Add parallel Print Page Options

Aisraeli onse analembedwa potsata mibado yawo mʼbuku la mafumu a Aisraeli.

Anthu a ku Yerusalemu

Anthu a ku Yuda anatengedwa kunka ku ukapolo ku Babuloni chifukwa cha kusakhulupirika kwawo. Tsono anthu oyamba kukhala mʼmadera awo anali Aisraeli wamba, ansembe, Alevi ndi otumikira ku Nyumba ya Yehova.

Anthu a ku Yuda, Benjamini ndi Efereimu ndiponso Manase amene anakhala mu Yerusalemu anali awa:

Utai mwana wa Amihudi, mwana wa Omuri, mwana wa Imuri, mwana wa Bani, chidzukulu cha Perezi mwana wa Yuda.

A banja la Siloni:

Asaya mwana wake woyamba pamodzi ndi ana ake.

A banja la Zera:

Yeueli.

Anthu ochokera ku Yuda analipo 690.

A fuko la Benjamini:

Salu mwana wa Mesulamu, mwana wa Hodaviya, mwana wa Hasenuya;

Ibineya mwana wa Yerohamu; Ela mwana wa Uzi, mwana wa Mikiri; ndi Mesulamu mwana wa Sefatiya, mwana wa Reueli mwana wa Ibiniya.

Anthu ochokera ku Benjamini monga analembedwera mwa mibado yawo, analipo 956. Anthu onsewa anali atsogoleri a mabanja awo.

10 Ansembe:

Yedaya, Yehoyaribu; Yakini;

11 Azariya mwana wa Hilikiya, mwana wa Mesulamu, mwana wa Zadoki mwana wa Merayoti, mwana wa Ahitubi, wamkulu woyangʼanira Nyumba ya Mulungu;

12 Adaya mwana wa Yerohamu, mwana wa Pasi-Huri, mwana wa Malikiya; ndi Maasai mwana wa Adieli, mwana wa Yahizera, mwana wa Mesulamu, mwana wa Mesilemoti, mwana wa Imeri.

13 Ansembe amene anali atsogoleri a mabanja awo analipo 1,760. Anali anthu amphamvu ndi odziwa kutumikira mʼnyumba ya Mulungu.

14 Alevi:

Semaya mwana wa Hasubu, mwana wa Azirikamu, mwana wa Hasabiya, wa mʼbanja la Merari; 15 Bakibakara, Heresi, Galali ndi Mataniya mwana wa Mika, mwana wa Zikiri, mwana wa Asafu; 16 Obadiya mwana wa Semaya mwana wa Galali, mwana wa Yedutuni ndi Berekiya mwana wa Asa, mwana wa Elikana, amene ankakhala ku midzi ya Anetofati.

17 Alonda a pa makomo:

Salumu, Akubu, Talimoni, Ahimani ndi abale awo. Mtsogoleri wawo anali Salumu. 18 Amenewa amakhala pa chipata cha mfumu kummawa mpaka lero lino. Alonda a gulu la Alevi anali awa: 19 Salumu mwana wa Kore, mwana wa Ebiyasafu, mwana wa Kora, pamodzi ndi abale ake a ku banja la makolo ake, Akora aja ankanyangʼanira khomo la Tenti monga ankachitira abambo awo polondera khomo la malo okhalapo Yehova. 20 Masiku oyamba Finehasi mwana wa Eliezara anali woyangʼanira alonda apakhomo ndipo Yehova anali naye. 21 Zekariya mwana wa Meselemiya anali mlonda woyangʼanira pa chipata cha tenti ya msonkhano.

22 Onse amene anasankhidwa kukhala alonda pa khonde analipo 212. Iwo analembedwa mwa mibado yawo ku midzi yawo. Davide ndi mneneri Samueli ndiwo anawayika mʼmalo awo antchito chifukwa cha kukhulupirika kwawo. 23 Iwo ndi zidzukulu zawo anali oyangʼanira zipata za nyumba ya Yehova imene imatchedwa Tenti. 24 Alonda apakhomowa anali mbali zonse zinayi: kummawa, kumadzulo, kumpoto ndi kummwera. 25 Abale awo a ku midzi yawo amabwera nthawi ndi nthawi kudzagwira ntchito yawo kwa masiku asanu ndi awiri. 26 Koma atsogoleri akuluakulu anayi a alonda, amene anali Alevi, anapatsidwa udindo woyangʼanira zipinda ndi chuma cha nyumba ya Mulungu. 27 Iwo amakhala usiku wonse atayima mozungulira Nyumba ya Mulungu, chifukwa anayenera kuyilondera. Ndipo anali ndi kiyi wotsekulira mmawa uliwonse.

28 Ena amayangʼanira zipangizo zimene amagwiritsa ntchito pa ntchito mʼNyumba ya Mulungu. Iwo amaziwerenga zikamalowetsedwa ndi potulutsidwa. 29 Ena anapatsidwa udindo wosamalira zipangizo ndi zinthu zina zonse za ku malo opatulika, pamodzi ndi ufa, vinyo, mafuta, lubani ndi zonunkhira. 30 Koma ansembe ena amasakaniza zonunkhirazo. 31 Mlevi wotchedwa Matitiya mwana woyamba wa Salumu wa mʼbanja la Kora, anapatsidwa udindo woyangʼanira zophikidwa mʼziwaya. 32 Abale ake ena a mʼbanja la Akohati amaphika buledi wa pa Sabata lililonse amene amayikidwa pa tebulo.

33 Atsogoleri a mabanja a Alevi, amene anali ndi luso loyimba, amakhala mʼzipinda za Nyumba ya Mulungu ndipo samagwira ntchito zina chifukwa ankatumikira usana ndi usiku.

34 Onsewa anali atsogoleri a mabanja a Alevi, akuluakulu monga analembedwera pa mibado yawo, ndipo ankakhala mu Yerusalemu.

Mibado ya Sauli

35 Yeiyeli abambo a Gibiyoni ankakhala ku Gibiyoni.

Dzina la akazi awo linali Maaka, 36 ndipo mwana wawo woyamba kubadwa anali Abidoni, motsatana ndi Zuri, Kisi, Baala, Neri, Nadabu, 37 Gedori, Ahiyo, Zekariya ndi Mikiloti. 38 Mikiloti anabereka Simeamu. Iwonso ankakhala ndi abale awo ku Yerusalemu.

39 Neri anabereka Kisi, Kisi anabereka Sauli, ndipo Sauli anabereka Yonatani, Maliki-Suwa, Abinadabu ndi Esibaala.

40 Mwana wa Yonatani anali

Meri-Baala, amene anabereka Mika.

41 Ana a Mika anali:

Pitoni, Meleki, Tahireya ndi Ahazi.

42 Ahazi anabereka Yara, Yara anabereka Alemeti, Azimaveti ndi Zimuri, ndipo Zimiri anabereka Moza. 43 Moza anabereka Bineya. Ana ake anali Refaya, Eleasa ndi Azeli.

44 Azeli anali ndi ana asanu ndi mmodzi ndipo mayina awo anali awa:

Azirikamu, Bokeru, Ismaeli, Seariya, Obadiya ndi Hanani. Awa anali ana a Azeli.

All Israel(A) was listed in the genealogies recorded in the book of the kings of Israel and Judah. They were taken captive to Babylon(B) because of their unfaithfulness.(C)

The People in Jerusalem(D)

Now the first to resettle on their own property in their own towns(E) were some Israelites, priests, Levites and temple servants.(F)

Those from Judah, from Benjamin, and from Ephraim and Manasseh who lived in Jerusalem were:

Uthai son of Ammihud, the son of Omri, the son of Imri, the son of Bani, a descendant of Perez son of Judah.(G)

Of the Shelanites[a]:

Asaiah the firstborn and his sons.

Of the Zerahites:

Jeuel.

The people from Judah numbered 690.

Of the Benjamites:

Sallu son of Meshullam, the son of Hodaviah, the son of Hassenuah;

Ibneiah son of Jeroham; Elah son of Uzzi, the son of Mikri; and Meshullam son of Shephatiah, the son of Reuel, the son of Ibnijah.

The people from Benjamin, as listed in their genealogy, numbered 956. All these men were heads of their families.

10 Of the priests:

Jedaiah; Jehoiarib; Jakin;

11 Azariah son of Hilkiah, the son of Meshullam, the son of Zadok, the son of Meraioth, the son of Ahitub, the official in charge of the house of God;

12 Adaiah son of Jeroham, the son of Pashhur,(H) the son of Malkijah; and Maasai son of Adiel, the son of Jahzerah, the son of Meshullam, the son of Meshillemith, the son of Immer.

13 The priests, who were heads of families, numbered 1,760. They were able men, responsible for ministering in the house of God.

14 Of the Levites:

Shemaiah son of Hasshub, the son of Azrikam, the son of Hashabiah, a Merarite; 15 Bakbakkar, Heresh, Galal and Mattaniah(I) son of Mika, the son of Zikri, the son of Asaph; 16 Obadiah son of Shemaiah, the son of Galal, the son of Jeduthun; and Berekiah son of Asa, the son of Elkanah, who lived in the villages of the Netophathites.(J)

17 The gatekeepers:(K)

Shallum, Akkub, Talmon, Ahiman and their fellow Levites, Shallum their chief 18 being stationed at the King’s Gate(L) on the east, up to the present time. These were the gatekeepers belonging to the camp of the Levites. 19 Shallum(M) son of Kore, the son of Ebiasaph, the son of Korah, and his fellow gatekeepers from his family (the Korahites) were responsible for guarding the thresholds of the tent just as their ancestors had been responsible for guarding the entrance to the dwelling of the Lord. 20 In earlier times Phinehas(N) son of Eleazar was the official in charge of the gatekeepers, and the Lord was with him. 21 Zechariah(O) son of Meshelemiah was the gatekeeper at the entrance to the tent of meeting.

22 Altogether, those chosen to be gatekeepers(P) at the thresholds numbered 212. They were registered by genealogy in their villages. The gatekeepers had been assigned to their positions of trust by David and Samuel the seer.(Q) 23 They and their descendants were in charge of guarding the gates of the house of the Lord—the house called the tent of meeting. 24 The gatekeepers were on the four sides: east, west, north and south. 25 Their fellow Levites in their villages had to come from time to time and share their duties for seven-day(R) periods. 26 But the four principal gatekeepers, who were Levites, were entrusted with the responsibility for the rooms and treasuries(S) in the house of God. 27 They would spend the night stationed around the house of God,(T) because they had to guard it; and they had charge of the key(U) for opening it each morning.

28 Some of them were in charge of the articles used in the temple service; they counted them when they were brought in and when they were taken out. 29 Others were assigned to take care of the furnishings and all the other articles of the sanctuary,(V) as well as the special flour and wine, and the olive oil, incense and spices. 30 But some(W) of the priests took care of mixing the spices. 31 A Levite named Mattithiah, the firstborn son of Shallum the Korahite, was entrusted with the responsibility for baking the offering bread. 32 Some of the Kohathites, their fellow Levites, were in charge of preparing for every Sabbath the bread set out on the table.(X)

33 Those who were musicians,(Y) heads of Levite families, stayed in the rooms of the temple and were exempt from other duties because they were responsible for the work day and night.(Z)

34 All these were heads of Levite families, chiefs as listed in their genealogy, and they lived in Jerusalem.

The Genealogy of Saul(AA)

35 Jeiel(AB) the father[b] of Gibeon lived in Gibeon.

His wife’s name was Maakah, 36 and his firstborn son was Abdon, followed by Zur, Kish, Baal, Ner, Nadab, 37 Gedor, Ahio, Zechariah and Mikloth. 38 Mikloth was the father of Shimeam. They too lived near their relatives in Jerusalem.

39 Ner(AC) was the father of Kish,(AD) Kish the father of Saul, and Saul the father of Jonathan,(AE) Malki-Shua, Abinadab and Esh-Baal.[c](AF)

40 The son of Jonathan:

Merib-Baal,[d](AG) who was the father of Micah.

41 The sons of Micah:

Pithon, Melek, Tahrea and Ahaz.[e]

42 Ahaz was the father of Jadah, Jadah[f] was the father of Alemeth, Azmaveth and Zimri, and Zimri was the father of Moza. 43 Moza was the father of Binea; Rephaiah was his son, Eleasah his son and Azel his son.

44 Azel had six sons, and these were their names:

Azrikam, Bokeru, Ishmael, Sheariah, Obadiah and Hanan. These were the sons of Azel.

Footnotes

  1. 1 Chronicles 9:5 See Num. 26:20; Hebrew Shilonites.
  2. 1 Chronicles 9:35 Father may mean civic leader or military leader.
  3. 1 Chronicles 9:39 Also known as Ish-Bosheth
  4. 1 Chronicles 9:40 Also known as Mephibosheth
  5. 1 Chronicles 9:41 Vulgate and Syriac (see also Septuagint and 8:35); Hebrew does not have and Ahaz.
  6. 1 Chronicles 9:42 Some Hebrew manuscripts and Septuagint (see also 8:36); most Hebrew manuscripts Jarah, Jarah