Add parallel Print Page Options

Mpingo ndi Atsogoleri Ake

Ndipo abale sindikanakuyankhulani ngati auzimu koma adziko lapansi, makanda chabe mwa Khristu. Ndinakupatsani mkaka osati chakudya cholimba pakuti munali musanakonzeke kuchilandira. Zoonadi, simunakonzekebe. Mukanali adziko lapansi. Pakuti pakati panu pali kaduka ndi kukangana, kodi si inu a dziko lapansi? Kodi simukuchita ngati anthu wamba? Pamene wina anena kuti, “Ine ndimatsatira Paulo,” ndipo wina akuti, “Ine ndimatsatira Apolo,” Kodi si inu akunja?

Ndiponso kodi Apolo ndi ndani? Nanga Paulo ndi ndani? Otumikira chabe, omwe kudzera mwa iwo inu munakhulupirira monga Ambuye anawagawira aliyense ntchito yake. Ine ndinadzala mbewu, Apolo anayithirira, koma Mulungu ndiye anayikulitsa. Choncho kuphatikiza iye wodzala ndi iye wothirira, onse sali kanthu, koma Mulungu yekha amene amakulitsa zinthu. Munthu wodzala ndi munthu wothirira ali ndi cholinga chimodzi, ndipo aliyense adzapatsidwa mphotho molingana ndi ntchito yake. Pakuti ife ndife antchito anzake a Mulungu; inu ndinu munda wa Mulungu, Nyumba ya Mulungu.

10 Mwachisomo chimene Mulungu wandipatsa, ine ndinayika maziko monga mmisiri waluntha, ndipo ena akumangapo. Koma aliyense ayenera kuchenjera mmene akumangira. 11 Pakuti wina sangayikenso maziko ena oposera amene anakhazikitsidwa kale, amene ndi Yesu Khristu. 12 Ngati munthu aliyense amanga pa maziko awa pogwiritsa ntchito golide, siliva, miyala yamtengowapatali, milimo yamitengo, tsekera kapena udzu, 13 ntchito yake idzaonekera pamene Tsiku la chiweruzo lidzazionetsa poyera. Tsikulo lidzafika ndi moto, ndipo motowo ndi umene udzayesa ntchito ya munthu aliyense. 14 Ngati zimene zamangidwazo sizidzagwa, adzalandira mphotho yake. 15 Ndipo ngati zidzanyeke ndi moto, sadzalandira mphotho koma iye mwini adzapulumukabe, koma monga ngati munthu amene wapulumuka mʼmoto.

16 Kodi inu simukudziwa kuti ndinu Nyumba ya Mulungu ndipo kuti Mzimu wa Mulungu amakhala mwa inu? 17 Ngati wina aliyense awononga Nyumba ya Mulunguyo, Mulungu nayenso adzamuwononga ameneyo; popeza Nyumba ya Mulungu ndi yopatulika ndipo Nyumbayo ndi inu amene.

18 Choncho musadzinyenge. Ngati wina wa inu akuganiza kuti ndi wanzeru pa mulingo wa mʼbado uno, ayenera kukhala “wopusa” kuti athe kukhala wanzeru. 19 Pakuti nzeru ya dziko lapansi ndi yopusa pamaso pa Mulungu. Monga kwalembedwera kuti, “Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo,” 20 ndiponso, “Ambuye amadziwa kuti maganizo a wanzeru ndi opandapake.” 21 Choncho, wina asanyadire anthu chabe! Zonse ndi zanu, 22 kaya Paulo kapena Apolo kapena Kefa kapena dziko lapansi, kapena moyo, kapena imfa, kapena tsopano, kapena mʼtsogolo, zonse ndi zanu, 23 ndipo inu ndinu a Khristu, ndipo Khristu ndi wa Mulungu.

The Church and Its Leaders

Brothers and sisters, I could not address you as people who live by the Spirit(A) but as people who are still worldly(B)—mere infants(C) in Christ. I gave you milk, not solid food,(D) for you were not yet ready for it.(E) Indeed, you are still not ready. You are still worldly. For since there is jealousy and quarreling(F) among you, are you not worldly? Are you not acting like mere humans? For when one says, “I follow Paul,” and another, “I follow Apollos,”(G) are you not mere human beings?

What, after all, is Apollos?(H) And what is Paul? Only servants,(I) through whom you came to believe—as the Lord has assigned to each his task. I planted the seed,(J) Apollos watered it, but God has been making it grow. So neither the one who plants nor the one who waters is anything, but only God, who makes things grow. The one who plants and the one who waters have one purpose, and they will each be rewarded according to their own labor.(K) For we are co-workers in God’s service;(L) you are God’s field,(M) God’s building.(N)

10 By the grace God has given me,(O) I laid a foundation(P) as a wise builder, and someone else is building on it. But each one should build with care. 11 For no one can lay any foundation other than the one already laid, which is Jesus Christ.(Q) 12 If anyone builds on this foundation using gold, silver, costly stones, wood, hay or straw, 13 their work will be shown for what it is,(R) because the Day(S) will bring it to light. It will be revealed with fire, and the fire will test the quality of each person’s work.(T) 14 If what has been built survives, the builder will receive a reward.(U) 15 If it is burned up, the builder will suffer loss but yet will be saved—even though only as one escaping through the flames.(V)

16 Don’t you know that you yourselves are God’s temple(W) and that God’s Spirit dwells in your midst?(X) 17 If anyone destroys God’s temple, God will destroy that person; for God’s temple is sacred, and you together are that temple.

18 Do not deceive yourselves. If any of you think you are wise(Y) by the standards of this age,(Z) you should become “fools” so that you may become wise. 19 For the wisdom of this world is foolishness(AA) in God’s sight. As it is written: “He catches the wise in their craftiness”[a];(AB) 20 and again, “The Lord knows that the thoughts of the wise are futile.”[b](AC) 21 So then, no more boasting about human leaders!(AD) All things are yours,(AE) 22 whether Paul or Apollos(AF) or Cephas[c](AG) or the world or life or death or the present or the future(AH)—all are yours, 23 and you are of Christ,(AI) and Christ is of God.

Footnotes

  1. 1 Corinthians 3:19 Job 5:13
  2. 1 Corinthians 3:20 Psalm 94:11
  3. 1 Corinthians 3:22 That is, Peter