Add parallel Print Page Options

Salimo la Davide.

26 Weruzeni Inu Yehova
    pakuti ndakhala moyo wosalakwa.
Ndadalira Yehova
    popanda kugwedezeka.
Patseni mayeso, Inu Yehova ndipo ndiyeseni,
    santhulani mtima wanga ndi maganizo anga;
pakuti chikondi chanu chili pamaso panga nthawi zonse,
    ndipo ndimayenda mʼchoonadi chanu nthawi zonse.
Ine sindikhala pansi pamodzi ndi anthu achinyengo,
    kapena kufunsa nzeru kwa achiphamaso.
Ndimanyansidwa ndi msonkhano wa anthu ochita zoyipa
    ndipo ndimakana kukhala pansi pamodzi ndi oyipa.
Ndimasamba mʼmanja mwanga kuonetsa kusalakwa kwanga
    ndi kupita kukatumikira pa guwa lanu la nsembe, Inu Yehova,
kulengeza mofuwula za matamando anu
    ndi kuwuza onse za ntchito zanu zodabwitsa.
Ndimakonda Nyumba imene Inu Yehova mumakhalamo,
    malo amene ulemerero wanu umapezekako.

Musachotse moyo wanga pamodzi ndi ochimwa,
    moyo wanga pamodzi ndi anthu akupha anzawo,
10 amene mʼmanja mwawo muli ndondomeko zoyipa,
    dzanja lawo lamanja ladzaza ndi ziphuphu.
11 Koma ine ndimakhala moyo wosalakwa;
    mu msonkhano wa anthu anu ndidzatamanda Yehova.

12 Ndayima pa malo wopanda zovuta
    ndipo ndidzatamanda Yehova mu msonkhano waukulu.