Add parallel Print Page Options

96 Imbirani Yehova nyimbo yatsopano;
    Imbirani Yehova dziko lonse lapansi.
Imbirani Yehova, tamandani dzina lake;
    lalikirani chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.
Lengezani ulemerero wake pakati pa mayiko,
    ntchito zake zodabwitsa pakati pa mitundu yonse ya anthu.

Pakuti wamkulu ndi Yehova ndipo ndi woyenera kwambiri kumutamanda;
    ayenera kuopedwa kupambana milungu yonse.
Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano,
    koma Yehova analenga mayiko akumwamba.
Ulemu ndi ufumu zili pamaso pake,
    mphamvu ndi ulemerero zili mʼmalo ake opatulika.

Perekani kwa Yehova, inu mabanja a anthu a mitundu ina,
    perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake;
    bweretsani chopereka ndipo mulowe mʼmabwalo ake.
Lambirani Yehova mu ulemerero wa chiyero chake;
    njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi.

10 Nenani pakati pa mitundu ya anthu, “Yehova akulamulira.”
    Dziko lonse lakhazikika molimba, silingasunthidwe;
    Iye adzaweruza mitundu ya anthu molungama.
11 Mayiko akumwamba asangalale, dziko lapansi likondwere;
    nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo;
12     minda ikondwere pamodzi ndi chilichonse chili mʼmenemo.
Pamenepo mitengo yonse ya mʼnkhalango idzayimba ndi chimwemwe;
13     idzayimba pamaso pa Yehova,
    pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi;
adzaweruza dziko lonse mwachilungamo
    ndi mitundu ya anthu onse mʼchoonadi.