Add parallel Print Page Options

10 Monga ntchentche zakufa zimayika fungo loyipa mʼmafuta onunkhira,
    choncho kupusa pangʼono kumawononganso nzeru ndi ulemu.
Mtima wa munthu wanzeru umamutsogolera bwino,
    koma mtima wa munthu wopusa umamusocheretsa.
Chitsiru ngakhale chikamayenda mu msewu,
    zochita zake ndi zopanda nzeru
    ndipo chimaonetsa aliyense kuti icho ndi chitsirudi.
Ngati wolamulira akukwiyira,
    usachoke pa ntchito yako;
    kufatsa kumakonza zolakwa zazikulu.

Pali choyipa chimene ndinachiona pansi pano,
    kulakwitsa kumene kumachokera kwa wolamulira:
Zitsiru amazipatsa ntchito zambiri zapamwamba,
    pamene anthu olemera amawapatsa ntchito zotsika.
Ndaona akapolo atakwera pa akavalo,
    pamene akalonga akuyenda pansi ngati akapolo.

Amene amakumba dzenje adzagwamo yekha;
    amene amabowola khoma adzalumidwa ndi njoka.
Amene amaphwanya miyala adzapwetekedwa ndi miyalayo;
    amene amawaza nkhuni adzapwetekedwa nazo.

10 Ngati nkhwangwa ili yobuntha
    yosanoledwa,
pamafunika mphamvu zambiri potema,
    koma luso limabweretsa chipambano.

11 Nʼkopanda phindu kudziwa kuseweretsa njoka
    ngati njokayo yakuluma kale.

12 Mawu a pakamwa pa munthu wanzeru ndi okondweretsa,
    koma chitsiru chidzawonongedwa ndi milomo yake yomwe.
13 Chitsiru chimayamba ndi mawu opusa;
    potsiriza pake zoyankhula zake ndi zamisala
14     ndipo chitsiru chimachulukitsa mawu.

Palibe amene amadziwa zimene zikubwera mʼtsogolo,
    ndani angamuwuze zomwe zidzachitika iye akadzafa?

15 Chitsiru chimatopa msanga ndi ntchito yochepa;
    ndipo sichikhala ndi mphamvu zobwererera ku mudzi.

16 Tsoka kwa iwe, iwe dziko ngati mfumu yako ikali mwana,
    ndipo atsogoleri ako amakhala pa madyerero mmamawa.
17 Wodala iwe, iwe dziko ngati mfumu yako ndi mwana wolemekezeka
    ndipo atsogoleri ako amadya pa nthawi yake,
    kuti apeze mphamvu osati kuti aledzere.

18 Ngati munthu ndi waulesi, denga lake limaloshoka;
    ngati manja ake ndi alobodo nyumba yake imadontha.

19 Phwando ndi lokondweretsa anthu,
    ndipo vinyo ndi wosangalatsa moyo,
    koma ndalama ndi yankho la chilichonse.

20 Usanyoze mfumu ngakhale mu mtima mwako,
    kapena kutukwana munthu wachuma mʼchipinda chako,
pakuti mbalame yamlengalenga itha kutenga mawu ako
    nʼkukafotokoza zomwe wanena.