Add parallel Print Page Options

Hezekiya Achita Chikondwerero cha Paska

30 Hezekiya anatumiza uthenga mʼdziko lonse la Israeli ndi ku Yuda ndiponso analemba makalata ku Efereimu ndi Manase, oyitana anthu kuti abwere ku Nyumba ya Yehova ku Yerusalemu kudzakondwerera Paska wa Yehova, Mulungu wa Israeli. Mfumu ndi akuluakulu ake pamodzi ndi anthu onse a mu Yerusalemu anagwirizana kuti akondwerere Paska pa mwezi wachiwiri. Iwo sanathe kukondwerera pa nthawi yake chifukwa si ansembe ambiri amene anadziyeretsa ndiponso anthu anali asanasonkhane mu Yerusalemu. Chikonzerochi chinaoneka kuti chinali chabwino kwa mfumu pamodzi ndi anthu onse. Iwo anagwirizana zoti alengeze mu Israeli monse kuyambira ku Beeriseba mpaka ku Dani, kuyitana anthu kuti abwere ku Yerusalemu ndi kudzakondwerera Paska wa Yehova, Mulungu wa Israeli. Si ambiri amene ankachita chikondwererochi monga momwe kunalembedwera.

Molamulidwa ndi mfumu, amithenga anapita mu Israeli yense ndi Yuda ndi makalata ochokera kwa mfumu ndi kwa akuluakulu ake, olembedwa kuti,

“Aisraeli bwererani kwa Yehova, Mulungu wa Abrahamu, Isake ndi Israeli, kuti abwerere kwa inu amene mwatsala, amene mwapulumuka mʼdzanja la mafumu a ku Asiriya. Musakhale ngati makolo anu ndi abale anu, amene anali osakhulupirika kwa Yehova Mulungu wa makolo awo kotero kuti anawachititsa kuti akhale chinthu chochititsa mantha, monga mukuoneramu. Musawumitse khosi monga anachitira makolo anu, Gonjerani Yehova. Bwerani ku malo opatulika, amene anawapatula kwamuyaya. Tumikirani Yehova Mulungu wanu kuti mkwiyo wake ukuchokereni. Ngati inu mubwerera kwa Yehova, pamenepo abale anu ndi ana anu adzachitiridwa chifundo ndi amene anawagwira ukapolo ndipo adzabwereranso ku dziko lino pakuti Yehova, Mulungu wanu ndi wokoma mtima ndi wachifundo. Iye sadzakufulatirani ngati inuyo mubwerera kwa Iye.”

10 Amithenga aja anapita mzinda ndi mzinda wa ku Efereimu ndi Manase mpaka ku Zebuloni, koma anthu anawanyoza ndi kuwachita chipongwe. 11 Komabe anthu ena a ku Aseri, Manase ndi Zebuloni anadzichepetsa ndipo anapita ku Yerusalemu. 12 Dzanja la Mulungu linalinso pa anthu a ku Yuda, kuwapatsa mtima umodzi wochita zimene mfumu ndi akuluakulu ake analamula potsata mawu a Yehova.

13 Gulu lalikulu la anthu linasonkhana mu Yerusalemu kudzachita chikondwerero cha Buledi Wopanda Yisiti pa mwezi wachiwiri. 14 Anachotsa mu Yerusalemu maguwa ofukizira lubani ndipo anakawaponya mʼchigwa cha Kidroni.

15 Iwo anapha mwana wankhosa wa Paska pa tsiku la 14 la mwezi wachiwiri. Ansembe ndi Alevi anachita manyazi ndipo anadziyeretsa ndi kubweretsa nsembe zopsereza ku Nyumba ya Yehova. 16 Ndipo anakhala mʼmalo awo a nthawi zonse potsatira zolembedwa mʼmalamulo a Mose munthu wa Mulungu. Ansembe anawaza magazi amene anawapatsa Alevi. 17 Popeza ambiri mʼgululo anali asanadziyeretse, Alevi anapha ana ankhosa a Paska a iwo amene, mwa mwambo, anali osayeretsedwa ndipo sakanatha kupereka ana ankhosa awo kwa Yehova. 18 Ngakhale kuti ambiri mwa anthu ochokera ku Efereimu, Manase, Isakara ndi Zebuloni sanadziyeretse okha, komabe anadya Paska motsutsana ndi zimene zinalembedwa. Koma Hezekiya anawapempherera, kunena kuti, “Yehova wabwino, khululukirani aliyense 19 amene wayika mtima wake kufunafuna Yehova, Mulungu wa makolo ake, ngakhale ali wosayeretsedwa molingana ndi malamulo a malo opatulika.” 20 Ndipo Yehova anamvera Hezekiya ndipo anachiritsa anthuwo.

21 Aisraeli amene anali mu Yerusalemu anachita chikondwerero cha Buledi Wopanda Yisiti kwa masiku asanu ndi awiri akusangalala kwambiri, pamene Alevi ndi ansembe amayimbira Yehova tsiku lililonse, akuyimbira zida zamatamando za Yehova.

22 Hezekiya anayankhula molimbikitsa Alevi onse amene anaonetsa kumvetsa bwino za kutumikira Yehova. Kwa masiku asanu ndi awiri anadya gawo lawo ndi kupereka nsembe zachiyanjano ndi kutamanda Yehova, Mulungu wa makolo awo.

23 Ndipo msonkhano wonse unagwirizana zopitiriza chikondwerero kwa masiku ena asanu ndi awiri. Kotero kwa masiku ena asanu ndi awiri anachita chikondwererocho mosangalala. 24 Hezekiya mfumu ya Yuda anapereka ngʼombe zamphongo 1,000 ndi nkhosa ndi mbuzi 7,000 ku msonkhanoko ndipo akuluakulu ake anapereka ngʼombe zamphongo 1,000, nkhosa ndi mbuzi 10,000. Ansembe ambiri anadziyeretsa. 25 Gulu lonse la ku Yuda linasangalala, pamodzi ndi ansembe ndi Alevi ndi onse amene anasonkhana ochokera ku Israeli, kuphatikizanso alendo amene anachokera ku Israeli ndi amene amakhala ku Yuda. 26 Munali chikondwerero chachikulu mu Yerusalemu, pakuti kuyambira masiku a Solomoni mwana wa Davide mfumu ya Israeli sizinachitikepo zotere mu Yerusalemu. 27 Ansembe ndi Alevi anayimirira kudalitsa anthu, ndipo Mulungu anawamvera pakuti pemphero lawo linafika kumwamba, malo ake oyera.

Hezekiah Celebrates the Passover

30 Hezekiah sent word to all Israel(A) and Judah and also wrote letters to Ephraim and Manasseh,(B) inviting them to come to the temple of the Lord in Jerusalem and celebrate the Passover(C) to the Lord, the God of Israel. The king and his officials and the whole assembly in Jerusalem decided to celebrate(D) the Passover in the second month. They had not been able to celebrate it at the regular time because not enough priests had consecrated(E) themselves and the people had not assembled in Jerusalem. The plan seemed right both to the king and to the whole assembly. They decided to send a proclamation throughout Israel, from Beersheba to Dan,(F) calling the people to come to Jerusalem and celebrate the Passover to the Lord, the God of Israel. It had not been celebrated in large numbers according to what was written.

At the king’s command, couriers went throughout Israel and Judah with letters from the king and from his officials, which read:

“People of Israel, return to the Lord, the God of Abraham, Isaac and Israel, that he may return to you who are left, who have escaped from the hand of the kings of Assyria. Do not be like your parents(G) and your fellow Israelites, who were unfaithful(H) to the Lord, the God of their ancestors, so that he made them an object of horror,(I) as you see. Do not be stiff-necked,(J) as your ancestors were; submit to the Lord. Come to his sanctuary, which he has consecrated forever. Serve the Lord your God, so that his fierce anger(K) will turn away from you. If you return(L) to the Lord, then your fellow Israelites and your children will be shown compassion(M) by their captors and will return to this land, for the Lord your God is gracious and compassionate.(N) He will not turn his face from you if you return to him.”

10 The couriers went from town to town in Ephraim and Manasseh, as far as Zebulun, but people scorned and ridiculed(O) them. 11 Nevertheless, some from Asher, Manasseh and Zebulun humbled(P) themselves and went to Jerusalem.(Q) 12 Also in Judah the hand of God was on the people to give them unity(R) of mind to carry out what the king and his officials had ordered, following the word of the Lord.

13 A very large crowd of people assembled in Jerusalem to celebrate the Festival of Unleavened Bread(S) in the second month. 14 They removed the altars(T) in Jerusalem and cleared away the incense altars and threw them into the Kidron Valley.(U)

15 They slaughtered the Passover lamb on the fourteenth day of the second month. The priests and the Levites were ashamed and consecrated(V) themselves and brought burnt offerings to the temple of the Lord. 16 Then they took up their regular positions(W) as prescribed in the Law of Moses the man of God. The priests splashed against the altar the blood handed to them by the Levites. 17 Since many in the crowd had not consecrated themselves, the Levites had to kill(X) the Passover lambs for all those who were not ceremonially clean and could not consecrate their lambs[a] to the Lord. 18 Although most of the many people who came from Ephraim, Manasseh, Issachar and Zebulun had not purified themselves,(Y) yet they ate the Passover, contrary to what was written. But Hezekiah prayed for them, saying, “May the Lord, who is good, pardon everyone 19 who sets their heart on seeking God—the Lord, the God of their ancestors—even if they are not clean according to the rules of the sanctuary.” 20 And the Lord heard(Z) Hezekiah and healed(AA) the people.(AB)

21 The Israelites who were present in Jerusalem celebrated the Festival of Unleavened Bread(AC) for seven days with great rejoicing, while the Levites and priests praised the Lord every day with resounding instruments dedicated to the Lord.[b]

22 Hezekiah spoke encouragingly to all the Levites, who showed good understanding of the service of the Lord. For the seven days they ate their assigned portion and offered fellowship offerings and praised[c] the Lord, the God of their ancestors.

23 The whole assembly then agreed to celebrate(AD) the festival seven more days; so for another seven days they celebrated joyfully. 24 Hezekiah king of Judah provided(AE) a thousand bulls and seven thousand sheep and goats for the assembly, and the officials provided them with a thousand bulls and ten thousand sheep and goats. A great number of priests consecrated themselves. 25 The entire assembly of Judah rejoiced, along with the priests and Levites and all who had assembled from Israel(AF), including the foreigners who had come from Israel and also those who resided in Judah. 26 There was great joy in Jerusalem, for since the days of Solomon(AG) son of David king of Israel there had been nothing like this in Jerusalem. 27 The priests and the Levites stood to bless(AH) the people, and God heard them, for their prayer reached heaven, his holy dwelling place.

Footnotes

  1. 2 Chronicles 30:17 Or consecrate themselves
  2. 2 Chronicles 30:21 Or priests sang to the Lord every day, accompanied by the Lord’s instruments of praise
  3. 2 Chronicles 30:22 Or and confessed their sins to