Add parallel Print Page Options

Mawu Otsiriza a Davide

23 Nawa mawu otsiriza a Davide:

“Mawu a Davide mwana wa Yese,
    mawu a munthu amene wakwezedwa ndi Wammwambamwamba,
munthu wodzozedwa ndi Mulungu wa Yakobo,
    woyimba nyimbo za Israeli:

“Mzimu wa Yehova unayankhula kudzera mwa ine;
    mawu ake anali pakamwa panga.
Mulungu wa Israeli anayankhula,
    Thanthwe la Israeli linati kwa ine:
‘Pamene munthu alamulira anthu mwachilungamo,
    pamene alamulira moopa Mulungu,
amakhala ngati kuwala kwa mmamawa,
    mmawa wopanda mitambo,
monga kuwala pamene mvula yaleka kugwa
    imene imameretsa udzu mʼnthaka.’

“Kodi banja langa silolungama pamaso pa Mulungu?
    Kodi Iye sanachite pangano losatha ndi ine,
    lokonzedwa ndi lotetezedwa mbali zonse?
Kodi sadzakwaniritsa chipulumutso changa,
    ndi kundipatsa chokhumba changa chilichonse?
Koma anthu oyipa ndiwo ayenera kutayidwa kunja ngati minga,
    imene sitengedwa ndi manja.
Aliyense amene wayikhudza mingayo
    amayidula pogwiritsa ntchito chigwandali kapena ndodo ya mkondo;
    nayitentha pa moto.”

Ankhondo Otchuka a Davide

Nawa mayina a ankhondo amphamvu a Davide:

Yosebu-Basebeti wa ku Takemoni mkulu wa atsogoleri a ankhondo atatu. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 800 nthawi imodzi.

Wotsatana naye anali Eliezara mwana wa Dodo Mwahohi. Monga mmodzi mwa ankhondo atatu amphamvu a Davide, iye anali ndi Davide pamene anazunza Afilisti amene anasonkhana ku Pasi-Damimu kuchita nkhondo. Kenaka ankhondo a Israeli anabwerera mʼmbuyo. 10 Koma iye anayima osasuntha ndipo anakantha Afilisti mpaka mkono wake unatopa ndipo unakanirira ku lupanga lake. Yehova anapereka chigonjetso chachikulu pa tsiku limenelo. Asilikali anabwerera kwa Eliezara, kukatenga katundu wa anthu ophedwa.

11 Wotsatana naye anali Sama mwana wa Age Mharari. Pamene Afilisti anasonkhana pamalo pamene panali munda wa mphodza, ankhondo a Israeli anathawa Afilistiwo. 12 Koma Sama anayima pakati pa mundawo. Iye anawuteteza nakantha Afilistiwo ndipo Yehova anawapambanitsa koposa.

13 Pa nthawi yokolola, atatu mwa atsogoleri makumi atatu anabwera kwa Davide ku phanga la Adulamu, pamene gulu la Afilisti linali litamanga misasa mʼchigwa cha Refaimu. 14 Nthawi imeneyo Davide anali mu linga, ndipo boma la Afilisti linali ku Betelehemu. 15 Davide analakalaka madzi ndipo anati, “Haa, pakanapezeka munthu wokanditungira madzi a mʼchitsime chomwe chili pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu!” 16 Choncho anthu amphamvu atatuwa anadutsa mizere ya Afilisti, natunga madzi amene anali mʼchitsime chomwe chinali pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu nabwera nawo kwa Davide. Koma iye anakana kumwa. Mʼmalo mwake anathira pansi pamaso pa Yehova. 17 Iye anati, “Inu Yehova, musalole kuti ine ndichite chinthu ichi! Kodi awa si magazi a anthu amene anayika miyoyo yawo pachiswe?” Ndipo Davide sanamwe madziwo.

Zimenezi ndi zimene anachita anthu amphamvu atatuwo.

18 Abisai mʼbale wa Yowabu mwana wa Zeruya ndiye anali mtsogoleri wa anthu atatuwa. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 300, choncho iyeyo anali wotchuka pakati pa anthu atatu aja. 19 Kodi iyeyo sanali wolemekezeka koposa? Iye anakhala mtsogoleri wawo ngakhale kuti sanali mʼgulu la anthu atatu aja.

20 Benaya mwana wa Yehoyada wa ku Kabizeeli anali munthu wolimba mtima amene anachita zinthu zamphamvu. Iye anakantha ankhondo awiri otchuka a ku Mowabu. Tsiku lina kukuzizira kwambiri, iye analowa mʼdzenje ndi kuphamo mkango. 21 Ndipo iye anakanthanso Mwigupto wamkulu msinkhu. Ngakhale kuti Mwiguptoyo anali ndi mkondo mʼdzanja mwake, Benaya anapita kukamenyana naye ali ndi chibonga chokha mʼmanja. Iye analanda mkondo mʼdzanja la Mwiguptoyo ndi kumupha ndi mkondo wake womwe. 22 Izi ndi zamphamvu zimene Benaya mwana wa Yehoyada anachita. Iyeyo analinso wotchuka ngati anthu atatu amphamvu aja. 23 Iye ankalemekezedwa kuposa wina aliyense mwa anthu makumi atatu aja, koma sanali mʼgulu la anthu atatu aja. Ndipo Davide anamuyika kukhala woyangʼanira asilikali omuteteza.

24 Mʼgulu la anthu makumi atatu aja munalinso awa:

Asaheli mʼbale wa Yowabu,

Elihanani mwana wa Dodo wa ku Betelehemu,

25 Sama Mharodi,

Elika Mherodi,

26 Helezi Mpaliti,

Ira mwana wa Ikesi wa ku Tekowa,

27 Abiezeri wa ku Anatoti,

Sibekai Mhusati,

28 Zalimoni Mwahohi,

Maharai Mnetofa,

29 Heledi mwana wa Baana Mnetofa,

Itai mwana wa Ribai wa ku Gibeya ku Benjamini,

30 Benaya Mpiratoni,

Hidayi wa ku zigwa za Gaasi.

31 Abi-Aliboni Mwaribati,

Azimaveti Mbarihumi,

32 Eliyahiba Msaaliboni,

ana a Yaseni,

Yonatani, 33 mwana wa Sama Mharari,

Ahiamu mwana wa Sarari Mharari,

34 Elifeleti mwana wa Ahasibai Mmaakati,

Eliamu mwana wa Ahitofele Mgiloni,

35 Heziro wa ku Karimeli,

Paarai Mwaribi,

36 Igala mwana wa Natani wa ku Zoba,

mwana wa Hagiri,

37 Zeleki Mwamoni,

Naharai wa ku Beeroti, mnyamata wonyamula zida za Yowabu mwana wa Zeruya,

38 Ira Mwitiri,

Garebu Mwitiri,

39 ndi Uriya Mhiti.

Onse pamodzi analipo 37.

David’s Last Words

23 These are the last words of David:

“The inspired utterance of David son of Jesse,
    the utterance of the man exalted(A) by the Most High,
the man anointed(B) by the God of Jacob,
    the hero of Israel’s songs:

“The Spirit(C) of the Lord spoke through me;
    his word was on my tongue.
The God of Israel spoke,
    the Rock(D) of Israel said to me:
‘When one rules over people in righteousness,(E)
    when he rules in the fear(F) of God,(G)
he is like the light(H) of morning(I) at sunrise(J)
    on a cloudless morning,
like the brightness after rain(K)
    that brings grass from the earth.’

“If my house were not right with God,
    surely he would not have made with me an everlasting covenant,(L)
    arranged and secured in every part;
surely he would not bring to fruition my salvation
    and grant me my every desire.
But evil men are all to be cast aside like thorns,(M)
    which are not gathered with the hand.
Whoever touches thorns
    uses a tool of iron or the shaft of a spear;
    they are burned up where they lie.”

David’s Mighty Warriors(N)

These are the names of David’s mighty warriors:(O)

Josheb-Basshebeth,[a](P) a Tahkemonite,[b] was chief of the Three; he raised his spear against eight hundred men, whom he killed[c] in one encounter.

Next to him was Eleazar son of Dodai(Q) the Ahohite.(R) As one of the three mighty warriors, he was with David when they taunted the Philistines gathered at Pas Dammim[d] for battle. Then the Israelites retreated, 10 but Eleazar stood his ground and struck down the Philistines till his hand grew tired and froze to the sword. The Lord brought about a great victory that day. The troops returned to Eleazar, but only to strip the dead.

11 Next to him was Shammah son of Agee the Hararite. When the Philistines banded together at a place where there was a field full of lentils, Israel’s troops fled from them. 12 But Shammah took his stand in the middle of the field. He defended it and struck the Philistines down, and the Lord brought about a great victory.

13 During harvest time, three of the thirty chief warriors came down to David at the cave of Adullam,(S) while a band of Philistines was encamped in the Valley of Rephaim.(T) 14 At that time David was in the stronghold,(U) and the Philistine garrison was at Bethlehem.(V) 15 David longed for water and said, “Oh, that someone would get me a drink of water from the well near the gate of Bethlehem!” 16 So the three mighty warriors broke through the Philistine lines, drew water from the well near the gate of Bethlehem and carried it back to David. But he refused to drink it; instead, he poured(W) it out before the Lord. 17 “Far be it from me, Lord, to do this!” he said. “Is it not the blood(X) of men who went at the risk of their lives?” And David would not drink it.

Such were the exploits of the three mighty warriors.

18 Abishai(Y) the brother of Joab son of Zeruiah was chief of the Three.[e] He raised his spear against three hundred men, whom he killed, and so he became as famous as the Three. 19 Was he not held in greater honor than the Three? He became their commander, even though he was not included among them.

20 Benaiah(Z) son of Jehoiada, a valiant fighter from Kabzeel,(AA) performed great exploits. He struck down Moab’s two mightiest warriors. He also went down into a pit on a snowy day and killed a lion. 21 And he struck down a huge Egyptian. Although the Egyptian had a spear in his hand, Benaiah went against him with a club. He snatched the spear from the Egyptian’s hand and killed him with his own spear. 22 Such were the exploits of Benaiah son of Jehoiada; he too was as famous as the three mighty warriors. 23 He was held in greater honor than any of the Thirty, but he was not included among the Three. And David put him in charge of his bodyguard.

24 Among the Thirty were:

Asahel(AB) the brother of Joab,

Elhanan son of Dodo from Bethlehem,

25 Shammah the Harodite,(AC)

Elika the Harodite,

26 Helez(AD) the Paltite,

Ira(AE) son of Ikkesh from Tekoa,

27 Abiezer(AF) from Anathoth,(AG)

Sibbekai[f] the Hushathite,

28 Zalmon the Ahohite,

Maharai(AH) the Netophathite,(AI)

29 Heled[g](AJ) son of Baanah the Netophathite,

Ithai son of Ribai from Gibeah(AK) in Benjamin,

30 Benaiah the Pirathonite,(AL)

Hiddai[h] from the ravines of Gaash,(AM)

31 Abi-Albon the Arbathite,

Azmaveth the Barhumite,(AN)

32 Eliahba the Shaalbonite,

the sons of Jashen,

Jonathan 33 son of[i] Shammah the Hararite,

Ahiam son of Sharar[j] the Hararite,

34 Eliphelet son of Ahasbai the Maakathite,(AO)

Eliam(AP) son of Ahithophel(AQ) the Gilonite,

35 Hezro the Carmelite,(AR)

Paarai the Arbite,

36 Igal son of Nathan from Zobah,(AS)

the son of Hagri,[k]

37 Zelek the Ammonite,

Naharai the Beerothite,(AT) the armor-bearer of Joab son of Zeruiah,

38 Ira the Ithrite,(AU)

Gareb the Ithrite

39 and Uriah(AV) the Hittite.

There were thirty-seven in all.

Footnotes

  1. 2 Samuel 23:8 Hebrew; some Septuagint manuscripts suggest Ish-Bosheth, that is, Esh-Baal (see also 1 Chron. 11:11 Jashobeam).
  2. 2 Samuel 23:8 Probably a variant of Hakmonite (see 1 Chron. 11:11)
  3. 2 Samuel 23:8 Some Septuagint manuscripts (see also 1 Chron. 11:11); Hebrew and other Septuagint manuscripts Three; it was Adino the Eznite who killed eight hundred men
  4. 2 Samuel 23:9 See 1 Chron. 11:13; Hebrew gathered there.
  5. 2 Samuel 23:18 Most Hebrew manuscripts (see also 1 Chron. 11:20); two Hebrew manuscripts and Syriac Thirty
  6. 2 Samuel 23:27 Some Septuagint manuscripts (see also 21:18; 1 Chron. 11:29); Hebrew Mebunnai
  7. 2 Samuel 23:29 Some Hebrew manuscripts and Vulgate (see also 1 Chron. 11:30); most Hebrew manuscripts Heleb
  8. 2 Samuel 23:30 Hebrew; some Septuagint manuscripts (see also 1 Chron. 11:32) Hurai
  9. 2 Samuel 23:33 Some Septuagint manuscripts (see also 1 Chron. 11:34); Hebrew does not have son of.
  10. 2 Samuel 23:33 Hebrew; some Septuagint manuscripts (see also 1 Chron. 11:35) Sakar
  11. 2 Samuel 23:36 Some Septuagint manuscripts (see also 1 Chron. 11:38); Hebrew Haggadi