Add parallel Print Page Options

Akulu Ampingo ndi Anyamata mu Mpingo

Ine ndikupempha akulu a mpingo amene ali pakati panu, monga inenso mkulu mnzawo, mboni ya zowawa za Khristu ndiponso amene ndidzalandira nawo ulemerero umene uti udzaonetsedwe. Wetani gulu la Mulungu limene lili mʼmanja mwanu, muziliyangʼanira. Muzichita osati mowumirizidwa, koma mwakufuna kwanu, monga momwe Mulungu akufunira kuti mutero. Musachite chifukwa chadyera la ndalama, koma ndi mtima ofuna kutumikira. Musakhale ngati mafumu pa amene mukuwayangʼanira, koma mukhale chitsanzo kwa gululo. Ndipo Mʼbusa wamkulu akadzaonekera, mudzalandira chipewa cha ulemerero chosafota.

Momwemonso, inu anyamata gonjerani amene ndi akulu. Inu nonse mukhale odzichepetsa kuti mutumikirane, chifukwa,

“Mulungu amatsutsana nawo odzikuza,
    koma amapereka chisomo kwa odzichepetsa.”

Choncho, mudzichepetse pamaso pa Mulungu wamphamvu, kuti pa nthawi yake adzakukwezeni. Tayani pa Iye nkhawa zanu zonse chifukwa ndiye amakusamalani.

Khalani odziretsa ndi atcheru. Mdani wanu mdierekezi amayendayenda monga mkango wobangula kufunafuna wina kuti amumeze. Mukaneni iye, ndipo mukhazikike mʼchikhulupiriro, chifukwa mukudziwa kuti abale anzanu pa dziko lonse lapansi nawonso akumva zowawa zomwezi.

10 Ndipo Mulungu wachisomo chonse, amene anakuyitanani ku ulemerero wake wamuyaya mwa Khristu, mutamva zowawa pa kanthawi, adzakukonzaninso ndi kukulimbitsani pa maziko olimba. 11 Kwa Iye kukhale mphamvu mpaka muyaya, Ameni.

Mawu Otsiriza

12 Mothandizidwa ndi Sila, amene ndi mʼbale wokhulupirika, ndakulemberani mwachidule kukulimbikitsani ndi kuchita umboni kuti ichi ndi chisomo choona cha Mulungu. 13 Imani mwamphamvu mʼchisomochi. Mlongo wanu amene ali ku Babuloni, wosankhidwa pamodzi nanu akupereka moni, nayenso Marko, mwana wanga, akupereka moni. 14 Mupatsane moni ndi mpsopsono wachikondi. Mtendere ukhale ndi inu nonse amene muli mwa Khristu.

To the Elders and the Flock

To the elders among you, I appeal as a fellow elder(A) and a witness(B) of Christ’s sufferings who also will share in the glory to be revealed:(C) Be shepherds of God’s flock(D) that is under your care, watching over them—not because you must, but because you are willing, as God wants you to be;(E) not pursuing dishonest gain,(F) but eager to serve; not lording it over(G) those entrusted to you, but being examples(H) to the flock. And when the Chief Shepherd(I) appears, you will receive the crown of glory(J) that will never fade away.(K)

In the same way, you who are younger, submit yourselves(L) to your elders. All of you, clothe yourselves with humility(M) toward one another, because,

“God opposes the proud
    but shows favor to the humble.”[a](N)

Humble yourselves, therefore, under God’s mighty hand, that he may lift you up in due time.(O) Cast all your anxiety on him(P) because he cares for you.(Q)

Be alert and of sober mind.(R) Your enemy the devil prowls around(S) like a roaring lion(T) looking for someone to devour. Resist him,(U) standing firm in the faith,(V) because you know that the family of believers throughout the world is undergoing the same kind of sufferings.(W)

10 And the God of all grace, who called you(X) to his eternal glory(Y) in Christ, after you have suffered a little while,(Z) will himself restore you and make you strong,(AA) firm and steadfast. 11 To him be the power for ever and ever. Amen.(AB)

Final Greetings

12 With the help of Silas,[b](AC) whom I regard as a faithful brother, I have written to you briefly,(AD) encouraging you and testifying that this is the true grace of God. Stand fast in it.(AE)

13 She who is in Babylon, chosen together with you, sends you her greetings, and so does my son Mark.(AF) 14 Greet one another with a kiss of love.(AG)

Peace(AH) to all of you who are in Christ.

Footnotes

  1. 1 Peter 5:5 Prov. 3:34
  2. 1 Peter 5:12 Greek Silvanus, a variant of Silas