Add parallel Print Page Options

Pamene ndinabwera kwa inu, abale, sindinabwere ndi luntha lodziwa kuyankhula kapena nzeru zapamwamba pamene ndinachitira umboni chinsinsi cha Mulungu. Pakuti ndinatsimikiza pamene ndinali ndi inu kuti ndisadziwe kanthu kena kupatula Yesu Khristu wopachikidwayo. Ndinabwera kwa inu wofowoka ndi wamantha, ndiponso wonjenjemera kwambiri. Uthenga ndi ulaliki wanga sunali wa mawu anzeru ndi onyengerera koma woonetsa mphamvu za Mzimu, kuti chikhulupiriro chanu chisatsamire pa nzeru ya anthu koma pa mphamvu za Mulungu.

Nzeru Yochokera kwa Mzimu

Komabe ife timayankhula uthenga wa nzeru kwa okhwima, koma osati ndi nzeru ya mʼbado uno kapena ya olamula a mʼbado uno, amene mphamvu yawo ikutha. Ayi, ife timayankhula za nzeru yobisika ya Mulungu, nzeru imene inabisidwa ndipo imene Mulungu anatikonzera mu ulemerero wathu isanayambe nthawi. Palibe olamulira aliyense wa mʼbado uno amene anamumvetsetsa popeza anakamumvetsetsa sakanamupachika Ambuye wa ulemerero. Komabe monga zalembedwa kuti,

“Palibe diso linaona,
    palibe khutu linamva,
palibe amene anaganizira,
    zimene Mulungu anakonzera amene amukonda”

10 koma Mulungu waululira ife mwa Mzimu wake.

Mzimu amafufuza zinthu zonse, ndi zozama za Mulungu zomwe. 11 Kodi ndani mwa anthu angadziwe maganizo a munthu wina, kupatula mzimu wa munthuyo wokhala mʼkati mwake? Chimodzimodzinso palibe amene adziwa maganizo a Mulungu kupatula Mzimu wa Mulunguyo. 12 Mzimu amene tinalandira ife si wa dziko lapansi koma Mzimu wochokera kwa Mulungu wotipatsa ife mwaulere. 13 Izi ndi zimene timayankhula osati mʼmawu wophunzitsidwa ndi nzeru za munthu koma mʼmawu wophunzitsidwa ndi Mzimu, kufotokozera zoonadi zauzimu mʼmawu auzimu. 14 Munthu wopanda Mzimu savomereza zinthu zimene zichokera kwa Mzimu wa Mulungu, popeza ndi zopusa kwa iyeyo, ndipo sangazimvetsetse chifukwa zimazindikirika mwa Mzimu. 15 Munthu wauzimu amaweruza pa zinthu zonse, koma iye mwini saweruzidwa ndi munthu aliyense. 16 Pakuti

“Ndani anadziwa malingaliro a Ambuye,
    kuti akhoza kumulangiza Iye.”

Koma tili nawo mtima wa Khristu.

And so it was with me, brothers and sisters. When I came to you, I did not come with eloquence or human wisdom(A) as I proclaimed to you the testimony about God.[a] For I resolved to know nothing while I was with you except Jesus Christ and him crucified.(B) I came to you(C) in weakness(D) with great fear and trembling.(E) My message and my preaching were not with wise and persuasive words,(F) but with a demonstration of the Spirit’s power,(G) so that your faith might not rest on human wisdom, but on God’s power.(H)

God’s Wisdom Revealed by the Spirit

We do, however, speak a message of wisdom among the mature,(I) but not the wisdom of this age(J) or of the rulers of this age, who are coming to nothing.(K) No, we declare God’s wisdom, a mystery(L) that has been hidden(M) and that God destined for our glory before time began. None of the rulers of this age(N) understood it, for if they had, they would not have crucified the Lord of glory.(O) However, as it is written:

“What no eye has seen,
    what no ear has heard,
and what no human mind has conceived”[b]
    the things God has prepared for those who love him—(P)

10 these are the things God has revealed(Q) to us by his Spirit.(R)

The Spirit searches all things, even the deep things of God. 11 For who knows a person’s thoughts(S) except their own spirit(T) within them? In the same way no one knows the thoughts of God except the Spirit of God. 12 What we have received is not the spirit(U) of the world,(V) but the Spirit who is from God, so that we may understand what God has freely given us. 13 This is what we speak, not in words taught us by human wisdom(W) but in words taught by the Spirit, explaining spiritual realities with Spirit-taught words.[c] 14 The person without the Spirit does not accept the things that come from the Spirit of God(X) but considers them foolishness,(Y) and cannot understand them because they are discerned only through the Spirit. 15 The person with the Spirit(Z) makes judgments about all things, but such a person is not subject to merely human judgments, 16 for,

“Who has known the mind of the Lord
    so as to instruct him?”[d](AA)

But we have the mind of Christ.(AB)

Footnotes

  1. 1 Corinthians 2:1 Some manuscripts proclaimed to you God’s mystery
  2. 1 Corinthians 2:9 Isaiah 64:4
  3. 1 Corinthians 2:13 Or Spirit, interpreting spiritual truths to those who are spiritual
  4. 1 Corinthians 2:16 Isaiah 40:13