Add parallel Print Page Options

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

64 Ndimvereni Mulungu pomwe ndikunena madandawulo anga;
    tetezani moyo wanga ku chiopsezo cha mdani.
Ndibiseni ku chiwembu cha anthu oyipa,
    ku gulu laphokoso la anthu ochita zoyipa.

Iwo amanola malilime awo ngati malupanga,
    amaponya mawu awo olasa ngati mivi.
Iwo amaponya mivi yawo ali pa malo wobisala kwa munthu wosalakwa;
    amamulasa modzidzimutsa ndi mopanda mantha.

Iwo amalimbikitsana wina ndi mnzake pa chikonzero chawo choyipa,
    amayankhula zobisa misampha yawo;
    ndipo amati, “Adzayiona ndani?”
Iwo amakonzekera zosalungama ndipo amati,
    “Takonza ndondomeko yabwino kwambiri!”
    Ndithu maganizo ndi mtima wa munthu ndi zachinyengo.

Koma Mulungu adzawalasa ndi mivi;
    mwadzidzidzi adzakanthidwa.
Iye adzatembenuza milomo yawoyo kuwatsutsa
    ndi kuwasandutsa bwinja;
    onse amene adzawaona adzagwedeza mitu yawo mowanyoza.

Anthu onse adzachita mantha;
    adzalengeza ntchito za Mulungu
    ndi kulingalira mozama zomwe Iye wazichita.
10 Lolani wolungama akondwere mwa Yehova
    ndi kubisala mwa Iye,
    owongoka mtima onse atamande Iye!