2 Akorinto 2
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
2 Kotero ndinatsimikiza maganizo anga kuti ndisachitenso ulendo wina owawa wobwera kwanuko. 2 Pakuti ngati ndikumvetsani chisoni, kodi angandisangalatse ndani, kupatula inuyo amene ndakumvetsani chisoni? 3 Nʼchifukwa chake ndinakulemberani monga ndinachitiramo kuti nditabwera kwanuko ndisadzamve chisoni ndi anthu oyenera kundisangalatsa. Ndinali ndi chikhulupiriro ndi inu nonse kuti inuyo mukakhala ndi chimwemwe poona kuti inenso ndili ndi chimwemwe. 4 Pakuti ndinakulemberani kalata ija ndili wopsinjika ndi wowawidwa mtima kwambiri ndi kutuluka misozi yambiri, osati pofuna kukumvetsani chisoni koma kuti ndikudziwitseni kuti ndimakukondani kwambiri.
Za Kukhululukira Wolakwa
5 Koma ngati wina wamvetsa chisoni, sanamvetse chisoni ine ndekha, koma koposa mosawonjezera wakhumudwitsa nonsenu, kunenatu mosawonjezera. 6 Chilango chimene ambiri a inu mwamupatsa munthu ameneyu nʼchokwanira. 7 Mʼmalo mwake tsono, muyenera kumukhululukira ndi kumulimbikitsa mtima kuti asamve chisoni choposa muyeso, angataye mtima. 8 Choncho ndikukupemphani kuti mutsimikizire chikondi chanu pa iye. 9 Cholinga china chimene ndinakulemberani kalata ija chinali chofuna kukuonani ngati mudzandimvera pa zonse. 10 Aliyense amene mumukhululukire, inenso ndimukhululukira. Ndipo ndikakhululukira, ngati pali kanthu koti ndikhululukire, ndiye kuti ndakhululuka chifukwa cha inu pamaso pa Khristu, 11 kupewa kuti Satana angapezere mpata pa ife, pajatu timadziwa machenjerero ake.
Atumiki a Pangano Latsopano
12 Tsono nditafika ku Trowa kuti ndilalikire Uthenga Wabwino wa Khristu, nʼkupeza kuti Ambuye anditsekulira khomo, 13 ndinasowa mtendere mu mtima mwanga, chifukwa sindinapezeko mʼbale wanga Tito. Choncho ndinatsanzikana ndi anthu kumeneko nʼkupita ku Makedoniya.
14 Koma tithokoze Mulungu amene amatitsogolera nthawi zonse monga ogwidwa ku nkhondo a Khristu pa chipambano chake. Tsono amatigwiritsa ntchito yofalitsa ponseponse nzeru zodziwira Khristu ngati fungo labwino. 15 Pakuti kwa Mulungu ndife fungo labwino la Khristu pakati pa iwo amene akupulumutsidwa ndi amene akuwonongeka. 16 Kwa amene akuwonongeka ndife fungo la imfa, limawapha. Ndipo kwa amene akupulumuka ndife fungo lamoyo, limawapatsa moyo. Ndani angayithe ntchito yotereyi? 17 Kusiyana ndi ena ambiri, ife sitilalikira Mawu a Mulungu kuti tipeza phindu. Mʼmalo mwake, ife mwa Khristu timayankhula pamaso pa Mulungu moona mtima, monga anthu otumidwa ndi Mulungu.
2 Corinthians 2
New International Version
2 1 So I made up my mind that I would not make another painful visit to you.(A) 2 For if I grieve you,(B) who is left to make me glad but you whom I have grieved? 3 I wrote as I did,(C) so that when I came I would not be distressed(D) by those who should have made me rejoice. I had confidence(E) in all of you, that you would all share my joy. 4 For I wrote you(F) out of great distress and anguish of heart and with many tears, not to grieve you but to let you know the depth of my love for you.
Forgiveness for the Offender
5 If anyone has caused grief,(G) he has not so much grieved me as he has grieved all of you to some extent—not to put it too severely. 6 The punishment(H) inflicted on him by the majority is sufficient. 7 Now instead, you ought to forgive and comfort him,(I) so that he will not be overwhelmed by excessive sorrow. 8 I urge you, therefore, to reaffirm your love for him. 9 Another reason I wrote you(J) was to see if you would stand the test and be obedient in everything.(K) 10 Anyone you forgive, I also forgive. And what I have forgiven—if there was anything to forgive—I have forgiven in the sight of Christ for your sake, 11 in order that Satan(L) might not outwit us. For we are not unaware of his schemes.(M)
Ministers of the New Covenant
12 Now when I went to Troas(N) to preach the gospel of Christ(O) and found that the Lord had opened a door(P) for me, 13 I still had no peace of mind,(Q) because I did not find my brother Titus(R) there. So I said goodbye to them and went on to Macedonia.(S)
14 But thanks be to God,(T) who always leads us as captives in Christ’s triumphal procession and uses us to spread the aroma(U) of the knowledge(V) of him everywhere. 15 For we are to God the pleasing aroma(W) of Christ among those who are being saved and those who are perishing.(X) 16 To the one we are an aroma that brings death;(Y) to the other, an aroma that brings life. And who is equal to such a task?(Z) 17 Unlike so many, we do not peddle the word of God for profit.(AA) On the contrary, in Christ we speak before God with sincerity,(AB) as those sent from God.(AC)
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.