Add parallel Print Page Options

Moyo Wokondweretsa Mulungu

Potsiriza, abale, tinakulangizani kale momwe mukuyenera kukhalira kuti mukondweretse Mulungu, monga momwe mukukhaliramo. Tsopano tikukupemphani ndi kukulimbikitsani mwa Ambuye Yesu kuti muchite zimenezi koposa kale. Inu mukudziwa malangizo amene tinakupatsani mwa ulamuliro wa Ambuye Yesu.

Ndi chifuniro cha Mulungu kuti muyeretsedwe: kuti mupewe dama; aliyense wa inu aphunzire kulamulira thupi lake mʼnjira yoyera ndi yaulemu, osati yotsata chilakolako chonyansa monga amachitira akunja, amene sadziwa Mulungu. Pa zimenezi munthu asachimwire mʼbale wake kapena kumuonerera. Ambuye adzalanga anthu onse amene amachita machimo amenewa, monga tinakuwuzani kale ndi kukuchenjezani. Pakuti Mulungu sanatiyitane kuti tizichita zonyansa, koma kuti tikhale oyera mtima. Choncho, aliyense amene akukana malangizo awa sakukana munthu koma Mulungu, Mulungu weniweniyo amene amakupatsani Mzimu Woyera.

Tsono kunena za kukondana wina ndi mnzake, nʼkosafunikira kuti tikulembereni, popeza ndi Mulungu amene anakuphunzitsani za kukondana wina ndi mnzake. 10 Ndipo kunena zoona, mumakonda abale onse a mʼbanja la Mulungu a ku Makedoniya. Komabe, abale tikukulimbikitsani kuti muzichita zimenezi koposa kale.

11 Yesetsani kuti mukhale moyo wofatsa. Aliyense asamale ntchito yakeyake ndi kugwira ntchito ndi manja ake. 12 Mukatero akunja adzalemekeza makhalidwe anu a tsiku ndi tsiku, ndi kuti inuyo mukhale osadalira wina aliyense.

Kubweranso kwa Ambuye

13 Abale, ife sitikufuna mukhale osadziwa za amene akugona, kapena kumva chisoni ngati anthu ena opanda chiyembekezo. 14 Ife timakhulupirira kuti Yesu anamwalira naukanso. Moteronso timakhulupirira kuti amene anamwalira ali mwa Yesu, Mulungu adzawaukitsa nʼkubwera nawo pamodzi ndi Yesuyo. 15 Molingana ndi mawu a Ambuye mwini, tikukuwuzani kuti, ife amene tikanali ndi moyo, otsala mpaka kubwera kwa Ambuye, sitidzawasiya kumbuyo amene anagona kale. 16 Pakuti Ambuye mwini adzatsika kuchokera kumwamba, ndi mfuwu waulamuliro, ndi liwu la mngelo wamkulu, ndi kulira kwa lipenga la Mulungu, ndipo akufa amene ali mwa Yesu adzauka poyamba. 17 Kenaka, ife amene tili ndi moyo, otsalafe, tidzakwatulidwa pamodzi ndi iwo mʼmitambo kukakumana ndi Ambuye mlengalenga. Tsono ife tidzakhala ndi Ambuye mpaka muyaya. 18 Nʼchifukwa chake tsono muzilimbikitsana ndi mawu amenewa.

Living to Please God

As for other matters, brothers and sisters,(A) we instructed you how to live(B) in order to please God,(C) as in fact you are living. Now we ask you and urge you in the Lord Jesus to do this more and more. For you know what instructions we gave you by the authority of the Lord Jesus.

It is God’s will(D) that you should be sanctified: that you should avoid sexual immorality;(E) that each of you should learn to control your own body[a](F) in a way that is holy and honorable, not in passionate lust(G) like the pagans,(H) who do not know God;(I) and that in this matter no one should wrong or take advantage of a brother or sister.[b](J) The Lord will punish(K) all those who commit such sins,(L) as we told you and warned you before. For God did not call us to be impure, but to live a holy life.(M) Therefore, anyone who rejects this instruction does not reject a human being but God, the very God who gives you his Holy Spirit.(N)

Now about your love for one another(O) we do not need to write to you,(P) for you yourselves have been taught by God(Q) to love each other.(R) 10 And in fact, you do love all of God’s family throughout Macedonia.(S) Yet we urge you, brothers and sisters, to do so more and more,(T) 11 and to make it your ambition to lead a quiet life: You should mind your own business and work with your hands,(U) just as we told you, 12 so that your daily life may win the respect of outsiders(V) and so that you will not be dependent on anybody.

Believers Who Have Died

13 Brothers and sisters, we do not want you to be uninformed(W) about those who sleep in death,(X) so that you do not grieve like the rest of mankind, who have no hope.(Y) 14 For we believe that Jesus died and rose again,(Z) and so we believe that God will bring with Jesus those who have fallen asleep in him.(AA) 15 According to the Lord’s word, we tell you that we who are still alive, who are left until the coming of the Lord,(AB) will certainly not precede those who have fallen asleep.(AC) 16 For the Lord himself will come down from heaven,(AD) with a loud command, with the voice of the archangel(AE) and with the trumpet call of God,(AF) and the dead in Christ will rise first.(AG) 17 After that, we who are still alive and are left(AH) will be caught up together with them in the clouds(AI) to meet the Lord in the air. And so we will be with the Lord(AJ) forever. 18 Therefore encourage one another(AK) with these words.

Footnotes

  1. 1 Thessalonians 4:4 Or learn to live with your own wife; or learn to acquire a wife
  2. 1 Thessalonians 4:6 The Greek word for brother or sister (adelphos) refers here to a believer, whether man or woman, as part of God’s family.