Add parallel Print Page Options

Ndalama Zothandizira Akhristu a ku Yerusalemu

16 Tsopano za zopereka zothandiza anthu a Ambuye a ku Yerusalemu. Muchite zomwe ndinawuza mipingo ya ku Galatiya kuti ichite. Pa tsiku loyamba la sabata lililonse, aliyense wa inu azipatula ndalama molingana ndi zomwe wapezera. Asunge, kuti ndikabwera pasadzakhalenso msonkhamsonkha. Pamenepo, ndikadzafika, ndidzawapatsa makalata a umboni anthu amene mudzawasankhe ndi kuwatuma kuti akapereka mphatso zanu ku Yerusalemu. Ngati kutaoneka kuti nʼkoyenera kuti ndipite nawo, adzapita nane limodzi.

Paulo Afotokoza za Maulendo ake ndi Zina

Ndidzafika kwanuko nditadutsa ku Makedoniya pakuti ndikuyembekezera kudzera ku Makedoniyako. Mwina ndidzakhala nanu kanthawi kochepa kapenanso nyengo yonse yozizira, kuti mudzandithandize kupitiriza ulendo wanga kulikonse kumene ndingapite. Sindikufuna kuti ndikuoneni tsopano mongodutsa chabe, koma ndikuyembekezera kudzakhala nanu kwa kanthawi, ngati Ambuye alola. Koma ndikhala ndili ku Efeso mpaka nthawi ya Pentekosite, pakuti mwayi waukulu wapezeka woti nʼkugwira ntchito yaphindu, koma pali ambiri amene akutsutsana nane.

10 Ngati Timoteyo afike kwanuko, onetsetsani kuti pasakhale zina zomuchititsa mantha pamene ali pakati panu, pakuti iye akugwira ntchito ya Ambuye monga ine. 11 Wina aliyense asamunyoze. Muthandizeni kupitiriza ulendo wake mwamtendere kubwereranso kuli ine. Ndikumuyembekeza pamodzi ndi abale ena.

12 Tsono kunena za mʼbale wathu, Apolo, ndinamuwumiriza kwambiri kuti abwere kwa inu abale, ndipo iye sanafune kupita tsopano. Koma akadzapeza mpata wabwino adzabwera.

13 Khalani tcheru; khazikikani mʼchikhulupiriro chanu; limbani mtima; khalani amphamvu. 14 Chitani zonse mwachikondi.

15 Mukudziwa kuti a mʼbanja la Stefano ndiye anali oyamba kutembenuka mtima ku Akaya, ndipo akhala akudzipereka kutumikira oyera mtima. Choncho ndikukudandaulirani, inu abale, 16 kuti muziwamvera anthu oterewa, ndiponso aliyense wogwira nawo ntchitoyi modzipereka. 17 Ndikondwera kuti Stefano, Fortunato ndi Akayiko afika, chifukwa akhala akundithandiza pakuti inu simuli nane. 18 Pakuti anatsitsimutsa mzimu wanga ndi wanu womwe. Anthu a mtundu oterewa ngofunika kuwalemekeza.

Mawu Otsiriza

19 Mpingo wa mʼchigawo cha ku Asiya ukupereka moni. Akula ndi Prisila akuperekanso moni wachisangalalo, mwa Ambuye, ndiponso mpingo umene umakumana mʼnyumba mwawo ukupereka moni. 20 Abale onse kuno akupereka moni wawo. Patsanani moni wachikondi chenicheni.

21 Ineyo Paulo, ndikulemba ndi dzanja langa mawu awa akuti moni.

22 Ngati wina sakonda Ambuye akhale wotembereredwa. Maranatha! (Ambuye athu bwerani)!

23 Chisomo cha Ambuye Yesu chikhale ndi inu.

24 Chikondi changa chikhale ndi nonsenu mwa Khristu Yesu.

The Collection for the Lord’s People

16 Now about the collection(A) for the Lord’s people:(B) Do what I told the Galatian(C) churches to do. On the first day of every week,(D) each one of you should set aside a sum of money in keeping with your income, saving it up, so that when I come no collections will have to be made.(E) Then, when I arrive, I will give letters of introduction to the men you approve(F) and send them with your gift to Jerusalem. If it seems advisable for me to go also, they will accompany me.

Personal Requests

After I go through Macedonia, I will come to you(G)—for I will be going through Macedonia.(H) Perhaps I will stay with you for a while, or even spend the winter, so that you can help me on my journey,(I) wherever I go. For I do not want to see you now and make only a passing visit; I hope to spend some time with you, if the Lord permits.(J) But I will stay on at Ephesus(K) until Pentecost,(L) because a great door for effective work has opened to me,(M) and there are many who oppose me.

10 When Timothy(N) comes, see to it that he has nothing to fear while he is with you, for he is carrying on the work of the Lord,(O) just as I am. 11 No one, then, should treat him with contempt.(P) Send him on his way(Q) in peace(R) so that he may return to me. I am expecting him along with the brothers.

12 Now about our brother Apollos:(S) I strongly urged him to go to you with the brothers. He was quite unwilling to go now, but he will go when he has the opportunity.

13 Be on your guard; stand firm(T) in the faith; be courageous; be strong.(U) 14 Do everything in love.(V)

15 You know that the household of Stephanas(W) were the first converts(X) in Achaia,(Y) and they have devoted themselves to the service(Z) of the Lord’s people.(AA) I urge you, brothers and sisters, 16 to submit(AB) to such people and to everyone who joins in the work and labors at it. 17 I was glad when Stephanas, Fortunatus and Achaicus arrived, because they have supplied what was lacking from you.(AC) 18 For they refreshed(AD) my spirit and yours also. Such men deserve recognition.(AE)

Final Greetings

19 The churches in the province of Asia(AF) send you greetings. Aquila and Priscilla[a](AG) greet you warmly in the Lord, and so does the church that meets at their house.(AH) 20 All the brothers and sisters here send you greetings. Greet one another with a holy kiss.(AI)

21 I, Paul, write this greeting in my own hand.(AJ)

22 If anyone does not love the Lord,(AK) let that person be cursed!(AL) Come, Lord[b]!(AM)

23 The grace of the Lord Jesus be with you.(AN)

24 My love to all of you in Christ Jesus. Amen.[c]

Footnotes

  1. 1 Corinthians 16:19 Greek Prisca, a variant of Priscilla
  2. 1 Corinthians 16:22 The Greek for Come, Lord reproduces an Aramaic expression (Marana tha) used by early Christians.
  3. 1 Corinthians 16:24 Some manuscripts do not have Amen.