Add parallel Print Page Options

Nyama ya Nsembe za Mafano

Tsopano za chakudya choperekedwa nsembe kwa mafano: Ife tidziwa kuti tonse tili ndi chidziwitso. Komatu chidziwitso chokha chimadzitukumula, koma chikondi ndicho chimapindulitsa. Munthu amene amaganiza kuti amadziwa kanthu, ndiye kuti sakudziwa monga mmene amayenera kudziwira. Koma munthu amene amakonda Mulungu amadziwika ndi Mulunguyo.

Choncho kunena za chakudya choperekedwa nsembe kwa mafano; ife tikudziwa kuti mafano si kanthu nʼpangʼonongʼono pomwe pa dziko lapansi, ndiponso kuti palibe Mulungu wina koma mmodzi yekha. Popeza kuti ngakhale pali yotchedwa milungu, kaya ndi kumwamba kapena pa dziko lapansi (poti ilipodi milungu yambirimbiri ndi ambuye ambirimbiri), koma kwa ife pali Mulungu mmodzi yekha, Atate, zinthu zonse zinachokera mwa Iye ndipo ndife ake. Komanso pali Ambuye mmodzi Yesu Khristu kumene zinthu zonse zinachokera ndipo mwa Iye ife tili ndi moyo.

Koma saliyense amadziwa zimenezi. Alipo ena ozolowera mafano kwambiri mwakuti akadya chakudya chotere amaganiza kuti chakudyacho chinaperekedwa nsembe kwa mafano. Ndiye poti chikumbumtima chawo nʼchofowoka chimadetsedwadi. Koma chakudya sichitisendeza kufupi ndi Mulungu. Tikapanda kudya si vuto, tikadya sitisinthikanso.

Komabe samalani kuti ufulu wanu ochita zinthu usafike pokhumudwitsa ofowoka. 10 Pakuti ngati aliyense wachikumbumtima chofowoka akakuonani achidziwitsonu mukudya mʼnyumba yopembedzera mafano, kodi iyeyo sichidzamulimbitsa mtima kuti azidya chakudya choperekedwa nsembe kwa mafano? 11 Kotero kuti chifukwa cha chidziwitso chanu mʼbale wofowokayu amene chifukwa cha iye, Khristu anafa, wawonongeka chifukwa cha chidziwitso chanu. 12 Mukamachimwira abale anu motere ndikuwawonongera chikumbumtima chawo chofowokacho, mukuchimwira Khristu. 13 Nʼchifukwa chake ngati zimene ine ndimadya zichititsa mʼbale wanga kugwa mu tchimo, sindidzadyanso chakudyacho kuti mʼbaleyo ndisamuchimwitse.

Concerning Food Sacrificed to Idols

Now about food sacrificed to idols:(A) We know that “We all possess knowledge.”(B) But knowledge puffs up while love builds up. Those who think they know something(C) do not yet know as they ought to know.(D) But whoever loves God is known by God.[a](E)

So then, about eating food sacrificed to idols:(F) We know that “An idol is nothing at all in the world”(G) and that “There is no God but one.”(H) For even if there are so-called gods,(I) whether in heaven or on earth (as indeed there are many “gods” and many “lords”), yet for us there is but one God,(J) the Father,(K) from whom all things came(L) and for whom we live; and there is but one Lord,(M) Jesus Christ, through whom all things came(N) and through whom we live.

But not everyone possesses this knowledge.(O) Some people are still so accustomed to idols that when they eat sacrificial food they think of it as having been sacrificed to a god, and since their conscience is weak,(P) it is defiled. But food does not bring us near to God;(Q) we are no worse if we do not eat, and no better if we do.

Be careful, however, that the exercise of your rights does not become a stumbling block(R) to the weak.(S) 10 For if someone with a weak conscience sees you, with all your knowledge, eating in an idol’s temple, won’t that person be emboldened to eat what is sacrificed to idols?(T) 11 So this weak brother or sister, for whom Christ died, is destroyed(U) by your knowledge. 12 When you sin against them(V) in this way and wound their weak conscience, you sin against Christ.(W) 13 Therefore, if what I eat causes my brother or sister to fall into sin, I will never eat meat again, so that I will not cause them to fall.(X)

Footnotes

  1. 1 Corinthians 8:3 An early manuscript and another ancient witness think they have knowledge do not yet know as they ought to know. But whoever loves truly knows.