Add parallel Print Page Options

Adzukulu a Benjamini ndi Sauli

Benjamini anabereka Bela mwana wake woyamba,

wachiwiri Asibeli, wachitatu Ahara,

wachinayi Noha ndipo wachisanu Rafa.

Ana a Bela anali awa:

Adari, Gera, Abihudi, Abisuwa, Naamani, Ahowa, Gera, Sefufani ndi Hiramu.

Zidzukulu za Ehudi, zimene zinali atsogoleri a mabanja a amene amakhala ku Geba ndipo zinasamutsidwa kupita ku Manahati zinali izi:

Naamani, Ahiya ndi Gera, amene anawasamutsa ndipo anabereka Uza ndi Ahihudi.

Saharaimu anabereka ana ku Mowabu atalekana ndi akazi ake, Husimu ndi Baara. Mwa mkazi wake Hodesi anabereka Yobabu, Zibiya, Mesa, Malikamu, 10 Yeusi, Sakiya ndi Mirima. Awa ndiye ana ake, atsogoleri a mabanja awo. 11 Mwa mkazi wake Husimu anabereka Abitubi ndi Elipaala.

12 Ana a Elipaala anali awa:

Eberi, Misamu, Semedi (amene anamanga mizinda ya Ono ndi Lodi ndi midzi yake yozungulira) 13 ndiponso Beriya ndi Sema, amene anali atsogoleri a mabanja a amene ankakhala ku Ayaloni ndipo anathamangitsa nzika za ku Gati.

14 Ahiyo, Sasaki, Yeremoti, 15 Zebadiya, Aradi, Ederi, 16 Mikayeli, Isipa ndi Yoha anali ana a Beriya.

17 Zebadiya, Mesulamu, Hiziki, Heberi, 18 Isimerai, Iziliya ndi Yobabu anali ana a Elipaala.

19 Yakimu, Zikiri, Zabidi, 20 Elienai, Ziletai, Elieli, 21 Adaya, Beraya ndi Simirati anali ana a Simei.

22 Isipani, Eberi, Elieli, 23 Abidoni, Zikiri, Hanani, 24 Hananiya, Elamu, Anitotiya, 25 Ifideya ndi Penueli anali ana a Sasaki.

26 Samuserai, Sehariya, Ataliya, 27 Yaaresiya, Eliya ndi Zikiri anali ana a Yerohamu.

28 Onsewa anali atsogoleri a mabanja, anthu otchuka potsata mibado yawo, ndipo ankakhala mu Yerusalemu.

29 Yeiyeli amene amabereka Gibiyoni ankakhala ku Gibiyoni.

Dzina la mkazi wake linali Maaka, 30 ndipo mwana wake woyamba anali Abidoni, motsatana ndi Zuri, Kisi, Baala, Neri, Nadabu, 31 Gedori, Ahiyo, Zekeri 32 ndi Mikiloti, amene anabereka Simea. Iwowa ankakhalanso ku Yerusalemu ndi abale awo.

33 Neri anabereka Kisi. Kisi anabereka Sauli, ndipo Sauli anabereka Yonatani, Maliki-Suwa, Abinadabu ndi Esibaala.

34 Mwana wa Yonatani anali

Meri-Baala, amene anabereka Mika.

35 Ana a Mika anali awa:

Pitoni, Meleki, Tareya ndi Ahazi.

36 Ahazi anabereka Yehoyada, Yehoyada anabereka Alemeti, Azimaveti ndi Zimuri, ndipo Zimuri anabereka Moza. 37 Moza anabereka Bineya. Ana ake anali Rafa, Eleasa ndi Azeli.

38 Azeli anali ndi ana asanu ndi mmodzi, ndipo mayina awo anali awa:

Azirikamu, Bokeru, Ismaeli, Seariya, Obadiya ndi Hanani. Onsewa anali ana a Azeli.

39 Ana a Eseki mʼbale wake anali awa:

Mwana wake woyamba Ulamu, wachiwiri Yeusi ndipo wachitatu Elifeleti. 40 Ana a Ulamu anali asilikali olimba mtima amene amadziwa kugwiritsa ntchito uta. Iwo anali ndi ana ndi adzukulu ambiri ndipo onse analipo 150.

Onsewa anali adzukulu a Benjamini.