Add parallel Print Page Options

Bokosi la Chipangano Libwera ku Yerusalemu

Davide anasonkhanitsanso pamodzi ankhondo 3,000 osankhidwa pakati pa Aisraeli. Iye pamodzi ndi ankhondo ake onse anapita ku Baalahi ku Yuda kukatenga Bokosi la Chipangano la Mulungu, limene limadziwika ndi Dzina lake, dzina la Yehova Wamphamvuzonse, amene amakhala pakati pa Akerubi amene ali pa Bokosi la Chipanganolo. Iwo anayika Bokosi la Mulungu pa ngolo yatsopano nachoka nalo ku nyumba ya Abinadabu, imene inali pa phiri. Uza ndi Ahiyo ana a Abinadabu ndiwo ankayendetsa ngolo yatsopanoyo, imene inanyamula Bokosi la Mulungu, ndipo Ahiyo mwana wa Abinadabu ankayenda patsogolo pake. Davide pamodzi ndi Aisraeli onse ankakondwerera ndi mphamvu zawo zonse pamaso pa Yehova poyimba nyimbo pogwiritsa ntchito azeze, apangwe, matambolini, maseche ndi malipenga.

Atafika pa malo opunthira tirigu a Nakoni, Uza anatambalitsa dzanja lake kuti agwire Bokosi la Mulungu, chifukwa ngʼombe zinkafuna kugwa. Yehova anapsera mtima Uza chifukwa chochita chinthu chosayenera kuchitika. Choncho Mulungu anamukantha ndipo anafera pomwepo pambali pa Bokosi la Mulungulo.

Ndipo Davide anakhumudwa chifukwa Yehova anakantha Uza ndipo mpaka lero malowo amatchedwa Perezi Uza.

Tsiku limenelo Davide anachita mantha ndi Yehova ndipo anati, “Kodi Bokosi la Yehova lingafike bwanji kwathu?” 10 Iye sanafunenso kubwera ndi Bokosi la Yehova kawo ku mzinda wake wa Davide. Mʼmalo mwake anapita nalo ku nyumba ya Obedi-Edomu Mgiti. 11 Bokosi la Yehova linakhala mʼnyumba ya Obedi-Edomu Mgiti kwa miyezi itatu, ndipo Yehova anamudalitsa kwambiri iyeyo ndi banja lake lonse.

12 Tsono Mfumu Davide anawuzidwa kuti, “Yehova wadalitsa nyumba ya Obedi-Edomu ndi zonse zimene ali nazo, chifukwa cha Bokosi la Mulungu.” Choncho Davide anapita kukatenga Bokosi la Mulungu ku nyumba ya Obedi-Edomu ndi kupita nalo ku mzinda wa Davide akukondwera kwambiri. 13 Anthu amene ananyamula Bokosi la Yehova ankati akayenda mapazi asanu ndi limodzi, iye ankapereka nsembe ngʼombe yayimuna ndi mwana wangʼombe wonenepa. 14 Davide ankavina ndi mphamvu zake zonse pamaso pa Yehova atavala efodi ya nsalu yofewa yosalala, 15 pamene iyeyo pamodzi ndi Aisraeli onse ankabwera ndi Bokosi la Yehova, akufuwula ndi kuyimba malipenga.

16 Bokosi la Yehova likulowa mu Mzinda wa Davide, Mikala mwana wamkazi wa Sauli ankaona ali pa zenera. Ndipo ataona Mfumu Davide ikulumpha ndi kuvina pamaso pa Yehova, ankamunyogodola mu mtima mwake.

17 Iwo anabwera nalo Bokosi la Yehova ndipo analiyika pamalo pake mʼkati mwa tenti imene Davide anayimika ndipo Davideyo anapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano pamaso pa Yehova. 18 Atatsiriza kupereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano, iye anadalitsa anthu mʼdzina la Yehova Wamphamvuzonse. 19 Kenaka iye anagawira Aisraeli onsewo, aamuna ndi aakazi, aliyense buledi mmodzi, nthuli yanyama, ndiponso keke yamphesa zowuma. Ndipo anthu onse anachokapo, napita aliyense ku nyumba kwake.

20 Davide atabwerera ku nyumba kwake kukadalitsa banja lake, Mikala mwana wamkazi wa Sauli anatuluka kudzakumana naye ndipo anati, “Kodi mfumu ya Israeli ingatero kudzilemekeza kwake lero, kudzithyolathyola pamaso pa akapolo aakazi, antchito ake ngati munthu wamba.”

21 Davide anamuyankha Mikala kuti, “Ndachita zimenezi molemekeza Yehova, amene anandisankha ine kupambana abambo ako, kapenanso kupambana banja la abambo ako. Ndipo anandisankha kuti ndikhale wolamulira Aisraeli, anthu a Yehova. Nʼchifukwa chake ndidzasangalalabe pamaso pa Yehova. 22 Ineyo ndidzadzinyoza kuposa apa, ndipo ndidzakhala wonyozeka mʼmaso mwako. Koma pakati pa akapolo aakazi awa amene umanena za iwo, ndidzalemekezedwa.”

23 Ndipo Mikala mwana wa Sauli sanakhalenso ndi mwana mpaka anamwalira.

The Ark Brought to Jerusalem(A)(B)

David again brought together all the able young men of Israel—thirty thousand. He and all his men went to Baalah[a](C) in Judah to bring up from there the ark(D) of God, which is called by the Name,[b](E) the name of the Lord Almighty, who is enthroned(F) between the cherubim(G) on the ark. They set the ark of God on a new cart(H) and brought it from the house of Abinadab, which was on the hill.(I) Uzzah and Ahio, sons of Abinadab, were guiding the new cart with the ark of God on it,[c] and Ahio was walking in front of it. David and all Israel were celebrating(J) with all their might before the Lord, with castanets,[d] harps, lyres, timbrels, sistrums and cymbals.(K)

When they came to the threshing floor of Nakon, Uzzah reached out and took hold of(L) the ark of God, because the oxen stumbled. The Lord’s anger burned against Uzzah because of his irreverent act;(M) therefore God struck him down,(N) and he died there beside the ark of God.

Then David was angry because the Lord’s wrath(O) had broken out against Uzzah, and to this day that place is called Perez Uzzah.[e](P)

David was afraid of the Lord that day and said, “How(Q) can the ark of the Lord ever come to me?” 10 He was not willing to take the ark of the Lord to be with him in the City of David. Instead, he took it to the house of Obed-Edom(R) the Gittite. 11 The ark of the Lord remained in the house of Obed-Edom the Gittite for three months, and the Lord blessed him and his entire household.(S)

12 Now King David(T) was told, “The Lord has blessed the household of Obed-Edom and everything he has, because of the ark of God.” So David went to bring up the ark of God from the house of Obed-Edom to the City of David with rejoicing. 13 When those who were carrying the ark of the Lord had taken six steps, he sacrificed(U) a bull and a fattened calf. 14 Wearing a linen ephod,(V) David was dancing(W) before the Lord with all his might, 15 while he and all Israel were bringing up the ark of the Lord with shouts(X) and the sound of trumpets.(Y)

16 As the ark of the Lord was entering the City of David,(Z) Michal(AA) daughter of Saul watched from a window. And when she saw King David leaping and dancing before the Lord, she despised him in her heart.

17 They brought the ark of the Lord and set it in its place inside the tent that David had pitched for it,(AB) and David sacrificed burnt offerings(AC) and fellowship offerings before the Lord. 18 After he had finished sacrificing(AD) the burnt offerings and fellowship offerings, he blessed(AE) the people in the name of the Lord Almighty. 19 Then he gave a loaf of bread, a cake of dates and a cake of raisins(AF) to each person in the whole crowd of Israelites, both men and women.(AG) And all the people went to their homes.

20 When David returned home to bless his household, Michal daughter of Saul came out to meet him and said, “How the king of Israel has distinguished himself today, going around half-naked(AH) in full view of the slave girls of his servants as any vulgar fellow would!”

21 David said to Michal, “It was before the Lord, who chose me rather than your father or anyone from his house when he appointed(AI) me ruler(AJ) over the Lord’s people Israel—I will celebrate before the Lord. 22 I will become even more undignified than this, and I will be humiliated in my own eyes. But by these slave girls you spoke of, I will be held in honor.”

23 And Michal daughter of Saul had no children to the day of her death.

Footnotes

  1. 2 Samuel 6:2 That is, Kiriath Jearim (see 1 Chron. 13:6)
  2. 2 Samuel 6:2 Hebrew; Septuagint and Vulgate do not have the Name.
  3. 2 Samuel 6:4 Dead Sea Scrolls and some Septuagint manuscripts; Masoretic Text cart and they brought it with the ark of God from the house of Abinadab, which was on the hill
  4. 2 Samuel 6:5 Masoretic Text; Dead Sea Scrolls and Septuagint (see also 1 Chron. 13:8) songs
  5. 2 Samuel 6:8 Perez Uzzah means outbreak against Uzzah.