Add parallel Print Page Options

Mabanja Ena a Yuda

Ana a Yuda anali awa:

Perezi, Hezironi, Karimi, Huri ndi Sobali.

Reaya mwana wa Sobala anabereka Yahati, ndipo Yahati anabereka Ahumai ndi Lahadi. Awa anali mabanja a Azorati.

Ana a Etamu anali awa:

Yezireeli, Isima ndi Idibasi. Dzina la mlongo wawo linali Hazeleliponi. Penueli anabereka Gedori, ndipo Ezeri anabereka Husa.

Awa anali ana a Huri, mwana wachisamba wa Efurata ndi abambo a Betelehemu.

Asihuri abambo a Tekowa anali ndi akazi awiri, Hela ndi Naara.

Naara anamuberekera Ahuzamu, Heferi, Temani ndi Haahasitari. Awa ndiwo anali ana a Naara.

Ana a Hela:

Zereti, Zohari, Etinani, ndi Kozi, amene anali abambo ake a Anubi ndi Hazo-Beba ndi mabanja a Ahariheli mwana wa Harumi.

Yabesi anali munthu wolemekezeka kwambiri kuposa abale ake. Amayi ake anamutcha Yabesi kutanthauza kuti, “Chifukwa ndinamubala ndi ululu wambiri.” 10 Yabesi analira kwa Mulungu wa Israeli kuti, “Mundidalitse ndipo mukulitse dziko langa! Dzanja lanu likhale pa ine ndipo mundisunge kuti choyipa chisandigwere ndi kundisautsa.” Ndipo Mulungu anamupatsa chopempha chakecho.

11 Kelubi, mʼbale wa Suha, anabereka Mehiri, amene anabereka Esitoni. 12 Esitoni anabereka Beti-Rafa, Paseya ndi Tehina amene anabereka Iri Nahasi. Amenewa ndiwo anthu a ku Reka.

13 Ana a Kenazi anali awa:

Otanieli ndi Seraya.

Ana a Otanieli anali awa:

Hatati ndi Meonotai. 14 Meonotai anabereka Ofura.

Seraya anabereka Yowabu,

amene anabereka Ge-Harasimu. Anawatcha dzina ili chifukwa anthu ake anali amisiri.

15 Ana a Kalebe mwana wa Yefune anali awa:

Iru, Ela ndi Naama.

Mwana wa Ela anali

Kenazi.

16 Ana a Yehaleleli anali awa:

Zifi, Zifa, Tiriya ndi Asareli.

17 Ana a Ezara anali awa:

Yeteri, Meredi, Eferi ndi Yaloni. Mmodzi mwa akazi a Meredi anabereka Miriamu, Samai ndi Isiba abambo ake a Esitemowa. 18 (Mkazi wake wa Chiyuda anabereka Yaredi abambo ake a Gedori, Heberi abambo ake a Soko ndi Yekutieli abambo a Zanowa). Awa anali ana a mwana wamkazi wa Farao, Bitia, amene Meredi anakwatira.

19 Ana a mkazi wa Hodiya, mlongo wa Nahamu anali awa:

abambo ake a Keila wa ku Garimi ndi Esitemowa wa ku Maaka.

20 Ana a Simeoni anali awa:

Amnoni, Rina, Beni-Hanani ndi Tiloni.

Ana a Isi anali awa:

Zoheti ndi Beni-Zoheti.

21 Ana a Sela mwana wa Yuda anali awa:

Eri amene anabereka Leka, Laada amene anabereka Maresa ndi mabanja a anthu owomba nsalu zofewa ndi zosalala a ku Beti-Asibeya, 22 Yokimu, anthu a ku Kozeba, ndiponso Yowasi ndi Sarafi, amene ankalamulira Mowabu ndi Yasibu-Lehemu. (Nkhani zimenezi ndi zakalekale). 23 Iwo anali owumba mbiya amene ankakhala ku Netaimu ndi Gederi. Ankakhala kumeneko ndi kumatumikira mfumu.

Simeoni

24 Ana a Simeoni anali awa:

Nemueli, Yamini, Yaribu, Zera ndi Sauli;

25 Salumu anali mwana wa Sauli, Mibisamu anali mwana wa Salumu ndipo Misima anali mwana wa Mibisamu.

26 Zidzukulu za Misima zinali izi:

Hamueli, Zakuri ndi Simei.

27 Simei anali ndi ana aamuna 16 ndi ana aakazi 6, koma abale ake sanabereke ana ambiri; kotero banja lawo silinakule ngati anthu ena a ku Yuda. 28 Iwo amakhala ku Beeriseba, Molada, Hazari-Suwali, 29 Biliha, Ezemu, Toladi, 30 Betueli, Horima, Zikilagi, 31 Beti-Marikaboti, Hazari-Susimu, Beti-Biri ndi Saaraimu. Iyi inali mizinda yawo mpaka pa nthawi ya ulamuliro wa Davide. 32 Midzi yowazungulira inali Etamu, Aini, Rimoni, Tokeni ndi Asani, midzi isanu 33 ndi midzi yonse yozungulira mizinda imeneyi mpaka ku Baala. Awa anali malo awo okhalapo. Ndipo anasunga mbiri ya makolo awo.

34 Mesobabu, Yamuleki, Yosa mwana wa Amaziya, 35 Yoweli, Yehu mwana wa Yosibiya, mwana wa Seraya, mwana wa Asieli, 36 komanso Eliyoenai, Yaakoba, Yesohaya, Asaya, Adieli, Yesimieli, Benaya, 37 ndiponso Ziza mwana wa Sifi, mwana wa Aloni, mwana wa Yedaya, mwana wa Simiri, mwana wa Semaya.

38 Anthu amene atchulidwawa anali atsogoleri a mabanja awo. Mabanja awo anakula kwambiri 39 ndipo anakafika ku malire a Gedori ku chigwa cha kummawa kufuna msipu wodyetsa ziweto zawo. 40 Anapeza msipu wobiriwira ndi wabwino ndipo dziko linali lalikulu, la mtendere ndi bata. Kumeneko kunkakhala fuko la Hamu poyamba.

41 Anthu amene mayina awowa alembedwa, anabwera pa nthawi ya Hezekiya mfumu ya Yuda. Iwo anathira nkhondo fuko la Hamu mʼmalo awo amene amakhala komanso Ameuni amene anali kumeneko ndipo anawononga onsewo kotero kuti mbiri yawo simvekanso mpaka lero lino. Kotero iwo anakhala mʼmalo awo chifukwa kunali msipu wa ziweto zawo. 42 Ndipo anthu 500 a fuko la Simeoni, motsogozedwa ndi Pelatiya, Neariya, Refaya ndi Uzieli, ana a Isi, analanda dziko lamapiri la Seiri. 43 Iwo anapha Aamaleki otsala amene anali atapulumuka ndipo akukhala kumeneko mpaka lero lino.

Other Clans of Judah

The descendants of Judah:(A)

Perez, Hezron,(B) Karmi, Hur and Shobal.

Reaiah son of Shobal was the father of Jahath, and Jahath the father of Ahumai and Lahad. These were the clans of the Zorathites.

These were the sons[a] of Etam:

Jezreel, Ishma and Idbash. Their sister was named Hazzelelponi. Penuel was the father of Gedor, and Ezer the father of Hushah.

These were the descendants of Hur,(C) the firstborn of Ephrathah and father[b] of Bethlehem.(D)

Ashhur(E) the father of Tekoa had two wives, Helah and Naarah.

Naarah bore him Ahuzzam, Hepher, Temeni and Haahashtari. These were the descendants of Naarah.

The sons of Helah:

Zereth, Zohar, Ethnan, and Koz, who was the father of Anub and Hazzobebah and of the clans of Aharhel son of Harum.

Jabez was more honorable than his brothers. His mother had named him Jabez,[c] saying, “I gave birth to him in pain.” 10 Jabez cried out to the God of Israel, “Oh, that you would bless me and enlarge my territory! Let your hand be with me, and keep me from harm so that I will be free from pain.” And God granted his request.

11 Kelub, Shuhah’s brother, was the father of Mehir, who was the father of Eshton. 12 Eshton was the father of Beth Rapha, Paseah and Tehinnah the father of Ir Nahash.[d] These were the men of Rekah.

13 The sons of Kenaz:

Othniel(F) and Seraiah.

The sons of Othniel:

Hathath and Meonothai.[e] 14 Meonothai was the father of Ophrah.

Seraiah was the father of Joab,

the father of Ge Harashim.[f] It was called this because its people were skilled workers.

15 The sons of Caleb son of Jephunneh:

Iru, Elah and Naam.

The son of Elah:

Kenaz.

16 The sons of Jehallelel:

Ziph, Ziphah, Tiria and Asarel.

17 The sons of Ezrah:

Jether, Mered, Epher and Jalon. One of Mered’s wives gave birth to Miriam,(G) Shammai and Ishbah the father of Eshtemoa. 18 (His wife from the tribe of Judah gave birth to Jered the father of Gedor, Heber the father of Soko, and Jekuthiel the father of Zanoah.(H)) These were the children of Pharaoh’s daughter Bithiah, whom Mered had married.

19 The sons of Hodiah’s wife, the sister of Naham:

the father of Keilah(I) the Garmite, and Eshtemoa the Maakathite.(J)

20 The sons of Shimon:

Amnon, Rinnah, Ben-Hanan and Tilon.

The descendants of Ishi:

Zoheth and Ben-Zoheth.

21 The sons of Shelah(K) son of Judah:

Er the father of Lekah, Laadah the father of Mareshah and the clans of the linen workers at Beth Ashbea, 22 Jokim, the men of Kozeba, and Joash and Saraph, who ruled in Moab and Jashubi Lehem. (These records are from ancient times.) 23 They were the potters who lived at Netaim and Gederah; they stayed there and worked for the king.

Simeon(L)

24 The descendants of Simeon:(M)

Nemuel, Jamin, Jarib,(N) Zerah and Shaul;

25 Shallum was Shaul’s son, Mibsam his son and Mishma his son.

26 The descendants of Mishma:

Hammuel his son, Zakkur his son and Shimei his son.

27 Shimei had sixteen sons and six daughters, but his brothers did not have many children; so their entire clan did not become as numerous as the people of Judah. 28 They lived in Beersheba,(O) Moladah,(P) Hazar Shual, 29 Bilhah, Ezem,(Q) Tolad, 30 Bethuel, Hormah,(R) Ziklag,(S) 31 Beth Markaboth, Hazar Susim, Beth Biri and Shaaraim.(T) These were their towns until the reign of David. 32 Their surrounding villages were Etam, Ain,(U) Rimmon, Token and Ashan(V)—five towns— 33 and all the villages around these towns as far as Baalath.[g] These were their settlements. And they kept a genealogical record.

34 Meshobab, Jamlech, Joshah son of Amaziah, 35 Joel, Jehu son of Joshibiah, the son of Seraiah, the son of Asiel, 36 also Elioenai, Jaakobah, Jeshohaiah, Asaiah, Adiel, Jesimiel, Benaiah, 37 and Ziza son of Shiphi, the son of Allon, the son of Jedaiah, the son of Shimri, the son of Shemaiah.

38 The men listed above by name were leaders of their clans. Their families increased greatly, 39 and they went to the outskirts of Gedor(W) to the east of the valley in search of pasture for their flocks. 40 They found rich, good pasture, and the land was spacious, peaceful and quiet.(X) Some Hamites had lived there formerly.

41 The men whose names were listed came in the days of Hezekiah king of Judah. They attacked the Hamites in their dwellings and also the Meunites(Y) who were there and completely destroyed[h] them, as is evident to this day. Then they settled in their place, because there was pasture for their flocks. 42 And five hundred of these Simeonites, led by Pelatiah, Neariah, Rephaiah and Uzziel, the sons of Ishi, invaded the hill country of Seir.(Z) 43 They killed the remaining Amalekites(AA) who had escaped, and they have lived there to this day.

Footnotes

  1. 1 Chronicles 4:3 Some Septuagint manuscripts (see also Vulgate); Hebrew father
  2. 1 Chronicles 4:4 Father may mean civic leader or military leader; also in verses 12, 14, 17, 18 and possibly elsewhere.
  3. 1 Chronicles 4:9 Jabez sounds like the Hebrew for pain.
  4. 1 Chronicles 4:12 Or of the city of Nahash
  5. 1 Chronicles 4:13 Some Septuagint manuscripts and Vulgate; Hebrew does not have and Meonothai.
  6. 1 Chronicles 4:14 Ge Harashim means valley of skilled workers.
  7. 1 Chronicles 4:33 Some Septuagint manuscripts (see also Joshua 19:8); Hebrew Baal
  8. 1 Chronicles 4:41 The Hebrew term refers to the irrevocable giving over of things or persons to the Lord, often by totally destroying them.