Add parallel Print Page Options

Paulo, woyitanidwa mwachifuniro cha Mulungu kuti akhale mtumwi wa Khristu Yesu ndi mʼbale wathu Sositene.

Kupita ku mpingo wa Mulungu ku Korinto, kwa oyeretsedwa mwa Khristu Yesu ndi oyitanidwa kukhala opatulika ndiponso kwa onse amene amapemphera mʼdzina la Ambuye athu Yesu Khristu mʼdziko lonse lapansi, amene ndi Ambuye wawo ndi wathunso.

Landirani chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye athu Yesu Khristu.

Kuthokoza

Nthawi zonse ndimayamika Mulungu chifukwa cha inu chifukwa cha chisomo chake chopatsidwa kwa inu mwa Khristu Yesu. Pakuti mwa Iye mwalemekezedwa mʼnjira iliyonse, mʼkuyankhula kwanu konse ndi mʼkudziwa kwanu konse, chifukwa umboni wathu pa za Khristu unatsimikizidwa mwa inu. Choncho inu simusowa mphatso yauzimu iliyonse pamene mukudikira mofunitsitsa kuti Ambuye athu Yesu Khristu avumbulutsidwe. Adzakulimbikitsani mpaka kumapeto kuti mudzakhale wopanda mlandu pa tsiku lobwera Ambuye athu Yesu Khristu. Mulungu amene wakuyitanani inu mu chiyanjano ndi Mwana wake Yesu Khristu Ambuye athu ngokhulupirika.

Kugawikana mu Mpingo

10 Ndidandaulira inu, abale, mʼdzina la Ambuye athu Yesu Khristu kuti nonsenu muvomerezane wina ndi mnzake kuti pasakhale kugawikana pakati panu ndi kuti mukhale amodzi kwenikweni mu nzeru ndi mʼmaganizo. 11 Abale anga, ena a ku nyumba ya Kloe andidziwitsa kuti pali mkangano pakati panu. 12 Chimene ndikutanthauza ndi ichi: wina amati, “Ndimatsatira Paulo,” wina, “Ndimatsatira Apolo,” wina, “Ndimatsatira Kefa,” winanso, “Ndimatsatira Khristu.”

13 Kodi Khristu wagawikana? Kodi Paulo anapachikidwa pa mtanda chifukwa cha inu? Kodi munabatizidwa mʼdzina la Paulo? 14 Ine ndikuyamika kuti sindinabatizepo mmodzi mwa inu kupatula Krispo ndi Gayo, 15 mwakuti palibe amene anganene kuti anabatizidwa mʼdzina langa. 16 (Inde, ine ndinabatizanso a mʼbanja la Stefano, koma sindikumbukira ngati ndinabatizanso wina aliyense). 17 Pakuti Khristu sananditume ine kudzabatiza, koma kudzalalikira Uthenga Wabwino, osati ndi mawu anzeru za umunthu, kuopa kuti mtanda wa Khristu ungakhale wopanda mphamvu.

Khristu ndiye Nzeru ndi Mphamvu za Mulungu

18 Pakuti uthenga wa mtanda ndi chopusa kwa iwo amene akuwonongeka, koma kwa ife amene tikupulumutsidwa uthengawu ndi mphamvu ya Mulungu. 19 Pakuti kwalembedwa kuti,

“Ine ndidzawononga nzeru za anthu anzeru;
    luntha la anthu aluntha Ine ndidzalinyoza.”

20 Munthu wanzeru ali kuti? Munthu wozama ndi maphunziro ali kuti? Munthu wodziwa zakuya zamakono ali kuti? Kodi Mulungu sanazipusitse nzeru za dziko lapansi? 21 Tsono poti mwa nzeru za Mulungu dziko lapansi mu nzeru zake silinamudziwe Iye, Mulungu amakondweretsedwa kuti kudzera mu chopusa cha zomwe zinalalikidwa apulumutse iwo amene akhulupirira. 22 Ayuda amafuna zizindikiro zodabwitsa ndipo Agriki amafunafuna nzeru, 23 koma ife timalalikira Khristu wopachikidwa. Chitsa chokhumudwitsa kwa Ayuda ndi chopusa kwa a mitundu ina. 24 Koma kwa iwo amene Mulungu anawayitana, Ayuda ndi Agriki omwe, Khristu ndi mphamvu ya Mulungu ndi nzeru za Mulungu. 25 Pakuti za Mulungu zooneka ngati zopusa, ndi za nzeru kuposa nzeru za munthu, ndipo za Mulungu zooneka ngati zofowoka, zili ndi mphamvu kuposa mphamvu za munthu.

26 Abale taganizirani mmene munalili musanayitanidwe. Si ambiri a inu munali a nzeru, si ambiri a inu munali a mphamvu zamakopedwe. Si ambiri a inu munali obadwa pa ulemerero. 27 Koma Mulungu anasankha zinthu zopusa za dziko lapansi kuti achititse manyazi anzeru. Mulungu anasankha zinthu zofowoka za dziko lapansi kuti achititse manyazi amphamvu. 28 Anasankha zinthu zapansipansi ndi zopeputsidwa za dziko la pansi lino, zinthu zimene kulibe, kuti asukulutse zimene zilipo, 29 kuti munthu asanyade pamaso pa Mulungu. 30 Nʼchifukwa cha Iye kuti inu muli mwa Khristu Yesu, amene wakhala nzeru ya kwa Mulungu, kwa ife, kunena kuti kulungama kwathu, chiyero ndi chipulumutso. 31 Choncho poti zinalembedwa kuti, “Ngati munthu akufuna kunyadira, anyadire mwa Ambuye.”

Paul, called to be an apostle(A) of Christ Jesus by the will of God,(B) and our brother Sosthenes,(C)

To the church of God(D) in Corinth,(E) to those sanctified in Christ Jesus and called(F) to be his holy people, together with all those everywhere who call on the name(G) of our Lord Jesus Christ—their Lord and ours:

Grace and peace to you from God our Father and the Lord Jesus Christ.(H)

Thanksgiving

I always thank my God for you(I) because of his grace given you in Christ Jesus. For in him you have been enriched(J) in every way—with all kinds of speech and with all knowledge(K) God thus confirming our testimony(L) about Christ among you. Therefore you do not lack any spiritual gift(M) as you eagerly wait for our Lord Jesus Christ to be revealed.(N) He will also keep you firm to the end, so that you will be blameless(O) on the day of our Lord Jesus Christ.(P) God is faithful,(Q) who has called you(R) into fellowship with his Son, Jesus Christ our Lord.(S)

A Church Divided Over Leaders

10 I appeal to you, brothers and sisters,[a](T) in the name of our Lord Jesus Christ, that all of you agree with one another in what you say and that there be no divisions among you,(U) but that you be perfectly united(V) in mind and thought. 11 My brothers and sisters, some from Chloe’s household(W) have informed me that there are quarrels among you. 12 What I mean is this: One of you says, “I follow Paul”;(X) another, “I follow Apollos”;(Y) another, “I follow Cephas[b]”;(Z) still another, “I follow Christ.”

13 Is Christ divided? Was Paul crucified for you? Were you baptized in the name of Paul?(AA) 14 I thank God that I did not baptize any of you except Crispus(AB) and Gaius,(AC) 15 so no one can say that you were baptized in my name. 16 (Yes, I also baptized the household(AD) of Stephanas;(AE) beyond that, I don’t remember if I baptized anyone else.) 17 For Christ did not send me to baptize,(AF) but to preach the gospel—not with wisdom(AG) and eloquence, lest the cross of Christ be emptied of its power.

Christ Crucified Is God’s Power and Wisdom

18 For the message of the cross is foolishness(AH) to those who are perishing,(AI) but to us who are being saved(AJ) it is the power of God.(AK) 19 For it is written:

“I will destroy the wisdom of the wise;
    the intelligence of the intelligent I will frustrate.”[c](AL)

20 Where is the wise person?(AM) Where is the teacher of the law? Where is the philosopher of this age?(AN) Has not God made foolish(AO) the wisdom of the world? 21 For since in the wisdom of God the world(AP) through its wisdom did not know him, God was pleased through the foolishness of what was preached to save(AQ) those who believe.(AR) 22 Jews demand signs(AS) and Greeks look for wisdom, 23 but we preach Christ crucified:(AT) a stumbling block(AU) to Jews and foolishness(AV) to Gentiles, 24 but to those whom God has called,(AW) both Jews and Greeks, Christ the power of God(AX) and the wisdom of God.(AY) 25 For the foolishness(AZ) of God is wiser than human wisdom, and the weakness(BA) of God is stronger than human strength.

26 Brothers and sisters, think of what you were when you were called.(BB) Not many of you were wise(BC) by human standards; not many were influential; not many were of noble birth. 27 But God chose(BD) the foolish(BE) things of the world to shame the wise; God chose the weak things of the world to shame the strong. 28 God chose the lowly things of this world and the despised things—and the things that are not(BF)—to nullify the things that are, 29 so that no one may boast before him.(BG) 30 It is because of him that you are in Christ Jesus,(BH) who has become for us wisdom from God—that is, our righteousness,(BI) holiness(BJ) and redemption.(BK) 31 Therefore, as it is written: “Let the one who boasts boast in the Lord.”[d](BL)

Footnotes

  1. 1 Corinthians 1:10 The Greek word for brothers and sisters (adelphoi) refers here to believers, both men and women, as part of God’s family; also in verses 11 and 26; and in 2:1; 3:1; 4:6; 6:8; 7:24, 29; 10:1; 11:33; 12:1; 14:6, 20, 26, 39; 15:1, 6, 50, 58; 16:15, 20.
  2. 1 Corinthians 1:12 That is, Peter
  3. 1 Corinthians 1:19 Isaiah 29:14
  4. 1 Corinthians 1:31 Jer. 9:24