Add parallel Print Page Options

“Itana ngati ungathe, koma ndani adzakuyankhe?
    Kodi ndi kwa mngelo uti ungapezeko thandizo?
Mkwiyo umapha chitsiru,
    ndipo njiru imawononga wopusa.
Ine ndinaona chitsiru chitamera mizu,
    koma mwadzidzidzi nyumba yake inatembereredwa.
Ana ake alibe ndi chitetezo chomwe;
    amaponderezedwa mʼbwalo la milandu popanda owateteza.
Anthu anjala amamudyera zokolola zake,
    amamutengera ndi za pa minga pomwe,
    ndipo anthu akhwinthi amafunkha chuma chake.
Pakuti masautso satuluka mʼfumbi,
    ndipo kuwukira sikuchokera mʼdothi.
Komatu munthu amabadwira kuti azunzike
    monga momwe mbaliwali zimathethekera mlengalenga.

“Koma ndikanakhala ine, ndikanamudandawulira Mulungu;
    ndikanapereka mlandu wanga kwa Iye.
Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka,
    zodabwitsa zimene sizingatheke kuwerengedwa.
10 Iye amagwetsa mvula pa dziko lapansi,
    ndipo amathirira minda ya anthu.
11 Iye amakweza anthu wamba,
    ndipo iwo amene akulira amawayika pa malo otetezedwa.
12 Iyeyo amalepheretsa chiwembu cha anthu ochenjera,
    kotero kuti cholinga chawo sichipindula kanthu.
13 Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo,
    ndipo zolinga za atambwali amazithetsa msangamsanga.
14 Mdima umawagwera nthawi yamasana;
    nthawi yamasana amayenda moyambasayambasa monga nthawi ya usiku.
15 Mulungu amapulumutsa amphawi ku lupanga la mʼkamwa mwawo;
    amawapulumutsa mʼmanja mwa anthu amphamvu.
16 Choncho osauka ali ndi chiyembekezo,
    ndipo anthu opanda chilungamo amawatseka pakamwa.

17 “Wodala munthu amene Mulungu amamudzudzula;
    nʼchifukwa chake usanyoze chilango cha Wamphamvuzonse.
18 Pakuti Iye amavulaza koma amamanganso mabalawo;
    Iye amakantha munthu, komanso manja ake amachiritsa.
19 Pakuti adzakupulumutsa ku masautso nthawi ndi nthawi,
    mavuto angachuluke bwanji, sadzakukhudza ndi pangʼono pomwe.
20 Pa nthawi ya njala adzakulanditsa ku imfa,
    ndipo nthawi ya nkhondo adzakupulumutsa ku lupanga.
21 Adzakuteteza kwa anthu osinjirira,
    ndipo palibe chifukwa chochitira mantha pamene chiwonongeko chafika.
22 Uzidzaseka pa nthawi ya chiwonongeko ndi ya njala,
    ndipo palibe chifukwa chochitira mantha ndi zirombo za mʼdziko lapansi.
23 Pakuti udzachita pangano ndi miyala ya mʼmunda mwako,
    ndipo nyama zakuthengo zidzakhala nawe mwamtendere.
24 Udzadziwa kuti nyumba yako ndi malo otetezedwa;
    udzawerengera katundu wako ndipo sudzapeza kanthu kamene kasowapo.
25 Udzadziwa kuti ana ako adzakhala ambiri,
    ndipo zidzukulu zako zidzakhala ngati udzu wa mʼdziko lapansi.
26 Udzafika ku manda utakalamba,
    monga mitolo ya zokolola pa nyengo yake.

27 “Ife tafufuza zimenezi ndipo ndi zoona,
    choncho uzimvere ndi kuzitsata.”