpikisano wa liwiro ndipo ndasunga chikhulupiriro. Tsopano mphotho yanga ikundidikira imene ndi chipewa cha chilungamo, imene Ambuye, woweruza wolungama, adzandipatsa pa tsiku lijalo, osati ine ndekha komanso onse amene akufunitsitsa kubwera kwake.

Ndemanga ya Paulo

Uyesetse kubwera kuno msanga. 10 Paja Dema anandisiya chifukwa chokonda dziko lapansi lino, ndipo anapita ku Tesalonika. Kresike anapita ku Galatiya ndipo Tito anapita ku Dalimatiya. 11 Ndatsala ndi Luka yekha basi. Mutenge Marko ndipo ubwere naye kuno, chifukwa amandithandiza mu utumiki wanga. 12 Ndatumiza Tukiko ku Efeso. 13 Pobwera, unditengere chofunda pamwamba chimene ndinachisiya kwa Kupro ku Trowa. Unditengerenso mabuku anga, makamaka aja azikopawa.

14 Alekisandro, mmisiri wa zitsulo anandichitira zoyipa kwambiri. Ambuye adzamubwezera pa zimene anachita. 15 Iwenso ukhale naye tcheru chifukwa anatsutsa kwambiri uthenga wathu.

16 Podziteteza koyamba pa mlandu wanga, panalibe ndi mmodzi yemwe amene anandithandiza, koma aliyense anandithawa. Mulungu awakhululukire. 17 Koma Ambuye anayima nane limodzi, ndipo anandipatsa mphamvu, kuti kudzera mwa ine, uthenga ulalikidwe kwambiri, ndikuti anthu a mitundu ina amve. Ndipo ndinalanditsidwa mʼkamwa mwa mkango. 18 Ambuye adzandilanditsa ku chilichonse chofuna kundichita choyipa ndipo adzandisamalira bwino mpaka kundilowetsa chonse mu ufumu wake wakumwamba. Kwa Iye kukhale ulemerero mpaka muyaya.

Mawu Otsiriza

19 Pereka moni kwa Prisila ndi Akura pamodzi ndi banja lonse la Onesiforo. 20 Erasto anatsalira ku Korinto. Trofimo ndinamusiya akudwala ku Mileto. 21 Uyesetse kubwera kuno nthawi yozizira isanafike. Eubulo akupereka moni, ndiponso Pude, Lino, Klaudiya ndi abale onse nawonso akupereka moni.

22 Ambuye akhale ndi mzimu wako. Chisomo chikhale ndi inu nonse.

In the presence of God and of Christ Jesus, who will judge the living and the dead,(A) and in view of his appearing(B) and his kingdom, I give you this charge:(C) Preach(D) the word;(E) be prepared in season and out of season; correct, rebuke(F) and encourage(G)—with great patience and careful instruction. For the time will come when people will not put up with sound doctrine.(H) Instead, to suit their own desires, they will gather around them a great number of teachers to say what their itching ears want to hear.(I) They will turn their ears away from the truth and turn aside to myths.(J) But you, keep your head in all situations, endure hardship,(K) do the work of an evangelist,(L) discharge all the duties of your ministry.

For I am already being poured out like a drink offering,(M) and the time for my departure is near.(N) I have fought the good fight,(O) I have finished the race,(P) I have kept the faith. Now there is in store for me(Q) the crown of righteousness,(R) which the Lord, the righteous Judge, will award to me on that day(S)—and not only to me, but also to all who have longed for his appearing.(T)

Personal Remarks

Do your best to come to me quickly,(U) 10 for Demas,(V) because he loved this world,(W) has deserted me and has gone to Thessalonica.(X) Crescens has gone to Galatia,(Y) and Titus(Z) to Dalmatia. 11 Only Luke(AA) is with me.(AB) Get Mark(AC) and bring him with you, because he is helpful to me in my ministry. 12 I sent Tychicus(AD) to Ephesus.(AE) 13 When you come, bring the cloak that I left with Carpus at Troas,(AF) and my scrolls, especially the parchments.

14 Alexander(AG) the metalworker did me a great deal of harm. The Lord will repay him for what he has done.(AH) 15 You too should be on your guard against him, because he strongly opposed our message.

16 At my first defense, no one came to my support, but everyone deserted me. May it not be held against them.(AI) 17 But the Lord stood at my side(AJ) and gave me strength,(AK) so that through me the message might be fully proclaimed and all the Gentiles might hear it.(AL) And I was delivered from the lion’s mouth.(AM) 18 The Lord will rescue me from every evil attack(AN) and will bring me safely to his heavenly kingdom.(AO) To him be glory for ever and ever. Amen.(AP)

Final Greetings

19 Greet Priscilla[a] and Aquila(AQ) and the household of Onesiphorus.(AR) 20 Erastus(AS) stayed in Corinth, and I left Trophimus(AT) sick in Miletus.(AU) 21 Do your best to get here before winter.(AV) Eubulus greets you, and so do Pudens, Linus, Claudia and all the brothers and sisters.[b]

22 The Lord be with your spirit.(AW) Grace be with you all.(AX)

Footnotes

  1. 2 Timothy 4:19 Greek Prisca, a variant of Priscilla
  2. 2 Timothy 4:21 The Greek word for brothers and sisters (adelphoi) refers here to believers, both men and women, as part of God’s family.