Add parallel Print Page Options

Sauli Ayesanso Kupha Davide

19 Sauli anawuza mwana wake Yonatani ndi nduna zake zonse kuti aphe Davide. Koma Yonatani amamukonda kwambiri Davide. Choncho anawuza Davide kuti, “Abambo anga Sauli akufuna kukupha. Tsono uchenjere. Mmawa upite ukabisale ndipo ukakhale komweko. Ine ndidzapita ndi kukayima pafupi ndi abambo anga ku munda kumene iwe ukabisale. Ndipo ndidzayankhula ndi abambo anga za iwe ndipo chilichonse chimene ndikamve ndidzakuwuza.”

Tsono Yonatani anakanena zabwino za Davide kwa abambo ake Sauli ndipo anati, “Mfumu musachimwire mtumiki wanu Davide, sanakuchimwireni, koma amakuchitirani zabwino kwambiri. Iye anayika moyo wake pa chiswe pamene anapha Mfilisiti uja. Choncho Yehova anachita zazikulu popambanitsa Aisraeli pa nkhondo. Inu munaona zonsezo ndipo munakondwera. Nanga nʼchifukwa chiyani mukufuna kuchimwira munthu wosalakwa pofuna kupha Davide?”

Sauli anamvera mawu a Yonatani ndipo analumbira kuti, “Pali Yehova, Davide sadzaphedwa.”

Pambuyo pake Yonatani anayitana Davide namuwuza zonsezi. Choncho Yonatani anabwera naye Davide kwa Sauli ndipo ankamutumikira Sauliyo monga kale.

Panabukanso nkhondo ina ndipo Davide anapita ndi kukamenyana ndi Afilisti. Iye anawakantha mwamphamvu kotero kuti Afilisti anathawa.

Tsiku lina mzimu woyipa uja unafikanso pa Sauli. Nthawi imeneyi nʼkuti Sauli uja ali mʼnyumba mwake, mkondo uli mʼdzanja lake ndi Davide akuyimba zeze, 10 Sauli anafuna kumubaya Davide ndi kumukhomera kukhoma, koma Davide anapewa mkondowo kotero Sauli anakabaya pa khoma. Usiku womwewo Davide anathawa.

11 Usiku womwewo Sauli anatumiza anthu ku nyumba ya Davide kuti akamubisalire ndi kumupha mmamawa. Koma Mikala mkazi wake anamuchenjeza nati, “Ngati usiku uno supulumutsa moyo wako, mawa udzaphedwa.” 12 Choncho Mikala anamutulutsira Davide pa zenera, ndipo anathawa ndi kupulumuka. 13 Kenaka Mikala anatenga fano naligoneka pa bedi nayika pilo wa ubweya wa mbuzi ku mutu kwa fanolo ndipo analifunditsa nsalu.

14 Pamene amithenga a Sauli aja anafika kuti akamugwire Davide, Mikala anati, “Davide akudwala.”

15 Koma Sauli anatumanso anthuwo kuti akamuone Davide, nati, “Mubwere naye kuno ali pa bedi pomwepo kuti ndidzamuphe.” 16 Koma pamene anthuwo analowa, anangoona fano pa bedipo ndi pilo wa ubweya wa mbuzi ku mutu kwake.

17 Tsono Sauli anafunsa Mikala kuti, “Nʼchifukwa chiyani wandinamiza chotere polola kuti mdani wanga athawe?”

Mikala anayankha kuti, “Davide anandiwuza kuti, ‘Ukapanda kutero ndikupha.’ ”

18 Choncho Davide anathawa napulumuka. Pambuyo pake anapita kwa Samueli ku Rama nakamuwuza zonse zimene Sauli anamuchita. Kenaka iye ndi Samueli anapita kukakhala ku Nayoti. 19 Sauli anamva kuti, “Davide ali ku Nayoti ku Rama.” 20 Choncho iye anatumiza anthu kuti akamugwire Davide. Koma anaona gulu la aneneri likulosera ndi Samueli akuwatsogolera. Pomwepo Mzimu wa Mulungu unawafikira ndipo nawonso anayamba kulosera. 21 Sauli atamva zimenezi anatumizanso anthu ena, koma nawonso anayamba kulosa. Anatumanso anthu ena kachitatu, koma nawonso anayamba kulosa. 22 Pomaliza Sauli mwini wake ananyamuka kupita ku Rama ndipo anafika ku chitsime chachikulu cha ku Seku. Ndipo anafunsa, “Samueli ndi Davide ali kuti?”

Munthu wina anamuyankha kuti, “Ali ku Nayoti ku Rama.”

23 Choncho Sauli anapita ku Nayoti ku Rama. Koma Mzimu wa Mulungu unafikanso pa iye ndipo ankalosa akuyenda mpaka anafika ku Nayoti. 24 Nayenso anavula zovala zake nayamba kulosa pamaso pa Samueli. Kenaka anagona wamaliseche tsiku lonse ndi usiku wonse. Nʼchifukwa chake anthu amati, “Kodi Sauli alinso mmodzi wa aneneri?”

Saul Tries to Kill David

19 Saul told his son Jonathan(A) and all the attendants to kill(B) David. But Jonathan had taken a great liking to David and warned him, “My father Saul is looking for a chance to kill you. Be on your guard tomorrow morning; go into hiding(C) and stay there. I will go out and stand with my father in the field where you are. I’ll speak(D) to him about you and will tell you what I find out.”

Jonathan spoke(E) well of David to Saul his father and said to him, “Let not the king do wrong(F) to his servant David; he has not wronged you, and what he has done has benefited you greatly. He took his life(G) in his hands when he killed the Philistine. The Lord won a great victory(H) for all Israel, and you saw it and were glad. Why then would you do wrong to an innocent(I) man like David by killing him for no reason?”

Saul listened to Jonathan and took this oath: “As surely as the Lord lives, David will not be put to death.”

So Jonathan called David and told him the whole conversation. He brought him to Saul, and David was with Saul as before.(J)

Once more war broke out, and David went out and fought the Philistines. He struck them with such force that they fled before him.

But an evil[a] spirit(K) from the Lord came on Saul as he was sitting in his house with his spear in his hand. While David was playing the lyre,(L) 10 Saul tried to pin him to the wall with his spear, but David eluded(M) him as Saul drove the spear into the wall. That night David made good his escape.

11 Saul sent men to David’s house to watch(N) it and to kill him in the morning.(O) But Michal, David’s wife, warned him, “If you don’t run for your life tonight, tomorrow you’ll be killed.” 12 So Michal let David down through a window,(P) and he fled and escaped. 13 Then Michal took an idol(Q) and laid it on the bed, covering it with a garment and putting some goats’ hair at the head.

14 When Saul sent the men to capture David, Michal said,(R) “He is ill.”

15 Then Saul sent the men back to see David and told them, “Bring him up to me in his bed so that I may kill him.” 16 But when the men entered, there was the idol in the bed, and at the head was some goats’ hair.

17 Saul said to Michal, “Why did you deceive me like this and send my enemy away so that he escaped?”

Michal told him, “He said to me, ‘Let me get away. Why should I kill you?’”

18 When David had fled and made his escape, he went to Samuel at Ramah(S) and told him all that Saul had done to him. Then he and Samuel went to Naioth and stayed there. 19 Word came to Saul: “David is in Naioth at Ramah”; 20 so he sent men to capture him. But when they saw a group of prophets(T) prophesying, with Samuel standing there as their leader, the Spirit of God came on(U) Saul’s men, and they also prophesied.(V) 21 Saul was told about it, and he sent more men, and they prophesied too. Saul sent men a third time, and they also prophesied. 22 Finally, he himself left for Ramah and went to the great cistern at Seku. And he asked, “Where are Samuel and David?”

“Over in Naioth at Ramah,” they said.

23 So Saul went to Naioth at Ramah. But the Spirit of God came even on him, and he walked along prophesying(W) until he came to Naioth. 24 He stripped(X) off his garments, and he too prophesied in Samuel’s(Y) presence. He lay naked all that day and all that night. This is why people say, “Is Saul also among the prophets?”(Z)

Footnotes

  1. 1 Samuel 19:9 Or But a harmful