Add parallel Print Page Options

Za Kupasuka kwa Babuloni ndi Mafano Ake

46 Beli wagwada pansi, Nebo wawerama;
    nyama zonyamula katundu za nyamula milungu yawo.
Mafano awo asanduka katundu wolemera pa msana pa ngʼombe.
    Asandukadi ngati katundu pa msana pa nyama zotopa.
Nyamazo zikuwerama ndi kufuna kugwa ndi milunguyo;
    sizikutha kupulumutsa katunduyo,
    izo zomwe zikupita ku ukapolo.
Mverani Ine, Inu nyumba ya Yakobo,
    inu nonse otsala a mʼnyumba ya Israeli,
Ine ndakhala ndi kukusamalirani kuyambira mʼmimba ya amayi anu,
    ndakhala ndikukunyamulani chibadwire chanu.
Mpaka pamene mudzakalambe ndi kumera imvi
    ndidzakusamalirani ndithu.
Ndinakulengani ndipo ndidzakunyamulani,
    ndidzakusamalirani ndi kukulanditsani.

“Kodi inu mudzandifanizira ndi yani, kapena mufananitsa ndi yani?
    Kodi mudzandiyerekeza kapena kundifanizitsa ndi yani?
Anthu ena amakhuthula golide mʼzikwama zawo
    ndipo amayeza siliva pa masikelo;
amalemba ntchito mʼmisiri wosula kuti awapangire mulungu,
    kenaka iwo amagwada pansi ndikupembedza kamulunguko.
Amanyamula nʼkumayenda nayo milunguyo pa mapewa awo;
    amayikhazika pa malo pake ndipo imakhala pomwepo.
    Singathe kusuntha pamalo pakepo.
Ngakhale wina apemphere kwa milunguyo singathe kuyankha;
    kapena kumupulumutsa ku mavuto ake.

“Kumbukirani zimenezi ndipo muchite manyazi,
    Muzilingalire mu mtima, inu anthu owukira.
Kumbukirani zinthu zakale zinthu zamakedzana;
    chifukwa Ine ndine Mulungu
    ndipo palibe wina ofanana nane.
10 Ndinaneneratu zakumathero kuchokera pachiyambi pomwe.
    Kuyambira nthawi yamakedzana ndinaloseratu zoti zidzachitike.
Ndikanena zimene ndifuna kuchita ndipo zimachitikadi.
    Chilichonse chimene ndafuna ndimachichita.
11 Ndikuyitana chiwombankhanga kuchokera kummawa.
    Ndikuyitana kuchokera ku dziko lakutali munthu amene adzakwaniritsa cholinga changa.
Zimene ndanena ndidzazikwaniritsadi;
    zimene ndafuna ndidzazichitadi.
12 Ndimvereni, inu anthu owuma mtima,
    inu amene muli kutali ndi chipulumutso.
13 Ndikubweretsa pafupi tsiku la chipulumutso changa;
    sichili kutali.
    Tsikulo layandikira
ndipo sindidzachedwa kukupulumutsani
    ndi kupereka ulemerero wanga kwa Israeli.