Add parallel Print Page Options

Ntchito Zina za Solomoni

Patatha zaka makumi awiri, ndiye nthawi imene Solomoni anamanga Nyumba ya Mulungu ndi nyumba yake yaufumu, Solomoni anamanganso midzi imene anapatsidwa ndi Hiramu, ndipo anakhazikamo Aisraeli. Kenaka Solomoni anapita kukalanda Hamati-zoba. Iye anamanganso Tadimori ku chipululu ndi mizinda yonse yosungiramo chuma, imene anayimanga ku Hamati. Anamanganso Beti-Horoni Wakumtunda ndi Beti-Horoni Wakumunsi, mizinda yotetezedwa yokhala ndi makoma, zitseko ndi zitsulo zotchingira, pamodzinso ndi Baalati ndi mizinda yake yonse yosungira chuma, ndiponso mizinda yonse yosungiramo magaleta ake ndi akavalo ndi chilichonse anafuna kumanga ku Yerusalemu, ku Lebanoni ndi ku madera onse amene iye ankalamulira.

Panali anthu amene anatsala pakati pa mitundu ya Ahiti, Aamori, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi (anthu awa sanali Aisraeli). Zimenezi ndiye zinali zidzukulu zawo zotsalira mʼdzikoli, anthu amene Aisraeli sanathe kuwawononga kotheratu. Solomoni anawatenga ndi kukhala akapolo ake ogwira ntchito yathangata, monga zilili mpaka lero lino. Koma Solomoni sanagwiritse ntchito ya ukapolo Aisraeli; Iwo anali anthu ake ankhondo, atsogoleri a ankhondo, olamulira magaleta ndi oyendetsa magaleta ake. 10 Amenewa ndiwo anali akuluakulu oyangʼanira ntchito za mfumu Solomoni. Onse amene ankayangʼanira anthu analipo 250.

11 Solomoni anabweretsa mwana wamkazi wa Farao mu mzinda wa Davide ku nyumba yaufumu yomwe anamumangira, pakuti iye anati, “Mkazi wanga asakhale mʼnyumba yaufumu ya Davide mfumu ya Israeli, chifukwa malo amene Bokosi la Chipangano la Yehova lafikira ndi opatulika.”

12 Solomoni anapereka nsembe zopsereza pa guwa lansembe la Yehova limene anamanga patsogolo pa khonde la polowera, 13 monga momwe zinkafunikira pa tsiku lililonse. Ankapereka nsembezo potsata malamulo a Mose okhudza chikondwerero cha Masabata, chikondwerero cha Mwezi Watsopano ndi zikondwerero zitatu za pa chaka: Chikondwerero cha Buledi Wopanda yisiti, Chikondwerero cha Masabata ndi Chikondwerero cha Misasa. 14 Potsata malangizo a Davide abambo ake, iye anayika ansembe mʼmagulumagulu monga mwa ntchito zawo ndipo anayika Alevi kukhala otsogolera matamando ndi kuthandiza ansembe pa zofunika pa tsiku lililonse. Iye anasankhanso magulumagulu a alonda a pa zipata zosiyanasiyana, chifukwa izi ndi zimene munthu wa Mulungu, Davide analamula. 15 Anthu sanapatukepo pa zimene mfumu inalamula ansembe kapena Alevi pa china chilichonse, kuphatikiza za chuma.

16 Ntchito yonse ya Solomoni inachitika kuyambira tsiku limene maziko a Nyumba ya Mulungu anakhazikitsidwa mpaka kumaliza. Kotero Nyumba ya Yehova inamalizidwa.

17 Kenaka Solomoni anapita ku Ezioni-Geberi ndi Eloti, mʼmbali mwa nyanja ku Edomu. 18 Ndipo Hiramu anatumiza sitima zapamadzi zoyendetsedwa ndi antchito ake, antchito amene ankayidziwa bwino nyanja. Awa pamodzi ndi anthu a Solomoni, anayenda pa madzi kupita ku Ofiri ndipo anakatengako golide olemera makilogalamu 18,000 amene anabwera naye kwa mfumu Solomoni.

Solomon’s Other Activities(A)

At the end of twenty years, during which Solomon built the temple of the Lord and his own palace,(B) Solomon rebuilt the villages that Hiram[a] had given him, and settled Israelites in them. Solomon then went to Hamath Zobah and captured it. He also built up Tadmor in the desert and all the store cities he had built in Hamath.(C) He rebuilt Upper Beth Horon(D) and Lower Beth Horon as fortified cities, with walls and with gates and bars, as well as Baalath(E) and all his store cities, and all the cities for his chariots and for his horses[b]—whatever he desired to build in Jerusalem, in Lebanon and throughout all the territory he ruled.

There were still people left from the Hittites, Amorites, Perizzites, Hivites and Jebusites(F) (these people were not Israelites). Solomon conscripted(G) the descendants of all these people remaining in the land—whom the Israelites had not destroyed—to serve as slave labor, as it is to this day. But Solomon did not make slaves of the Israelites for his work; they were his fighting men, commanders of his captains, and commanders of his chariots and charioteers. 10 They were also King Solomon’s chief officials—two hundred and fifty officials supervising the men.

11 Solomon brought Pharaoh’s daughter(H) up from the City of David to the palace he had built for her, for he said, “My wife must not live in the palace of David king of Israel, because the places the ark of the Lord has entered are holy.”

12 On the altar(I) of the Lord that he had built in front of the portico, Solomon sacrificed burnt offerings to the Lord, 13 according to the daily requirement(J) for offerings commanded by Moses for the Sabbaths,(K) the New Moons(L) and the three(M) annual festivals—the Festival of Unleavened Bread,(N) the Festival of Weeks(O) and the Festival of Tabernacles.(P) 14 In keeping with the ordinance of his father David, he appointed the divisions(Q) of the priests for their duties, and the Levites(R) to lead the praise and to assist the priests according to each day’s requirement. He also appointed the gatekeepers(S) by divisions for the various gates, because this was what David the man of God(T) had ordered.(U) 15 They did not deviate from the king’s commands to the priests or to the Levites in any matter, including that of the treasuries.

16 All Solomon’s work was carried out, from the day the foundation of the temple of the Lord was laid until its completion. So the temple of the Lord was finished.

17 Then Solomon went to Ezion Geber and Elath on the coast of Edom. 18 And Hiram sent him ships commanded by his own men, sailors who knew the sea. These, with Solomon’s men, sailed to Ophir and brought back four hundred and fifty talents[c] of gold,(V) which they delivered to King Solomon.

Footnotes

  1. 2 Chronicles 8:2 Hebrew Huram, a variant of Hiram; also in verse 18
  2. 2 Chronicles 8:6 Or charioteers
  3. 2 Chronicles 8:18 That is, about 17 tons or about 15 metric tons