Add parallel Print Page Options

Uthenga Wotsutsa Damasiko

17 Uthenga wonena za Damasiko:

“Taonani, mzinda wa Damasiko sudzakhalanso mzinda,
    koma udzasanduka bwinja.
Mizinda ya Aroeri idzakhala yopanda anthu
    ndipo idzakhala ya ziweto, zimene zidzagona pansi
    popanda wina woziopseza.
Ku Efereimu sikudzakhalanso linga,
    ndipo ku Damasiko sikudzakhalanso ufumu;
Otsalira a ku Siriya adzachotsedwa ulemu
    monga anthu a ku Israeli,”
            akutero Yehova Wamphamvuzonse.

“Tsiku limenelo ulemerero wa Yakobo udzazimirira;
    ndipo chuma chake chidzasanduka umphawi.
Israeli adzakhala ngati munda wa tirigu
    umene anatsiriza kukolola.
Adzakhalanso ngati munda wa mʼchigwa cha Refaimu
    anthu atatha kukunkha ngala za tirigu.
Komabe Aisraeli ochepa okha ndiwo ati adzatsale
    monga mʼmene zimatsalira zipatso ziwiri kapena zitatu pa nthambi ya pamwamba penipeni
kapena zipatso zisanu pa nthambi za mʼmunsi
    mwa mtengo wa olivi akawugwedeza,”
            akutero Yehova, Mulungu wa Israeli.

Tsiku limenelo anthu adzayangʼana Mlengi wawo
    ndipo adzatembenukira kwa Woyerayo wa Israeli.
Iwo sadzakhulupiriranso maguwa ansembe,
    ntchito ya manja awo,
ndipo sadzadaliranso mitengo ya mafano a Asera,
    ndiponso maguwa ofukizirapo lubani amene manja awo anapanga.

Tsiku limenelo mizinda yawo yamphamvu, imene anasiya chifukwa cha Aisraeli, idzakhala ngati malo osiyidwa kuti awirire ndi kumera ziyangoyango. Ndipo yonse idzakhala mabwinja.

10 Inu mwayiwalatu Mulungu Mpulumutsi wanu;
    simunakumbukire Thanthwe, linga lanu.
Choncho, ngakhale munadzala mbewu zabwino,
    ndi kuyitanitsa kunja mitengo ya mpesa,
11 nimuyembekeza kuti zikule tsiku lomwelo
    ndi kuphukira maluwa mmawa mwake,
komabe zimenezi sizidzakupindulirani
    pa tsiku la mavuto.

12 Aa, mkokomo wa anthu a mitundu yambiri,
    akusokosa ngati kukokoma kwa nyanja!
Aa, phokoso la anthu a mitundu ina,
    akusokosa ngati mkokomo wa madzi amphamvu!
13 Ngakhale ankhondo a mitundu ina akubwera ndi mkokomo ngati wa madzi ambiri,
    koma adzathawira kutali Mulungu akadzawadzudzula.
Yehova adzawapirikitsa ngati mankhusu owuluka ndi mphepo pa phiri,
    ndi ngati fumbi la kamvuluvulu asanayambe.
14 Pofika nthawi yamadzulo zoopsa zidzayamba kuchitika,
    ndipo zidzakhala zitatha pofika mmawa.
Izi ndizo zidzachitikire anthu otilanda zinthu,
    gawo la amene amatibera zinthu zathu.