Add parallel Print Page Options

Davide Apita ku Nobi

21 Davide anapita ku Nobi kwa wansembe Ahimeleki. Ahimelekiyo ankanjenjemera pamene ankamuchingamira, ndipo anafunsa kuti, “Muli nokha chifukwa chiyani? Chifukwa chiyani mulibe wokuperekezani?”

Davide anayankha Ahimeleki kuti, “Mfumu yandituma zinthu zina ndipo yandiwuza kuti, ‘Munthu aliyense asadziwe za zimene ndakutumazo.’ Kunena za anthu anga, ndawawuza kuti tikakumane pamalo pena pake. Kodi muli ndi chakudya? Patseniko malofu a buledi asanu, kapena chilichonse muli nacho.”

Koma wansembeyo anamuyankha Davide kuti, “Ine ndilibe buledi wamba woti ndikupatseni. Koma pali buledi wachipembedzo yekha. Ngati anthu amene muli nawo sanagone ndi akazi awo mukhoza kudya.”

Davide anayankha kuti, “Kunena zoona sitinakhudzane ndi mkazi monga timachitira nthawi zonse tikakhala pa ulendo. Anthu anga salola kudziyipitsa ndi mkazi ngakhale pa ulendo wamba. Nanji lero tili pa ulendo woterewu!” Choncho wansembe uja anamupatsa buledi wachipembedzo popeza kunalibeko buledi wina aliyense koma yekhayo amene amaperekedwa kwa Yehova. Uyu ndi amene anachotsedwa tsiku limenelo kuti ayikepo wina wotentha.

Koma tsiku limenelo mmodzi wa antchito a Sauli anali pomwepo kudikirira kuti achite mwambo wa chipembedzo mʼnyumba ya Mulungu. Munthuyu dzina lake anali Doegi Mwedomu, munthu wamphamvu pakati pa abusa a Sauli.

Davide anafunsa Ahimeleki kuti, “Kodi muli ndi mkondo kapena lupanga pano? Ine sindinatenge lupanga langa kapena chida china chilichonse chifukwa zimene andituma amfumu ndi zamsangamsanga.”

Wansembeyo anayankha kuti, “Kuno kuli lupanga la Goliati Mfilisiti uja amene unamupha mʼchigwa cha Ela, lakulungidwa mʼnsalu paseli pa Efodi. Ngati mufuna kulitenga, tengani popeza kuno kulibe lina koma lokhalo.”

Davide anati, “Palibe lina lofanana nalo. Ndipatseni lomwelo.”

Davide ku Gati

10 Tsiku lomwelo Davide ananyamuka kuthawa Sauli ndipo anapita kwa Akisi, mfumu wa ku Gati. 11 Koma nduna za Akisi zinafunsa mfumuyo kuti, “Kodi uyu si Davide mfumu ya dzikoli? Kodi iyeyu si uja pomuvinira ankayimba kuti,

“Sauli wapha 1,000,
    koma Davide wapha miyandamiyanda?”

12 Mawu amenewa anamulowa kwambiri Davide mu mtima ndipo anayamba kuopa kwambiri Akisi mfumu ya ku Gati. 13 Choncho anasintha makhalidwe ake pamaso pawo, nʼkudzisandutsa ngati wamisala. Iye ankangolembalemba pa zitseko za chipata ndi kumangotuluka dovi, nʼkumayenderera mʼndevu zake.

14 Akisi anawuza nduna zake kuti, “Mukumuona munthu uyu kuti ndi wamisala! Nʼchifukwa chiyani mukubwera naye kwa ine? 15 Kodi ine ndikusowa anthu amisala kuti muzibwera naye munthuyu kwa ine kuti azidzachita zamisala zake pamaso panga? Kodi munthu ameneyu nʼkulowa mʼnyumba mwanga?”

David at Nob

21 [a]David went to Nob,(A) to Ahimelek the priest. Ahimelek trembled(B) when he met him, and asked, “Why are you alone? Why is no one with you?”

David answered Ahimelek the priest, “The king sent me on a mission and said to me, ‘No one is to know anything about the mission I am sending you on.’ As for my men, I have told them to meet me at a certain place. Now then, what do you have on hand? Give me five loaves of bread, or whatever you can find.”

But the priest answered David, “I don’t have any ordinary bread(C) on hand; however, there is some consecrated(D) bread here—provided the men have kept(E) themselves from women.”

David replied, “Indeed women have been kept from us, as usual(F) whenever[b] I set out. The men’s bodies are holy(G) even on missions that are not holy. How much more so today!” So the priest gave him the consecrated bread,(H) since there was no bread there except the bread of the Presence that had been removed from before the Lord and replaced by hot bread on the day it was taken away.

Now one of Saul’s servants was there that day, detained before the Lord; he was Doeg(I) the Edomite,(J) Saul’s chief shepherd.

David asked Ahimelek, “Don’t you have a spear or a sword here? I haven’t brought my sword or any other weapon, because the king’s mission was urgent.”

The priest replied, “The sword(K) of Goliath(L) the Philistine, whom you killed in the Valley of Elah,(M) is here; it is wrapped in a cloth behind the ephod. If you want it, take it; there is no sword here but that one.”

David said, “There is none like it; give it to me.”

David at Gath

10 That day David fled from Saul and went(N) to Achish king of Gath. 11 But the servants of Achish said to him, “Isn’t this David, the king of the land? Isn’t he the one they sing about in their dances:

“‘Saul has slain his thousands,
    and David his tens of thousands’?”(O)

12 David took these words to heart and was very much afraid of Achish king of Gath. 13 So he pretended to be insane(P) in their presence; and while he was in their hands he acted like a madman, making marks on the doors of the gate and letting saliva run down his beard.

14 Achish said to his servants, “Look at the man! He is insane! Why bring him to me? 15 Am I so short of madmen that you have to bring this fellow here to carry on like this in front of me? Must this man come into my house?”

Footnotes

  1. 1 Samuel 21:1 In Hebrew texts 21:1-15 is numbered 21:2-16.
  2. 1 Samuel 21:5 Or from us in the past few days since