Add parallel Print Page Options

Kulimbikitsa Zopereka

Ndipo tsopano, abale, tikufuna kuti mudziwe za chisomo chimene Mulungu wapereka ku mipingo ya ku Makedoniya. Pakati pa mayesero owawitsa, chimwemwe chawo chosefukira ndi umphawi wawo otheratu, anapereka mowolowamanja kwambiri. Motero ndikuchitira umboni kuti anapereka mmene akanathera, ndipo mwinanso kuposera mmene akathera kupereka. Anapereka mosakakamizidwa, ndipo anatipempha motiwumiriza kuti tiwapatse mwayi woti nawonso athandize anthu oyera mtima a ku Yudeya. Iwo anachita moposera mmene ife timayembekezera. Choyamba anadzipereka kwa Ambuye ndipo kenaka kwa ife monga mwa chifuniro cha Mulungu. Choncho tinamupempha Tito kuti atsirize poti nʼkuti atayamba kale ntchito yachisomoyi pakati panu. Popeza pa zinthu zonse munachita bwino, monga pachikhulupiriro, poyankhula, pachidziwitso, pakhama lambiri ndi pachikondi chanu pa ife, onetsetsani kuti muchitenso bwino pachisomo ichi chopereka.

Sindikukulamulirani, koma ndikufuna kuona ngati chikondi chanu nʼchoona pofananitsa ndi changu cha anthu ena. Pakuti mukudziwa chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu, kuti ngakhale anali wolemera, koma chifukwa cha inuyo anasanduka wosauka, kuti umphawi wakewo, inuyo mulemere.

10 Ndipo nawa malangizo anga pa zoyenera inu kuchita pa nkhaniyi. Chaka chatha munali oyamba, osati ongofuna kupereka kokha komanso okhala ndi mtima ofuna kupereka. 11 Tsopano tsirizani ntchitoyi, ndipo changu chanu chofunitsitsa kugwira ntchitoyi ndi kuyitsiriza chichitike molingana ndi zimene muli nazo. 12 Ndipo ngati mtima ofunitsitsa ulipo, mphatsoyo imalandiridwa molingana ndi zimene munthuyo ali nazo, osati zimene alibe.

13 Cholinga chathu sikuti tipeputse ena pamene inuyo mukuvutika, koma kuti pakhale kufanana. 14 Zambiri zimene muli nazo pakati panu muthandize nazo osowa, kuti nawonso akadzakhala nazo zambiri adzakuthandizeni pa zosowa zanu. Cholinga nʼkuchita mofanana, 15 monga kwalembedwa kuti, “Iye amene anatola zambiri sizinamutsalireko ndipo amene anatola pangʼono sizinamuchepere.”

Tito Atumidwa ku Korinto

16 Tithokoze Mulungu amene anayika mu mtima wa Tito changu chomwecho chimene ine ndili nacho pa inu. 17 Pakuti Tito sanangovomera kokha pempho lathu, koma yekha anafunitsitsa kwambiri kubwera kwa inu mwa iye yekha. 18 Ndipo tikumutumiza pamodzi ndi mʼbale amene mipingo yonse yamuyamikira chifukwa cha utumiki wake wa Uthenga Wabwino. 19 Chowonjezera china nʼchakuti anasankhidwa ndi mipingo kuti atiperekeze pamene ife tikukapereka zopereka, zimene tikuchita pofuna kupereka ulemu kwa Ambuye mwini ndi kuonetsa kufunitsitsa kwathu pothandiza. 20 Tikufuna kupewa kutikayikira kulikonse za mmene tikuyendetsera mphatso zochulukazi. 21 Pakuti tikuyesetsa kuchita zolondola, osati pamaso pa Ambuye pokha komanso pamaso pa anthu.

22 Kuwonjezera apo, tikuwatumiza pamodzi ndi mʼbale wathu, amene nthawi zambiri watitsimikizira mʼnjira zosiyanasiyana kuti ndi wachangu ndiponso chifukwa ali ndi chikhulupiriro chachikulu mwa inu. 23 Kunena za Tito, ndiye mnzanga ndi wogwira naye ntchito pakati panu. Kunena za abale athu, ndiwo oyimirira mipingo ndi olemekezetsa Khristu. 24 Choncho anthu amenewa atsimikizireni za chikondi chanu ndipo adziwe chifukwa chimene ife timakunyadirani, kuti mipingo yonse iwone chimenechi.

The Collection for the Lord’s People

And now, brothers and sisters, we want you to know about the grace that God has given the Macedonian(A) churches. In the midst of a very severe trial, their overflowing joy and their extreme poverty welled up in rich generosity.(B) For I testify that they gave as much as they were able,(C) and even beyond their ability. Entirely on their own, they urgently pleaded with us for the privilege of sharing(D) in this service(E) to the Lord’s people.(F) And they exceeded our expectations: They gave themselves first of all to the Lord, and then by the will of God also to us. So we urged(G) Titus,(H) just as he had earlier made a beginning, to bring also to completion(I) this act of grace on your part. But since you excel in everything(J)—in faith, in speech, in knowledge,(K) in complete earnestness and in the love we have kindled in you[a]—see that you also excel in this grace of giving.

I am not commanding you,(L) but I want to test the sincerity of your love by comparing it with the earnestness of others. For you know the grace(M) of our Lord Jesus Christ,(N) that though he was rich, yet for your sake he became poor,(O) so that you through his poverty might become rich.(P)

10 And here is my judgment(Q) about what is best for you in this matter. Last year you were the first not only to give but also to have the desire to do so.(R) 11 Now finish the work, so that your eager willingness(S) to do it may be matched by your completion of it, according to your means. 12 For if the willingness is there, the gift is acceptable according to what one has,(T) not according to what one does not have.

13 Our desire is not that others might be relieved while you are hard pressed, but that there might be equality. 14 At the present time your plenty will supply what they need,(U) so that in turn their plenty will supply what you need. The goal is equality, 15 as it is written: “The one who gathered much did not have too much, and the one who gathered little did not have too little.”[b](V)

Titus Sent to Receive the Collection

16 Thanks be to God,(W) who put into the heart(X) of Titus(Y) the same concern I have for you. 17 For Titus not only welcomed our appeal, but he is coming to you with much enthusiasm and on his own initiative.(Z) 18 And we are sending along with him the brother(AA) who is praised by all the churches(AB) for his service to the gospel.(AC) 19 What is more, he was chosen by the churches to accompany us(AD) as we carry the offering, which we administer in order to honor the Lord himself and to show our eagerness to help.(AE) 20 We want to avoid any criticism of the way we administer this liberal gift. 21 For we are taking pains to do what is right, not only in the eyes of the Lord but also in the eyes of man.(AF)

22 In addition, we are sending with them our brother who has often proved to us in many ways that he is zealous, and now even more so because of his great confidence in you. 23 As for Titus,(AG) he is my partner(AH) and co-worker(AI) among you; as for our brothers,(AJ) they are representatives of the churches and an honor to Christ. 24 Therefore show these men the proof of your love and the reason for our pride in you,(AK) so that the churches can see it.

Footnotes

  1. 2 Corinthians 8:7 Some manuscripts and in your love for us
  2. 2 Corinthians 8:15 Exodus 16:18