Add parallel Print Page Options

Kupulumutsidwa kwa Yerusalemu

19 Mfumu Hezekiya atamva zimenezi, anangʼamba zovala zake navala chiguduli ndipo analowa mʼNyumba ya Yehova. Iye anatuma Eliyakimu, woyangʼanira nyumba ya mfumu, Sebina mlembi wa bwalo ndi ansembe akuluakulu, onse atavala ziguduli, kwa mneneri Yesaya mwana wa Amozi. Iwo anamuwuza kuti, “Hezekiya akunena kuti, ‘Lero ndi tsiku lamavuto, lachilango ndi lamanyazi. Ife lero tili ngati mayi woyembekezera amene pofika nthawi yoti achire akupezeka kuti alibe mphamvu zoberekera. Mwina Yehova Mulungu wanu adzamva mawu onse a Rabusake amene mbuye wake, mfumu ya ku Asiriya anamutuma kudzanyoza Mulungu wamoyo, ndipo Mulunguyo adzamulanga chifukwa cha mawu amene Yehova Mulungu wanu wamva. Choncho pemphererani anthu otsala amene akanali ndi moyo.’ ”

Akuluakulu a Mfumu Hezekiya atafika kwa Yesaya, Yesaya anawawuza kuti, “Kawuzeni mbuye wanu kuti, ‘Yehova akunena kuti: Usachite mantha ndi zimene wamva, mawu amene nthumwi za mfumu ya ku Asiriya zandinyoza nawo Ine. Tamverani! Ine ndidzayika mwa mfumuyo mzimu wina kotero kuti akadzamva mphekesera ya nkhondo, adzabwerera ku dziko lake ndipo Ine ndidzachititsa kuti aphedwe ndi lupanga kwawo komweko.’ ”

Rabusake atamva kuti mfumu ya ku Asiriya yachoka ku Lakisi, iye anabwerera mʼmbuyo ndipo anakapeza mfumu ikuchita nkhondo ndi mzinda wa Libina.

Nthawi imeneyi Senakeribu analandira uthenga wakuti Tirihaka, mfumu ya ku Kusi, akubwera kudzachita naye nkhondo. Choncho iye anatumanso amithenga kwa Hezekiya ndi mawu awa: 10 “Kawuzeni Hezekiya mfumu ya Yuda kuti: Usalole kuti Mulungu amene ukumudalira akupusitse ponena kuti, ‘Yerusalemu sadzaperekedwa mʼmanja mwa mfumu ya ku Asiriya.’ 11 Ndithu iwe unamva chimene mafumu a Asiriya anachita ku mayiko ena onse, kuti anawawononga kotheratu. Ndipo kodi iwe nʼkupulumuka? 12 Kodi milungu ya mitundu imene makolo anga anayigonjetsa, milungu ya anthu a ku Gozani, Harani, Rezefi ndi Aedeni amene anali ku Teli Asara, inawapulumutsa? 13 Kodi mafumu a Hamati, Aripadi ndi mafumu a mizinda ya Sefaravaimu, Hena ndi Iva, ali kuti?”

Pemphero la Hezekiya

14 Hezekiya analandira kalata kwa amithenga aja nayiwerenga. Pomwepo anapita ku Nyumba ya Yehova nayika kalatayo pamaso pa Yehova. 15 Ndipo Hezekiya anapemphera kwa Yehova nati, “Inu Yehova Mulungu wa Israeli, Inu amene mumakhala pa Akerubi, Inu nokha ndinu Mulungu wolamulira maufumu onse a dziko lapansi. Inu munalenga kumwamba ndi dziko lapansi. 16 Inu Yehova, tcherani khutu lanu ndipo mumve Yehova tsekulani maso anu ndipo muone, imvani mawu onse amene Senakeribu watumiza kunyoza Inu Mulungu wamoyo.

17 “Inu Yehova, nʼzoonadi kuti mafumu a Asiriya anawononga mitundu iyi ndi mayiko awo. 18 Iwo anaponya milungu yawo pa moto ndi kuyiwononga pakuti sinali milungu koma mitengo ndi miyala chabe, yopangidwa ndi anthu. 19 Ndipo tsopano Inu Yehova Mulungu wathu, tipulumutseni ndithu mʼdzanja lake, kuti maufumu onse a dziko lapansi adziwe kuti Inu nokha, Inu Yehova, ndinu Mulungu.”

Yankho la Mulungu Kudzera mwa Yesaya

20 Ndipo Yesaya mwana wa Amozi anatumiza uthenga kwa Hezekiya wakuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ndamva pemphero lako lonena za Senakeribu mfumu ya ku Asiriya.’ ” 21 Mawu amene Yehova wayankhula wotsutsana naye ndi awa:

“Namwali wa Ziyoni
    akukunyoza ndi kukuseka iwe.
Mwana wamkazi wa Yerusalemu
    akupukusa mutu wake kumbuyo kwako.
22 Kodi iweyo wanyoza ndi kuchitira chipongwe yani?
    Kodi ndani amene wamufuwulira mawu ako
ndi kumuyangʼana monyada?
    Wachitiratu izi Woyera wa Israeli!
23 Kudzera mwa amithenga ako
    wonyoza Ambuye.
Ndipo wanena kuti,
    ‘Ndi magaleta ochuluka
ndinakwera mapiri ataliatali,
    pa msonga za mapiri a Lebanoni.
Ndigwetsa mitengo yake ya mkungudza yayitali kwambiri,
    mitengo yake ya payini yabwino kwambiri.
Ndalowanso mʼkati mwake mwenimweni,
    mwa nkhalango yake yowirira kwambiri.
24 Ndakumba zitsime ku mayiko achilendo
    ndipo ndinamwa madzi a kumeneko.
Ndi mapazi anga
    ndawumitsa mitsinje yonse ya ku Igupto.’ ”

25 “ ‘Kodi sunamvepo?
    Zimenezi ndinazikhazikitsa kalekale.
Ndinazikonzeratu masiku amakedzana;
    tsopano ndachita kuti zichitikedi,
iwe kwako kunali kungosandutsa mizinda yotetezedwa
    kukhala milu ya miyala.
26 Anthu a kumeneko ndi opanda mphamvu,
    athedwa nzeru ndipo ali ndi manyazi.
Ali ngati mbewu za mʼmunda,
    ngati udzu wanthete,
ali ngati udzu womera pa denga,
    umene umawuma usanakule nʼkomwe.’ ”

27 “ ‘Koma Ine ndimadziwa kukhala kwako,
    kutuluka kwako ndi kulowa kwako,
    ndi mkwiyo wako pa Ine.
28 Chifukwa chakuti wandikwiyira
    ndipo ndamva za mwano wako,
ndidzakola mphuno yako ndi mbedza
    ndi kuyika chitsulo changa mʼkamwa mwako,
ndipo ndidzakubweza pokudzeretsa
    njira yomwe unadzera pobwera.’

29 “Koma iwe Hezekiya, chizindikiro chako chidzakhala ichi:

“Chaka chino mudzadya tirigu wamphulumukwa,
    ndipo chaka chamawa mudzadya tirigu wongodzimerera.
Koma chaka chachitatu mudzadzala ndi kukolola,
    mudzawoka mphesa ndipo mudzadya zipatso zake.
30 Anthu a nyumba ya Yuda amene adzatsale
    adzazika mizu ndi kubereka zipatso.
31 Pakuti ku Yerusalemu kudzachokera anthu otsala,
    ndi ku phiri la Ziyoni kudzachokera gulu la anthu opulumuka.”

“Changu cha Yehova Wamphamvuzonse chidzachita zimenezi.

32 “Choncho chimene Yehova akunena za mfumu ya ku Asiriya ndi ichi:

“ ‘Iye sadzalowa mu mzinda umenewu
    kapena kuponyamo muvi.
Sadzayandikira mzindawu ndi zishango zake
    kapena kumanga nthumbira ya nkhondo.
33 Adzabwerera potsata njira imene anadzera pobwera;
    sadzalowa mu mzinda umenewu,
            akutero Yehova.
34 Ndidzateteza mzinda umenewu kuwupulumutsa,
    chifukwa cha Ine mwini ndiponso chifukwa cha Davide mtumiki wanga.’ ”

35 Usiku umenewo mngelo wa Yehova anapita ku misasa ya ku Asiriya ndi kupha ankhondo 185,000. Ndipo pamene anthu anadzuka mmawa, taonani, mitembo inali ngundangunda! 36 Choncho Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anapasula misasa ndi kuchoka. Anabwerera ku Ninive nakakhala kumeneko.

37 Tsiku lina, pamene Senakeribu ankapembedza mʼnyumba ya Nisiroki mulungu wake, ana ake Adirameleki ndi Sarezeri anamupha ndi lupanga ndipo anathawira ku dziko la Ararati. Tsono Esrahadoni, mwana wake, analowa ufumu mʼmalo mwake.

Jerusalem’s Deliverance Foretold(A)

19 When King Hezekiah heard this, he tore(B) his clothes and put on sackcloth and went into the temple of the Lord. He sent Eliakim(C) the palace administrator, Shebna the secretary and the leading priests,(D) all wearing sackcloth,(E) to the prophet Isaiah(F) son of Amoz. They told him, “This is what Hezekiah says: This day is a day of distress and rebuke and disgrace, as when children come to the moment(G) of birth and there is no strength to deliver them. It may be that the Lord your God will hear all the words of the field commander, whom his master, the king of Assyria, has sent to ridicule(H) the living God, and that he will rebuke(I) him for the words the Lord your God has heard. Therefore pray for the remnant(J) that still survives.”

When King Hezekiah’s officials came to Isaiah, Isaiah said to them, “Tell your master, ‘This is what the Lord says: Do not be afraid(K) of what you have heard—those words with which the underlings of the king of Assyria have blasphemed(L) me. Listen! When he hears a certain report,(M) I will make him want to return to his own country, and there I will have him cut down with the sword.(N)’”

When the field commander heard that the king of Assyria had left Lachish,(O) he withdrew and found the king fighting against Libnah.(P)

Now Sennacherib received a report that Tirhakah, the king of Cush,[a] was marching out to fight against him. So he again sent messengers to Hezekiah with this word: 10 “Say to Hezekiah king of Judah: Do not let the god you depend(Q) on deceive(R) you when he says, ‘Jerusalem will not be given into the hands of the king of Assyria.’ 11 Surely you have heard what the kings of Assyria have done to all the countries, destroying them completely. And will you be delivered? 12 Did the gods of the nations that were destroyed by my predecessors deliver(S) them—the gods of Gozan,(T) Harran,(U) Rezeph and the people of Eden who were in Tel Assar? 13 Where is the king of Hamath or the king of Arpad? Where are the kings of Lair, Sepharvaim, Hena and Ivvah?”(V)

Hezekiah’s Prayer(W)

14 Hezekiah received the letter(X) from the messengers and read it. Then he went up to the temple of the Lord and spread it out before the Lord. 15 And Hezekiah prayed to the Lord: “Lord, the God of Israel, enthroned between the cherubim,(Y) you alone(Z) are God over all the kingdoms of the earth. You have made heaven and earth. 16 Give ear,(AA) Lord, and hear;(AB) open your eyes,(AC) Lord, and see; listen to the words Sennacherib has sent to ridicule the living God.

17 “It is true, Lord, that the Assyrian kings have laid waste these nations and their lands. 18 They have thrown their gods into the fire and destroyed them, for they were not gods(AD) but only wood and stone, fashioned by human hands.(AE) 19 Now, Lord our God, deliver(AF) us from his hand, so that all the kingdoms(AG) of the earth may know(AH) that you alone, Lord, are God.”

Isaiah Prophesies Sennacherib’s Fall(AI)(AJ)

20 Then Isaiah son of Amoz sent a message to Hezekiah: “This is what the Lord, the God of Israel, says: I have heard(AK) your prayer concerning Sennacherib king of Assyria. 21 This is the word that the Lord has spoken against(AL) him:

“‘Virgin Daughter(AM) Zion
    despises(AN) you and mocks(AO) you.
Daughter Jerusalem
    tosses her head(AP) as you flee.
22 Who is it you have ridiculed and blasphemed?(AQ)
    Against whom have you raised your voice
and lifted your eyes in pride?
    Against the Holy One(AR) of Israel!
23 By your messengers
    you have ridiculed the Lord.
And you have said,(AS)
    “With my many chariots(AT)
I have ascended the heights of the mountains,
    the utmost heights of Lebanon.
I have cut down(AU) its tallest cedars,
    the choicest of its junipers.
I have reached its remotest parts,
    the finest of its forests.
24 I have dug wells in foreign lands
    and drunk the water there.
With the soles of my feet
    I have dried up all the streams of Egypt.”

25 “‘Have you not heard?(AV)
    Long ago I ordained it.
In days of old I planned(AW) it;
    now I have brought it to pass,
that you have turned fortified cities
    into piles of stone.(AX)
26 Their people, drained of power,(AY)
    are dismayed(AZ) and put to shame.
They are like plants in the field,
    like tender green shoots,(BA)
like grass sprouting on the roof,
    scorched(BB) before it grows up.

27 “‘But I know(BC) where you are
    and when you come and go
    and how you rage against me.
28 Because you rage against me
    and because your insolence has reached my ears,
I will put my hook(BD) in your nose
    and my bit(BE) in your mouth,
and I will make you return(BF)
    by the way you came.’

29 “This will be the sign(BG) for you, Hezekiah:

“This year you will eat what grows by itself,(BH)
    and the second year what springs from that.
But in the third year sow and reap,
    plant vineyards(BI) and eat their fruit.
30 Once more a remnant(BJ) of the kingdom of Judah
    will take root(BK) below and bear fruit above.
31 For out of Jerusalem will come a remnant,(BL)
    and out of Mount Zion a band of survivors.(BM)

“The zeal(BN) of the Lord Almighty will accomplish this.

32 “Therefore this is what the Lord says concerning the king of Assyria:

“‘He will not enter this city
    or shoot an arrow here.
He will not come before it with shield
    or build a siege ramp against it.
33 By the way that he came he will return;(BO)
    he will not enter this city,
declares the Lord.
34 I will defend(BP) this city and save it,
    for my sake and for the sake of David(BQ) my servant.’”

35 That night the angel of the Lord(BR) went out and put to death a hundred and eighty-five thousand in the Assyrian camp. When the people got up the next morning—there were all the dead bodies!(BS) 36 So Sennacherib king of Assyria broke camp and withdrew.(BT) He returned to Nineveh(BU) and stayed there.

37 One day, while he was worshiping in the temple of his god Nisrok, his sons Adrammelek(BV) and Sharezer killed him with the sword,(BW) and they escaped to the land of Ararat.(BX) And Esarhaddon(BY) his son succeeded him as king.

Footnotes

  1. 2 Kings 19:9 That is, the upper Nile region