Add parallel Print Page Options

Chenjezo Kuchokera Mʼmbiri ya Israeli

10 Pakuti sindikufuna kuti inu mukhale osadziwa zenizeni, abale, kuti makolo athu anatsogozedwa ndi mtambo ndikuti onse anawoloka nyanja. Ndipo onse anabatizidwa mwa Mose mu mtambo ndi mʼnyanja. Onse anadya chakudya chimodzi chauzimu ndipo anamwa chakumwa chimodzi chauzimu; popeza anamwa kuchokera mʼthanthwe lomwe anayenda nalo, ndipo thanthwe limeneli linali Khristu. Ngakhale zinali choncho, Mulungu sanakondwere ndi ambiri a iwo, motero ambiri mwa iwo anafera mʼchipululu.

Tsono zinthu izi zinachitika kuti zikhale chitsanzo, kuti ife tisayike mitima yathu pa zinthu zoyipa monga anachitira makolo athuwo. Musakhale anthu opembedza mafano, monga analili ena mwa iwo. Pakuti zalembedwa kuti, “Anthuwo anakhala pansi nayamba kudya ndi kumwa. Kenaka anayimirira nayamba kuvina mwachilendo.” Tisachite chigololo monga ena mwa iwo anachitira ndipo tsiku limodzi anafapo anthu 23,000. Tisamuyese Khristu, monga ena mwa iwo anachitira ndipo anaphedwa ndi njoka. 10 Ndipo osamawiringula, monga ena mwa iwo anachitira naphedwa ndi mngelo wowononga.

11 Zinthu izi zinawachitikira kuti zikhale chitsanzo ndipo zinalembedwa kuti zikhale chenjezo kwa ife, amene tiyandikira nthawi ya kutha kwa zonse. 12 Choncho, ngati mukuganiza kuti mwayima mwamphamvu, samalani mungagwe! 13 Palibe mayesero amene mwakumana nawo oposa amene anthu ena onse anakumana nawo. Mulungu ngokhulupirika; sadzalola kuti inu muyesedwe koposa muyeso umene mutha kupirira. Koma pamene mwayesedwa, Iyenso adzakupatsani njira yopambanira mayeserowo.

Maphwando a Mafano ndi Mgonero wa Ambuye

14 Choncho abwenzi anga okondedwa, lekani kupembedza mafano. 15 Ndikuyankhula kwa a anthu anzeru zawo, nokha muweruze pa zimene ndikunenazi. 16 Pamene tidalitsa chikho cha Mgonero wa Ambuye, mothokoza Mulungu, kodi sitikugawana magazi a Khristu? Nanga buledi amene timanyemayo, kodi sitikugawana thupi la Khristu? 17 Pakuti buledi ndi mmodzi yekha, ifenso ngakhale tili ambiri, ndife thupi limodzi, popeza tonse timagawana buledi mmodzi yemweyo.

18 Taganizirani zimene amachita Aisraeli. Kodi onse amene amadya zoperekedwa nsembe, samachita nawo miyambo ya pa guwapo? 19 Kodi ndikutanthauza kuti nsembe zoperekedwa kwa mafano ndi kanthu konse, kapena kuti mafano ndi kanthu konse? 20 Ayi. Nsembe za osakhulupirira zimaperekedwa kwa ziwanda, osati kwa Mulungu, ndipo sindikufuna kuti muziyanjana ndi ziwandazo. 21 Simungamwe chikho cha Ambuye, ndi kukamweranso chikho cha ziwanda. Simungadyere pa tebulo la Ambuye ndiponso la ziwanda. 22 Kodi tikufuna kuwutsa mkwiyo wa Ambuye? Kodi ndife amphamvu kuposa Iye?

Ufulu wa Munthu Wokhulupirira

23 Mutha kunena kuti, “Zinthu zonse nʼzololedwa,” komatu si zonse zili za phindu. “Zinthu zonse nʼzololedwa,” komatu si zonse zimathandiza. 24 Munthu aliyense asafunefune zokomera iye yekha, koma zokomeranso ena.

25 Idyani nyama iliyonse imene amagulitsa pa msika, osafunsa mafunso okhudzana ndi chikumbumtima chanu. 26 Popeza kuti, “Dziko lapansi ndi la Ambuye ndi zonse za mʼmenemo ndi zake.”

27 Ngati wosakhulupirira akuyitanani kuti mukadye naye, inuyo ndi kuvomera kupitako, mukadye chilichonse chimene akakupatseni ndipo musakafunse mafunso okhudzana ndi chikumbumtima chanu. 28 Koma ngati wina akuwuzani kuti, “Izi zaperekedwa nsembe,” musadye zimenezo, pofuna kuthandiza amene wakuwuzaniyo komanso chifukwa cha chikumbumtima. 29 Ndikunena za chikumbumtima cha winayo osati chanu. Tsono mungafunse kuti, nʼchifukwa chiyani ufulu wanga ukuphwanyidwa chifukwa cha chikumbumtima cha munthu wina? 30 Ngati ndikuyamika Mulungu chifukwa cha chakudya, nanga munthu angandinyoze bwanji pa zinthu zomwe ndayamikira nazo Mulungu?

31 Nʼchifukwa chake chilichonse mungadye kapena kumwa, kapena chimene mungachite, chitani zonse ku ulemerero wa Mulungu. 32 Musakhumudwitse aliyense, kaya ndi Myuda, Mgriki, kapena mpingo wa Mulungu. 33 Mu zonse ndikuyesetsa kukondweretsa aliyense mʼnjira iliyonse. Popeza sindikufunafuna zokondweretsa ine ndekha koma zokomera ambiri kuti apulumutsidwe.

Warnings From Israel’s History

10 For I do not want you to be ignorant(A) of the fact, brothers and sisters, that our ancestors were all under the cloud(B) and that they all passed through the sea.(C) They were all baptized into(D) Moses in the cloud and in the sea. They all ate the same spiritual food(E) and drank the same spiritual drink; for they drank from the spiritual rock(F) that accompanied them, and that rock was Christ. Nevertheless, God was not pleased with most of them; their bodies were scattered in the wilderness.(G)

Now these things occurred as examples(H) to keep us from setting our hearts on evil things as they did. Do not be idolaters,(I) as some of them were; as it is written: “The people sat down to eat and drink and got up to indulge in revelry.”[a](J) We should not commit sexual immorality, as some of them did—and in one day twenty-three thousand of them died.(K) We should not test Christ,[b](L) as some of them did—and were killed by snakes.(M) 10 And do not grumble, as some of them did(N)—and were killed(O) by the destroying angel.(P)

11 These things happened to them as examples(Q) and were written down as warnings for us,(R) on whom the culmination of the ages has come.(S) 12 So, if you think you are standing firm,(T) be careful that you don’t fall! 13 No temptation[c] has overtaken you except what is common to mankind. And God is faithful;(U) he will not let you be tempted[d] beyond what you can bear.(V) But when you are tempted,[e] he will also provide a way out so that you can endure it.

Idol Feasts and the Lord’s Supper

14 Therefore, my dear friends,(W) flee from idolatry.(X) 15 I speak to sensible people; judge for yourselves what I say. 16 Is not the cup of thanksgiving for which we give thanks a participation in the blood of Christ? And is not the bread that we break(Y) a participation in the body of Christ?(Z) 17 Because there is one loaf, we, who are many, are one body,(AA) for we all share the one loaf.

18 Consider the people of Israel: Do not those who eat the sacrifices(AB) participate in the altar? 19 Do I mean then that food sacrificed to an idol is anything, or that an idol is anything?(AC) 20 No, but the sacrifices of pagans are offered to demons,(AD) not to God, and I do not want you to be participants with demons. 21 You cannot drink the cup of the Lord and the cup of demons too; you cannot have a part in both the Lord’s table and the table of demons.(AE) 22 Are we trying to arouse the Lord’s jealousy?(AF) Are we stronger than he?(AG)

The Believer’s Freedom

23 “I have the right to do anything,” you say—but not everything is beneficial.(AH) “I have the right to do anything”—but not everything is constructive. 24 No one should seek their own good, but the good of others.(AI)

25 Eat anything sold in the meat market without raising questions of conscience,(AJ) 26 for, “The earth is the Lord’s, and everything in it.”[f](AK)

27 If an unbeliever invites you to a meal and you want to go, eat whatever is put before you(AL) without raising questions of conscience. 28 But if someone says to you, “This has been offered in sacrifice,” then do not eat it, both for the sake of the one who told you and for the sake of conscience.(AM) 29 I am referring to the other person’s conscience, not yours. For why is my freedom(AN) being judged by another’s conscience? 30 If I take part in the meal with thankfulness, why am I denounced because of something I thank God for?(AO)

31 So whether you eat or drink or whatever you do, do it all for the glory of God.(AP) 32 Do not cause anyone to stumble,(AQ) whether Jews, Greeks or the church of God(AR) 33 even as I try to please everyone in every way.(AS) For I am not seeking my own good but the good of many,(AT) so that they may be saved.(AU)

Footnotes

  1. 1 Corinthians 10:7 Exodus 32:6
  2. 1 Corinthians 10:9 Some manuscripts test the Lord
  3. 1 Corinthians 10:13 The Greek for temptation and tempted can also mean testing and tested.
  4. 1 Corinthians 10:13 The Greek for temptation and tempted can also mean testing and tested.
  5. 1 Corinthians 10:13 The Greek for temptation and tempted can also mean testing and tested.
  6. 1 Corinthians 10:26 Psalm 24:1