Add parallel Print Page Options

Kugwa kwa Babuloni

47 “Tsika, ndi kukhala pa fumbi,
    iwe namwali, Babuloni;
khala pansi wopanda mpando waufumu,
    iwe namwali, Kaldeya
pakuti sadzakutchulanso wanthete kapena woyenera
    kumugwira mosamala.
Tenga mphero ndipo upere ufa;
    chotsa nsalu yako yophimba nkhope
kwinya chovala chako mpaka ntchafu
    ndipo woloka mitsinje.
Maliseche ako adzakhala poyera
    ndipo udzachita manyazi.
Ndidzabwezera chilango
    ndipo palibe amene adzandiletse.”

Woyerayo wa Israeli ndiye Mpulumutsi wathu,
    dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.

“Khala chete, ndipo lowa mu mdima,
    iwe namwali, Kaldeya;
chifukwa sadzakutchulanso
    mfumukazi ya maufumu.
Ndinawakwiyira anthu anga,
    osawasamalanso.
Ndinawapereka manja mwako,
    ndipo iwe sunawachitire chifundo.
Iwe unachitira nkhanza
    ngakhale nkhalamba.
Iwe unati, ‘Ine ndidzakhalapo nthawi zonse
    ngati mfumukazi.’
Koma sunaganizire zinthu izi
    kapena kusinkhasinkha za mmene ziti zidzathere.

“Ndipo tsopano, tamvera, iwe wongokonda zokondweretsawe,
    amene ukukhala mosatekesekawe,
umaganiza mu mtima mwako kuti,
    ‘Ine ndi Ine, ndipo kupatula ine palibenso wina.
Sindidzakhala konse mkazi wamasiye,
    ndipo ana anga sadzamwalira.’
Koma mʼkamphindi, ndiponso tsiku limodzi,
    zinthu ziwiri izi zidzakuchitikira:
    ana ako kukufera komanso kukhala mkazi wamasiye.
Zimenezi zidzakuchitikira kwathunthu
    ngakhale ali ndi amatsenga ambiri
    ndi mawula amphamvu.
10 Iwe unkadalira kuyipa kwako
    ndipo unati, ‘Palibe amene akundiona.’
Kuchenjera ndi nzeru zako zidzakusokoneza,
    choncho ukuganiza mu mtima mwako kuti,
    ‘Ine ndine basi, ndipo kupatula ine palibenso wina.’
11 Ngozi yayikulu idzakugwera
    ndipo sudzadziwa momwe ungayipewere ndi matsenga ako.
Mavuto adzakugwera
    ndipo sudzatha kuwachotsa;
chipasupasu chimene iwe sukuchidziwa
    chidzakugwera mwadzidzidzi.

12 “Pitiriza tsono kukhala ndi matsenga ako,
    pamodzi ndi nyanga zako zochulukazo,
    wakhala ukuzigwiritsa ntchito kuyambira ubwana wako.
Mwina udzatha kupambana
    kapena kuopsezera nazo adani ako.
13 Malangizo onse amene unalandira angokutopetsa basi!
    Abwere patsogolopa anthu amene amatanthauzira za kumwamba kuti adzakupulumutseni.
Abwere amene amayangʼana nyenyezi, ndi kumalosera mwezi ndi mwezi
    zimene ziti zidzakuchitikire.
14 Ndithudi, anthuwo ali ngati phesi;
    adzapsa ndi moto.
Sangathe kudzipulumutsa okha
    ku mphamvu ya malawi a moto.
Awa si makala a moto woti wina nʼkuwotha;
    kapena moto woti wina nʼkuwukhalira pafupi.
15 Umu ndi mmene adzachitire amatsenga,
    anthu amene wakhala ukugwira nawo ntchito
    ndi kuchita nawo malonda chiyambire cha ubwana wako.
Onse adzamwazika ndi mantha,
    sipadzakhala ndi mmodzi yemwe wokupulumutsa.”