Add parallel Print Page Options

Mawu a Yobu

Pambuyo pake Yobu anatsekula pakamwa pake nayamba kutemberera tsiku limene iyeyo anabadwa. Ndipo Yobu anati:

“Tsiku limene ine ndinabadwa litembereredwe
    ndi usiku umene ananena kuti, ‘Mwana wamwamuna wabadwa!’
Tsiku limenelo lisanduke mdima;
    Mulungu wa kumwambako asalilabadirenso;
    kuwala kusaonekenso pa tsikulo.
Mdima ndi mthunzi wa imfa zikhale pa tsiku limeneli;
    mtambo uphimbe tsikuli;
    mdima wandiweyani udetse kuwala kwake.
Usiku umenewo ukutidwe ndi mdima wandiweyani;
    usawerengedwenso pamodzi ndi masiku a chaka,
    kapena kukhala pa mwezi wina uliwonse.
Usiku umenewo usabweretse chilichonse chabwino;
    kusamvekenso nthungululu za chikondwerero.
Odziwa kutemberera masiku alitemberere tsikulo,
    iwo amene akonzekera kuwutsa Leviyatani.
Nyenyezi zake za mʼbandakucha zikhale mdima;
    tsikulo liyembekezere kucha pachabe
    ndipo lisaonenso kuwala koyamba kwa mʼbandakucha.
10 Pakuti tsiku limenelo ndiye ndinatuluka mʼmimba ya amayi anga
    ndipo ndi limene linandionetsa zovuta.

11 “Bwanji ine sindinawonongeke pamene ndinkabadwa
    ndi kufa pamene ndimatuluka mʼmimba?
12 Chifukwa chiyani panali mawondo wondilandirirapo
    ndi mawere woti andiyamwitsepo?
13 Pakuti tsopano bwenzi ndili gone mwamtendere;
    ndikanakhala nditagona tulo ndili pa mpumulo
14 pamodzi ndi mafumu ndi aphungu a dziko lapansi,
    amene anadzimangira nyumba zikuluzikulu zimene tsopano ndi mabwinja,
15 pamodzi ndi olamulira amene anali ndi golide,
    amene anadzaza nyumba zawo ndi siliva.
16 Kapena, bwanji sindinakwiriridwe pansi monga mwana wobadwa wakufa kale,
    ngati khanda limene silinaone kuwala kwa dzuwa?
17 Ku mandako anthu oyipa sakhalanso pa mavuto,
    ndipo kumeneko anthu otopa ali pa mpumulo.
18 A mʼndende kumeneko akusangalala ndi mtendere;
    sakumvanso mawu ofuwula a kapitawo wa akapolo.
19 Anthu wamba ndi anthu apamwamba ali kumeneko,
    ndipo kapolo ndi womasuka kwa mbuye wake.

20 “Chifukwa chiyani dzuwa limawalira iwo amene ali pa mavuto,
    ndipo moyo umapatsidwa kwa owawidwa mtima,
21 kwa iwo amene amalakalaka imfa imene sibwera,
    amene amayifunafuna imfayo kupambana chuma chobisika,
22 amene amakondwa ndi kusangalala
    akamalowa mʼmanda?
23 Chifuwa chiyani moyo umaperekedwa kwa munthu
    amene njira yake yabisika,
    amene Mulungu wamuzinga ponseponse?
24 Mʼmalo moti ndidye, ndimalira,
    ndi kubuwula kwanga nʼkosalekeza.
25 Chimene ndinkachiopa chandigwera;
    chimene ndinkachita nacho mantha chandichitikira.
26 Ndilibe mtendere kapena bata,
    ndilibe mpumulo, koma mavuto okhaokha.”