Add parallel Print Page Options

Chiweruzo pa Adani a Israeli

Ulosi

Mawu a Yehova odzudzula dziko la Hadiraki
    ndi mzinda wa Damasiko
pakuti maso a anthu ndiponso mafuko onse a Israeli
    ali pa Yehova—
ndiponso mzinda wa Hamati, umene ukuchita malire ndi dzikoli,
    komanso pa Turo ndi Sidoni, ngakhale kuti iwo ndi anzeru kwambiri.
Ndipo Turo anadzimangira linga;
    wadziwunjikira siliva ngati fumbi,
    ndi golide ngati zinyalala za mʼmisewu.
Taonani Ambuye adzamulanda chuma chakecho
    ndi kuwononga mphamvu zake mʼnyanja,
    ndipo adzapserera ndi moto.
Mzinda wa Asikeloni udzaona zimenezi, nʼkuchita mantha;
    Gaza adzanjenjemera ndi ululu,
    chimodzimodzinso Ekroni, chifukwa chiyembekezo chake chidzatheratu.
Mfumu ya ku Gaza idzaphedwa
    ndipo Asikeloni adzakhala opanda anthu.
Mu Asidodi mudzakhala mlendo,
    ndipo ndidzathetsa kunyada kwa Afilisti.
Ndidzachotsa nyama ya magazi mʼkamwa mwawo,
    chakudya choletsedwa mʼmano mwawo.
Amene atsala adzakhala anthu a Mulungu wathu,
    adzasanduka atsogoleri mu Yuda,
    ndipo Ekroni adzakhala ngati Ayebusi.
Koma Ine ndidzalondera Nyumba yanga
    ndi kuyiteteza kwa ankhondo osakaza.
Palibenso mdani amene adzagonjetse anthu anga,
    pakuti tsopano ndikuwayangʼanira.

Kubwera kwa Mfumu ya Ziyoni

Sangalala kwambiri, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni!
    Fuwula, mwana wamkazi wa Yerusalemu!
Taona, mfumu yako ikubwera kwa iwe,
    yolungama ndi yogonjetsa adani,
    yodzichepetsa ndi yokwera pa bulu,
    pa mwana wamphongo wa bulu.
10 Ndidzachotsa magaleta ankhondo ku Efereimu
    ndi akavalo ankhondo ku Yerusalemu,
    ndipo uta wankhondo udzathyoka.
Mfumuyo idzabweretsa mtendere pakati pa mitundu ya anthu.
    Ulamuliro wake udzayambira ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina,
    ndipo kuchokera ku Mtsinje (Yufurate) mpaka ku malekezero a dziko lapansi.
11 Tsono kunena za iwe, chifukwa cha magazi a pangano lako ndi Ine,
    ndidzamasula amʼndende ako, ndidzawatulutsa mʼdzenje lopanda madzi.
12 Bwererani ku malo anu otetezedwa, inu amʼndende achiyembekezo;
    ngakhale tsopano ndikulengeza kuti ndidzakubwezerani zabwino mowirikiza.
13 Ndidzakoka Yuda monga ndimakokera uta wanga,
    ndipo Efereimu ndiye muvi wake.
Ndidzadzutsa ana ako iwe Ziyoni,
    kulimbana ndi ana ako iwe Grisi,
    ndipo ndidzakusandutsa iwe lupanga la munthu wankhondo.

Kuoneka kwa Yehova

14 Pamenepo Yehova adzaonekera kwa anthu ake;
    mivi yake idzangʼanima ngati chingʼaningʼani.
Ambuye Yehova adzaliza lipenga;
    ndipo adzayenda mu mkuntho wochokera kummwera,
15     ndipo Yehova Wamphamvuzonse adzawateteza.
Iwo adzawononga
    ndipo adzagonjetsa ndi miyala ya legeni.
Adzamwa magazi ndi kubangula ngati amwa vinyo;
    magazi adzayenderera ngati a mʼmbale yowazira magazi
    pa ngodya za guwa lansembe.
16 Tsiku limenelo Yehova Mulungu wawo adzawapulumutsa
    pakuti anthu ake ali ngati nkhosa.
Adzanyezimira mʼdziko lake
    ngati miyala yokongola pa chipewa chaufumu.
17 Taonani chikoka ndi kukongola kwawo!
    Tirigu adzasangalatsa anyamata,
    ndi vinyo watsopano anamwali.