Add parallel Print Page Options

Kubwera kwa Ambuye

Inu okondedwa, iyi ndi kalata yanga yachiwiri kwa inu. Ine ndalemba makalata onse awiri kuti ndikukumbutseni ndi kukutsitsimutsani ndi cholinga choti muzilingalira moyenera. Ndikufuna kuti mukumbukire mawu amene anayankhulidwa kale ndi aneneri oyera mtima ndiponso lamulo limene Ambuye ndi Mpulumutsi wathu analipereka kudzera mwa atumwi.

Poyamba mudziwe kuti mʼmasiku otsiriza kudzafika anthu onyoza, adzanyoza ndi kutsata zilakolako zawo zoyipa. Iwo adzati, “Kodi suja Ambuye analonjeza kuti adzabweranso? Nanga ali kuti? Lija nʼkale anamwalira makolo athu, koma zinthu zonse zili monga anazilengera poyamba paja.” Koma iwo akuyiwala dala kuti Mulungu atanena mawu, kumwamba kunakhalapo ndipo analenga dziko lapansi ndi madzi. Ndi madzinso achigumula, dziko lapansi la masiku amenewo linawonongedwa. Dziko la kumwamba ndi lapansi la masiku ano akulisunga ndi mawu omwewo kuti adzalitentha ndi moto. Akuzisunga mpaka tsiku limene adzaweruza ndi kuwononga anthu onse osapembedza Mulungu.

Koma abale okondedwa, musayiwale chinthu chimodzi ichi: Kuti pamaso pa Ambuye tsiku limodzi lili ngati zaka 1,000, ndipo zaka 1,000 zili ngati tsiku limodzi! Ambuye sazengereza kuchita zimene analonjeza, monga ena amaganizira. Iwo akukulezerani mtima, sakufuna kuti aliyense awonongeke, koma akufuna kuti aliyense alape.

10 Koma tsiku la Ambuye lidzafika ngati mbala. Pa tsikuli zinthu zakumwamba zidzachoka ndi phokoso lalikulu. Zinthu zonse zidzawonongedwa ndi moto, ndipo dziko lapansi ndi zonse zili mʼmenemo zidzapsa.

11 Popeza kuti zinthu zonse zidzawonongedwa motere, kodi inu muyenera kukhala anthu otani? Muyenera kukhala moyo wachiyero ndi opembedza Mulungu 12 pamene mukuyembekezera tsiku la Mulungu ndi kufulumiza kufika kwake. Pa tsiku limeneli zinthu zakumwamba zidzawonongedwa ndi moto, ndipo zidzasungunuka ndi kutentha. 13 Koma ife tikudikira kumwamba kwatsopano ndi dziko lapansi latsopano, zimene Mulungu analonjeza, mʼmene chilungamo chidzakhalamo.

14 Chomwecho okondedwa, popeza inu mukudikira zimenezi, chitani changu kuti mukhale wopanda chilema kuti mukhale pa mtendere ndi Iye. 15 Zindikirani kuti kuleza mtima kwa Ambuye kukutanthauza chipulumutso, monga momwe mʼbale wathu wokondedwa Paulo anakulemberaninso ndi nzeru zimene Mulungu anamupatsa. 16 Iye walemba chimodzimodzi makalata ake onse, kuyankhula za zinthu izi. Mʼmakalata ake mumakhala zinthu zina zovuta kuzimvetsa, zimene anthu osadziwa ndi osakhazikika amazipotoza, monga amachita ndi malemba ena onse, potero akudziwononga okha.

17 Nʼchifukwa chake, abale okondedwa, popeza mukuzidziwa kale zimenezi, chenjerani kuti musatengeke ndi zolakwa za anthu osaweruzika, mungagwe ndi kuchoka pamalo otetezedwa. 18 Koma kulani mu chisomo ndi mʼchidziwitso cha Ambuye ndi Mpulumutsi wathu Yesu Khristu. Kwa Iye kukhale ulemerero tsopano mpaka muyaya. Ameni.

The Day of the Lord

Dear friends,(A) this is now my second letter to you. I have written both of them as reminders(B) to stimulate you to wholesome thinking. I want you to recall the words spoken in the past by the holy prophets(C) and the command given by our Lord and Savior through your apostles.(D)

Above all, you must understand that in the last days(E) scoffers will come, scoffing and following their own evil desires.(F) They will say, “Where is this ‘coming’ he promised?(G) Ever since our ancestors died, everything goes on as it has since the beginning of creation.”(H) But they deliberately forget that long ago by God’s word(I) the heavens came into being and the earth was formed out of water and by water.(J) By these waters also the world of that time(K) was deluged and destroyed.(L) By the same word the present heavens and earth are reserved for fire,(M) being kept for the day of judgment(N) and destruction of the ungodly.

But do not forget this one thing, dear friends: With the Lord a day is like a thousand years, and a thousand years are like a day.(O) The Lord is not slow in keeping his promise,(P) as some understand slowness. Instead he is patient(Q) with you, not wanting anyone to perish, but everyone to come to repentance.(R)

10 But the day of the Lord will come like a thief.(S) The heavens will disappear with a roar;(T) the elements will be destroyed by fire,(U) and the earth and everything done in it will be laid bare.[a](V)

11 Since everything will be destroyed in this way, what kind of people ought you to be? You ought to live holy and godly lives 12 as you look forward(W) to the day of God and speed its coming.[b](X) That day will bring about the destruction of the heavens by fire, and the elements will melt in the heat.(Y) 13 But in keeping with his promise we are looking forward to a new heaven and a new earth,(Z) where righteousness dwells.

14 So then, dear friends, since you are looking forward to this, make every effort to be found spotless, blameless(AA) and at peace with him. 15 Bear in mind that our Lord’s patience(AB) means salvation,(AC) just as our dear brother Paul also wrote you with the wisdom that God gave him.(AD) 16 He writes the same way in all his letters, speaking in them of these matters. His letters contain some things that are hard to understand, which ignorant and unstable(AE) people distort,(AF) as they do the other Scriptures,(AG) to their own destruction.

17 Therefore, dear friends, since you have been forewarned, be on your guard(AH) so that you may not be carried away by the error(AI) of the lawless(AJ) and fall from your secure position.(AK) 18 But grow in the grace(AL) and knowledge(AM) of our Lord and Savior Jesus Christ.(AN) To him be glory both now and forever! Amen.(AO)

Footnotes

  1. 2 Peter 3:10 Some manuscripts be burned up
  2. 2 Peter 3:12 Or as you wait eagerly for the day of God to come